< Книга пророка Осии 8 >
1 В недре их, яко земля непроходима, яко орел в дому Господни: понеже преступиша завет Мой и на закон Мой нечествоваша.
“Ika lipenga pakamwa pako. Ngati chiwombankhanga, kutsutsana ndi nyumba ya Yehova chifukwa anthu aphwanya pangano langa ndiponso agalukira lamulo langa.
2 Ко Мне воззовут: Боже, познахом Тя,
Israeli akulirira kwa Ine kuti, ‘Inu Mulungu wathu, ife timakudziwani!’
3 яко Израиль отвратися благих, врага прогнаша.
Koma Israeli wakana zabwino; mdani adzamuthamangitsa.
4 Сами себе царя поставиша, а не Мною, началствоваша, и не явиша Ми: от сребра своего и от злата своего сотвориша себе кумиры, яко да потребятся.
Amalonga mafumu mosatsata kufuna kwanga. Amasankha akalonga popanda chilolezo changa. Amadzipangira mafano asiliva ndi agolide koma adzawonongeka nawo.
5 Сокруши телца твоего, Самарие, разгневася ярость Моя на ня: доколе не могут очиститися, иже во Израили?
Iwe Samariya, taya fano lako la mwana wangʼombe! Mkwiyo wanga wayakira anthuwo. Padzapita nthawi yayitali chotani asanasinthike kukhala oyera mtima?
6 И то древодель сотвори, и несть бог: зане льстяй бяше телец твой, Самарие.
Mafanowa ndi ochokera ku Israeli! Mwana wa ngʼombe uyu anapangidwa ndi munthu waluso; si Mulungu amene anamupanga. Adzaphwanyidwa nʼkukhala zidutswa, mwana wangʼombe wa ku Samariya.
7 Яко ветром истлено всеяша, и разрушение их приимет я: рукоять не имущая силы еже сотворити муку, аще же и сотворит, то чуждии поядят ю.
“Aisraeli amadzala mphepo ndipo amakolola kamvuluvulu. Tirigu alibe ngala; sadzabala chakudya. Akanabala chakudya alendo akanadya chakudyacho.
8 Поглощен бысть Израиль, ныне бысть во языцех яко сосуд непотребен,
Israeli wamezedwa, tsopano ali pakati pa anthu a mitundu ina ngati chinthu cha chabechabe.
9 понеже тии взыдоша ко Ассирианом: процвете о себе Ефрем, дары возлюби.
Pakuti iwo anapita ku Asiriya ngati mbidzi yongodziyendera pa yokha. Efereimu wadzigulitsa kwa zibwenzi zake.
10 Сего ради предадутся во языки: ныне восприиму их, и почиют мало еже помазати царя и князи.
Ngakhale wadzigulitsa pakati pa mitundu ya anthu, Ine ndidzawasonkhanitsa pamodzi. Iwo adzayamba kuzunzika pansi pa ulamuliro wankhanza wa mfumu yamphamvu.
11 Яко умножи Ефрем требища, во грехи быша ему требища возлюбленная.
“Ngakhale Efereimu anamanga maguwa ambiri a nsembe zoperekedwa chifukwa cha tchimo, maguwa amenewa akhala malo ochimwirapo.
12 Впишу ему множество, и законная его в чуждая вменишася требища возлюбленная.
Ndinawalembera zinthu zambiri za malamulo anga, koma iwo anaziyesa ngati zinthu zachilendo.
13 Темже аще и пожрут жертву и снедят мяса, Господь не приимет их: ныне помянет неправды их и отмстит грехи их: тии во Египет возвратишася и во Ассирии нечистая снедят.
Amapereka nsembe za nyama kwa Ine ndipo iwo amadya nyamayo, koma Yehova sakondwera nazo. Tsopano Iye adzakumbukira zoyipa zawo ndi kuwalanga chifukwa cha machimo awo: iwowo adzabwerera ku Igupto.
14 И забы Израиль Сотворшаго и и возгради требища, и Иуда умножи грады утверждены: но послю огнь на грады его, и потребит основания его.
Israeli wayiwala Mlengi wake ndipo wamanga nyumba zaufumu; Yuda wachulukitsa mizinda ya malinga. Koma Ine ndidzaponya moto pa mizinda yawoyo, moto umene udzatenthe malinga awo.”