< Послание к Ефесянам 5 >

1 Бывайте убо подражателе Богу, якоже чада возлюбленная,
Choncho, monga ana okondedwa, tsatirani chitsanzo cha Mulungu.
2 и ходите в любви, якоже и Христос возлюбил есть нас, и предаде Себе за ны приношение и жертву Богу в воню благоухания.
Muzikondana monga Khristu anakonda ife nadzipereka yekha chifukwa cha ife monga chopereka cha fungo lokoma ndi nsembe kwa Mulungu.
3 Блуд же и всяка нечистота и лихоимство ниже да именуется в вас, якоже подобает святым:
Koma pakati panu pasamveke nʼpangʼono pomwe zadama, kapena za mtundu wina uliwonse wa chodetsa, kapena za umbombo, chifukwa izi ndi zosayenera kwa anthu oyera a Mulungu.
4 и сквернословие, и буесловие, или кощуны, яже неподобная, но паче благодарение:
Musamatukwane, kuyankhula zopusa kapena kunena nthabwala zopanda pake, zomwe ndi zosayenera, koma mʼmalo mwake muziyamika.
5 сие бо да весте, яко всяк блудник, или нечист, или лихоимец, иже есть идолослужитель, не имать достояния в Царствии Христа и Бога.
Dziwani ichi, palibe wadama, wochita zonyansa kapena waumbombo, munthu wotero ali ngati wopembedza mafano, amenewa alibe malo mu ufumu wa Khristu ndi Mulungu.
6 Никтоже вас да льстит суетными словесы, сих бо ради грядет гнев Божий на сыны непокоривыя.
Musalole wina akunamizeni ndi mawu opanda pake, pakuti chifukwa cha zinthu ngati izi mkwiyo wa Mulungu ukubwera pa amene samvera.
7 Не бывайте убо сопричастницы сим.
Nʼchifukwa chake musamayanjane nawo anthu otere.
8 Бесте бо иногда тма, ныне же свет о Господе: якоже чада света ходите:
Pajatu inu nthawi ina munali mdima, koma tsopano ndinu kuwunika mwa Ambuye. Mukhale ngati ana akuwunika
9 плод бо духовный есть во всяцей благостыни и правде и истине:
(pakuti pamene pali kuwunika pamapezekaponso zabwino zonse, chilungamo ndi choonadi).
10 искушающе, что есть благоугодно Богови:
Inu mufufuze chimene chimakondweretsa Ambuye.
11 и не приюбщайтеся к делом неплодным тмы, паче же и обличайте.
Musayanjane nazo ntchito zosapindulitsa za mdima, koma mʼmalo mwake muzitsutse.
12 Бываемая бо отай от них, срамно есть и глаголати.
Pakuti ndi zochititsa manyazi ngakhale kutchula zomwe zimachitika mseri.
13 Вся же обличаемая от света являются, все бо являемое свет есть:
Koma kuwala kumawunikira zinthu, ndipo chilichonse chimaonekera poyera. Choncho chilichonse choonekera poyera chimasandukanso kuwala.
14 сего ради глаголет: востани, спяй, и воскресни от мертвых, и осветит тя Христос.
Nʼchifukwa chake Malemba akuti, “Dzuka, wamtulo iwe, uka kwa akufa, ndipo Khristu adzakuwalira.”
15 Блюдите убо, како опасно ходите, не якоже немудри, но якоже премудри,
Samalani makhalidwe anu, musakhale ngati opanda nzeru koma ngati anzeru.
16 искупующе время, яко дние лукави суть.
Gwiritsani ntchito mpata uliwonse, chifukwa masiku ano ndi oyipa.
17 Сего ради не бывайте несмысленни, но разумевайте, что есть воля Божия.
Choncho musakhale opusa, koma mudziwe zimene Ambuye akufuna kuti muchite.
18 И не упивайтеся вином, в немже есть блуд: но паче исполняйтеся Духом,
Musaledzere ndi vinyo, chifukwa adzawononga moyo wanu. Mʼmalo mwake, mudzazidwe ndi Mzimu Woyera.
19 глаголюще себе во псалмех и пениих и песнех духовных, воспевающе и поюще в сердцах ваших Господеви,
Muziyankhulana wina ndi mnzake mawu a Masalimo, nyimbo za Mulungu ndi nyimbo za uzimu. Muziyimbira Ambuye movomerezana ndi mitima yanu.
20 благодаряще всегда о всех о имени Господа нашего Иисуса Христа Богу и Отцу,
Muziyamika Mulungu Atate nthawi zonse chifukwa cha zonse, mʼdzina la Ambuye athu Yesu Khristu.
21 повинующеся друг другу в страсе Божии.
Gonjeranani wina ndi mnzake, kuonetsa kuopa Khristu.
22 Жены, своим мужем повинуйтеся, якоже Господу,
Inu akazi, muzigonjera amuna anu, monga mumagonjera kwa Ambuye.
23 зане муж глава есть жены, якоже и Христос глава Церкве, и Той есть Спаситель тела:
Pakuti mwamuna ndi mutu wa mkazi monga momwe Khristu ali mutu wa mpingo, thupi lake, limene Iyeyo ndi Mpulumutsi wake.
24 но якоже Церковь повинуется Христу, такожде и жены своим мужем во всем.
Tsono monga mpingo umagonjera Khristu, momwemonso akazi akuyenera kugonjera amuna awo mu zonse.
25 Мужие, любите своя жены, якоже и Христос возлюби Церковь, и Себе предаде за ню,
Inu amuna, kondani akazi anu monga momwe Khristu anakondera mpingo nadzipereka yekha mʼmalo mwa mpingowo
26 да освятит ю, очестив банею водною в глаголголе:
kuti awupatule ukhale oyera, atawuyeretsa powusambitsa ndi madzi omwe ndi mawu ake.
27 да представит ю Себе славну Церковь, не имущу скверны, или порока, или нечто от таковых, но да будет свята и непорочна.
Anachita zimenezi kuti awupereke mpingowo kwa Iye mwini, mpingo wowala ndi waulemerero, wopanda banga kapena makwinya kapena chilema chilichonse, koma oyera ndi wangwiro.
28 Тако должни суть мужие любити своя жены, яко своя телеса: любяй бо свою жену, себе самаго любит.
Momwemonso, amuna akuyenera kukonda akazi awo monga matupi awo. Iye amene akonda mkazi wake adzikondanso yekha.
29 Никтоже бо когда свою плоть возненавиде, но питает и греет ю, якоже и Господь Церковь:
Pakuti palibe amene amadana nalo thupi lake, koma amalidyetsa ndi kulisamalira bwino, monga momwe Khristu amachitira ndi mpingo wake
30 зане уди есмы Тела Его, от плоти Его и от костей Его.
pakuti ndife ziwalo za thupi lake.
31 Сего ради оставит человек отца своего и матерь, и прилепится к жене своей, и будета два в плоть едину.
“Pa chifukwa ichi, mwamuna adzasiya abambo ndi amayi ake nakaphatikana ndi mkazi wake, ndipo awiriwo adzakhala thupi limodzi.”
32 Тайна сия велика есть: аз же глаголю во Христа и во Церковь.
Ichi ndi chinsinsi chozama, koma ine ndikunena za Khristu ndi mpingo.
33 Обаче и вы, по единому кийждо свою жену сице да любит, якоже (и) себе: а жена да боится (своего) мужа.
Chomwecho, aliyense mwa inu akuyenera kukonda mkazi wake monga adzikondera iye mwini, ndipo mkazi akuyenera kulemekeza mwamuna wake.

< Послание к Ефесянам 5 >