< Второзаконие 28 >

1 И будет егда прейдете Иордан в землю, юже Господь Бог ваш дает вам, аще слухом послушаете гласа Господа Бога вашего хранити и творити вся заповеди Его, яже аз заповедаю тебе днесь, и даст тя Господь Бог твой вышше всех язык земли:
Ngati mumvera Yehova Mulungu wanu ndi kutsatira mosamalitsa malamulo ake onse amene ndikukupatsani lero lino, Yehova Mulungu wanu adzakukwezani pamwamba pa mitundu yonse ya pa dziko lapansi.
2 и приидут на тя вся благословения сия и обрящете тя. Аще слухом послушаеши гласа Господа Бога твоего,
Madalitso awa adzabwera kwa inu ndi kuyenda nanu ngati mumvera Yehova Mulungu wanu:
3 благословен ты во граде и благословен ты на селе,
Mudzadalitsika mʼmizinda yanu ndi kudalitsika mʼdzikolo.
4 благословена исчадия чрева твоего и плоды земли твоея, и стада волов твоих и паствы овец твоих,
Yehova adzadalitsa ana anu, zokolola za mʼdziko lanu, ngʼombe zanu pamodzi ndi ziweto zanu zonse.
5 благословены житницы твои и останцы твои,
Dengu lanu ndi chiwaya chanu cha buledi zidzadalitsika.
6 благословен ты внегда входити тебе и благословен ты внегда исходити тебе.
Mudzadalitsika pa kulowa kwanu ndi pa kutuluka kwanu.
7 Да предаст тебе Господь Бог враги твоя, сопротивящыяся тебе, сокрушены пред лицем твоим: путем единем изыдут на тя и седмию путьми побежат от лица твоего.
Yehova adzaonetsetsa kuti adani anu amene adzakuwukirani agonjetsedwe pamaso panu. Iwo adzabwera kwa inu kuchokera mbali imodzi koma adzakuthawani ku mbali zisanu ndi ziwiri.
8 Да послет Господь на тя благословение в хранилищах твоих и на вся, на няже возложиши руку твою на земли, юже Господь Бог твой дает тебе.
Yehova adzatumiza madalitso pa nkhokwe zanu ndi pa chilichonse chimene muchikhudza. Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani mʼdziko limene akukupatsani.
9 Да возставит тя Господь Бог твой Себе люд свят, якоже клятся отцем твоим. Аще послушаеши гласа Господа Бога твоего и ходити будеши в путех Его,
Yehova Mulungu wanu adzachititsa kuti mukhale anthu ake opatulika, monga momwe analonjezera pa malumbiro ake, ngati musunga malamulo ake ndi kuyenda mʼnjira zake.
10 и узрят тя вси языцы земнии яко имя Господа (Бога твоего) призвася на тя, и убоятся тебе,
Pamenepo anthu onse a dziko lapansi adzaona kuti mumadziwika ndi dzina la Yehova ndipo adzakuopani.
11 и умножит тя Господь Бог твой во благая во исчадиех утробы твоея и во исчадиех скотов твоих, и в плодех земли твоея, на земли твоей, юже клятся Господь отцем твоим дати тебе.
Yehova adzakupambanitsani kwambiri ndipo adzakupatsani ana ambiri, ziweto zambiri, ndi zokolola zochuluka, mʼdziko limene Yehova analumbira kwa makolo anu kuti adzakupatsani.
12 Да отверзет тебе Господь сокровище Свое благое, небо, иже дати дождь земли твоей во время свое, да благословит вся дела рук твоих: и даси взаим языком многим, ты же не одолжишися: и обладаеши ты многими языки, тобою же не возобладают.
Yehova adzatsekula kumwamba kumene amasungirako chuma chake, kutumiza mvula mʼdziko lanu pa nthawi yake ndi kudalitsa ntchito yonse ya manja anu. Mudzakongoza mitundu yambiri koma inu simudzakongola kwa aliyense.
13 Да поставит тя Господь Бог твой во главу, а не в хвост: и будеши тогда выше, и не будеши ниже, аще послушаеши заповедий Господа Бога твоего, елика аз заповедаю тебе днесь хранити и творити:
Yehova adzakuthandizani kukhala mutu osati mchira. Mukakhala ndi chidwi ndi malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani lero lino ndi kuwatsata mosamalitsa, inu mudzakhala apamwamba nthawi zonse osati apansi.
14 да не преступиши от всех словес, яже аз заповедаю тебе днесь, на десно ниже на лево, ходити вслед богов иных служити им.
Musapatukire ku dzanja lamanja kapena lamanzere pa lamulo lina lililonse limene ndikukupatsani lero lino ndi kumatsatira kapena kuyitumikira milungu ina.
15 И будет аще не послушаеши гласа Господа Бога твоего хранити и творити вся заповеди Его, елики аз заповедаю тебе днесь, и приидут на тя вся клятвы сия и постигнут тя:
Koma ngati simumvera Yehova Mulungu wanu ndi kusatsata mosamalitsa malamulo ake ndi malangizo ake onse amene ndikukupatsani lero lino, matemberero awa adzabwera pa inu ndikukugonjetsani:
16 проклят ты во граде и проклят ты на селе,
Mudzatembereredwa mu mzinda ndi kutembereredwa mʼmudzi.
17 прокляты житницы твои и останки твои,
Dengu lanu ndi chiwaya chanu cha buledi zidzatembereredwa.
18 проклята исчадия утробы твоея и плоды земли твоея, стада волов твоих и паствы овец твоих,
Zipatso za mʼmimba mwanu zidzatembereredwa, ndiponso zomera za mʼdziko lanu, ana angʼombe zanu ndi ana ankhosa zanu zidzatembereredwa.
19 проклят ты внегда входити тебе и проклят ты внегда исходити тебе.
Mudzatembereredwa pa kulowa kwanu ndi pa kutuluka kwanu.
20 Да послет тебе Господь скудость и глад и истребление на вся, на няже возложиши руку твою, елика аще сотвориши, дондеже потребит тя и дондеже погубит тя вскоре, злых ради начинаний твоих, зане оставил еси Мя.
Yehova adzakutumizirani matemberero, chisokonezo ndi minyozo pa chilichonse chimene mudzachichita mpaka mudzawonongedwa ndi kukhala bwinja mofulumira chifukwa cha zoyipa zimene mwazichita pa kumutaya Yehova.
21 Да прилепит Господь к тебе смерть, дондеже потребит тя от земли, в нюже ты входиши тамо наследити ю.
Yehova adzakugwetserani mliri wa matenda mpaka atakuwonongani mʼdziko limene mukulowa kukalitengali.
22 Да поразит тя Господь неимением и огневицею, и стужею и жжением, и убийством и ветром тлетворным и бледостию, и поженут тя, дондеже погубят тя.
Yehova adzakukanthani ndi nthenda yowondetsa, ya malungo ndi ya zotupatupa, ndi kutentha kwakukulu ndi chilala, ndi chinsikwi ndi chiwawu zimene zidzakusautsani mpaka mutawonongeka.
23 И будет небо над главою твоею медяно и земля под тобою железна.
Mitambo ya pamutu panu idzawuma ngati mkuwa ndipo sidzagwetsa mvula mpaka nthaka yanu idzawuma gwaa ngati chitsulo.
24 Да даст Господь дождь земли твоей прах, и персть с небесе снидет на тя, дондеже сокрушит тя и дондеже погубит тя.
Mʼmalo mwa mvula Yehova adzakupatsani fumbi ndi dothi ndipo lidzakugwerani kuchokera kumwamba mpaka mutawonongeka.
25 Да даст тя Господь на изсечение пред враги твоими: путем единем изыдеши к ним и седмию пути побежиши от лица их, и будеши в разсеяние во всех царствах земных,
Yehova adzalola kuti adani anu akugonjetseni. Mudzadzera njira imodzi pokalimbana ndi adani anu koma pothawa mudzabalalika mbali zisanu ndi ziwiri. Mudzakhala chinthu chochititsa mantha pakati pa maufumu onse a dziko lapansi.
26 и будут мертвецы ваши снедь птицам небесным и зверем земным, и не будет отгоняяй.
Mitembo yanu idzadyedwa ndi mbalame zamumlengalenga ndi nyama zakutchire, ndipo palibe amene adzaziyingitse.
27 Да поразит тя Господь вредом Египетским в седалищах и крастою дивиею и свербом, яко не мощи тебе исцелитися.
Yehova adzakusautsani ndi zithupsa za ku Igupto ndi zotupatupa, zipere, ndi mphere zimene simudzachiritsika nazo.
28 Поразит тя Господь неистовством и слепотою и изступлением ума,
Yehova adzakusautsani inu ndi misala, khungu ndi chisokonekero cha maganizo.
29 и будеши осязаяй в полудни, якоже осязает слепый во тме, и не исправит путий твоих: и будеши тогда обидим и расхищаемь во вся дни, и не будет помогаяй тебе.
Masanasana mudzayenda ngati muli mu mdima, kumafufuzira njira ngati wosaona. Mudzakhala olephera pa chilichonse mungachite. Tsiku ndi tsiku mudzaponderezedwa ndi kuberedwa wopanda wokupulumutsani.
30 Жену поймеши, и ин муж возимеет ю: дом созиждеши, и не поживеши в нем: виноград насадиши, и не обереши его:
Mudzachita chinkhoswe ndi mkazi, koma wina adzakulandani ndi kumukwatira. Mudzamanga nyumba koma simudzagonamo. Mudzalima munda wamphesa koma simudzadyako zipatso zake.
31 телец твой заклан пред тобою, и не снеси от него: осля твое отято от тебе, и не отдастся тебе: овцы твоя отданы (будут) врагом твоим, и не будет тебе помогаяй:
Ngʼombe yanu yamtheno idzaphedwa inu muli pomwepo koma simudzadyako. Bulu wanu adzalandidwa kwa inu mwamakani osabwera nayenso. Nkhosa zanu zidzapatsidwa kwa adani anu, ndipo palibe amene adzazipulumutsa.
32 сынове твои и дщери твоя отданы (будут) языку иному, и очи твои узрят истаевающе на сия, и не возможет рука твоя:
Ana anu aamuna ndi aakazi adzaperekedwa kwa anthu a mitundu ina ndipo inu mudzafika potopa ndi kulefuka nʼkudikirira tsiku ndi tsiku kuti mwina anawo abwerako.
33 плоды земли твоея и вся труды твоя пояст язык, егоже не веси, и будеши обидимь и сокрушаем во вся дни,
Anthu amene simukuwadziwa adzakudyerani zokolola zanu, ndipo mudzakhala mukuponderezedwa mwankhanza masiku onse.
34 и будеши изумлен, видений ради очес твоих, яже узриши.
Zimene muzidzaziona zidzakusokonezani mitu.
35 Да поразит тя Господь вредом злым на коленах и на голенех, яко не мощи исцелитися тебе от стоп ног твоих даже до верха (главы) твоея.
Yehova adzakusautsani ndi zithupsa zaululu ndi zosachiritsika za mʼmawondo ndi mʼmiyendo ndipo zidzafalikira kuchoka kuphazi mpaka kumutu.
36 Да отведет тя Господь и князи твоя, яже поставиши себе, в язык, егоже не веси ты и отцы твои, и послужиши тамо богом иным, древу и камению,
Yehova adzakuthamangitsirani, inu ndi mafumu anu amene muwayika, ku dziko losadziwika kwa inu ndi kwa makolo anu. Kumeneko mudzakapembedza milungu ina, milungu ya mitengo ndi miyala.
37 и будеши тамо в гадание и в притчу и повесть во всех языцех, в няже введет тя Господь (Бог) тамо.
Inu mudzakhala chinthu chochititsa mantha kuchisunga ndiponso chinthu chotukwanidwa ndi chonyozeka kwa anthu a mitundu yonse kumene Yehova adzakuthamangitsirani.
38 Семя много изнесеши на поле, и мало внесеши, яко поядят я прузи:
Mudzadzala mbewu zambiri ku munda koma mudzakolola pangʼono, chifukwa dzombe lidzaziwononga.
39 виноград насадиши и возделаеши, и вина не испиеши, ниже возвеселишися от него, яко пояст я червь:
Mudzadzala mpesa ndi kulimirira koma vinyo wake simudzamumwa kapena kukolola mphesazo, chifukwa mphutsi zidzadya mphesazo.
40 маслины будут тебе во всех пределех твоих, и елеем не помажешися, яко истечет маслина твоя:
Mudzakhala ndi mitengo ya olivi mʼdziko lanu lonse koma simudzagwiritsa ntchito mafuta ake, chifukwa zipatso zake zidzayoyoka.
41 сыны и дщери родиши, и не будут тебе, отидут бо в плен:
Mudzabereka ana aamuna ndi aakazi koma sadzakhala anu, chifukwa adzapita ku ukapolo.
42 вся древесная твоя и вся жита земли твоея потребит ржа:
Magulumagulu a dzombe adzawononga mitengo yanu ndi mbewu za mʼdziko lanu.
43 пришлец, иже есть у тебе, взыдет над тя выше выше, ты же низидеши низу низу:
Mlendo wokhala pakati panu adzatukuka kuposa inu, koma inuyo mudzaloweralowera pansi.
44 сей взаим даст тебе, ты же ему взаим не даси: сей будет глава, ты же будеши хвост.
Iye adzakubwereketsani, koma inu simudzatha kubwereketsa. Iye adzakhala mutu ndipo inu mudzakhala mchira.
45 И приидут на тя вся клятвы сия, и поженут тя и постигнут тя, дондеже потребят тя и дондеже погубят тя: яко не послушал еси гласа Господа Бога твоего, еже хранити заповеди Его и оправдания Его, елика заповеда тебе.
Matemberero onsewa adzabwera pa inu. Adzakulondolani ndi kukugonjetsani mpaka mutawonongeka, chifukwa simunamvere Yehova Mulungu wanu ndi kusunga malamulo ndi malangizo amene anakupatsani.
46 И будут на тебе знамения и чудеса, и в семени твоем до века,
Matemberero amenewa adzakhala chizindikiro ndi chozizwitsa kwa inu ndi zidzukulu zanu mpaka kalekale.
47 понеже не послужил еси Господеви Богу твоему с веселием и благим сердцем, множества ради всех (благих),
Pakuti inu simunatumikire Yehova Mulungu wanu pa nthawi imene zinthu zinkakuyenderani bwino,
48 и послужиши врагом твоим, яже послет Господь Бог твой на тя с гладом и жаждею, и наготою и оскудеением всех: и возложит ярем железен на выю твою, дондеже сокрушит тя.
chomwecho pa nthawi ya njala ndi ludzu, ya maliseche ndi umphawi woopsa, mudzatumikira adani amene Yehova adzakutumizirani. Iye adzayika goli lachitsulo mʼkhosi mwanu kufikira atakuwonongani.
49 И наведет Господь на тя язык издалеча от края земли аки устремление орле, язык, егоже не уразумееши глагола,
Yehova adzakutumizirani mtundu wa anthu kuchokera kutali kumapeto kwa dziko lapansi nudzachita ngati mphungu yowulukira pansi, mtundu wa anthu umene chiyankhulo chawo simudzachimva,
50 язык безстуден лицем, иже не удивится лицу старчу и юна не помилует:
mtundu wooneka wochititsa mantha, wopanda ulemu kwa okalamba kapena chisoni kwa ana.
51 и пояст плоды скотов твоих и плоды земли твоея, яко не оставит тебе пшеницы, ни вина, ни елеа, стад волов твоих и паств овец твоих, дондеже погубит тя:
Iwo adzagwira ana a ziweto zanu, natenga zokolola za mʼdziko lanu kufikira mutawonongeka. Iwo sadzakusiyirani tirigu, vinyo watsopano kapena mafuta a olivi, kapena mwana wangʼombe aliyense kapena mwana wankhosa mpaka mutasanduka bwinja.
52 и сокрушит тя во всех градех твоих, дондеже разорятся стены твоя высокия и крепкия, на нихже ты уповаеши, во всей земли твоей: и озлобит тя во всех градех твоих, яже даде тебе Господь Бог твой.
Iwo adzathira nkhondo mizinda yonse mʼdziko lanu lonse mpaka malinga anu ataliatali omwe mumadalira aja atagwa. Adzathira nkhondo mizinda yonse ya mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
53 И снеси чада утробы твоея, плоть сынов и дщерей твоих, ихже даде тебе Господь Бог твой, в тесноте твоей и в скорби твоей, еюже оскорбит тя враг твой.
Chifukwa cha zosautsa zimene mdani wanu adzabweretsa pa nthawi yokuthirani nkhondo, inu mudzadya ana anu, mnofu wa ana anu aamuna ndi aakazi amene Yehova Mulungu wanu wakupatsani.
54 Юный в вас и младый зело позавидит оком своим брату своему и жене яже на лоне его, и оставшымся чадом, яже аще останутся ему:
Ngakhale munthu woleza mtima ndi wachifundo kwambiri pakati panu sadzakhala ndi chifundo pa mʼbale wake weniweni kapena mkazi wake amene iye amamukonda kapena ana ake otsalawo,
55 яко дати единому их от плотей чад своих, ихже ял еси, понеже ничто остася ему в тесноте и скорби твоей, еюже оскорбят тя врази твои во всех градех твоих.
ndipo sadzagawirako aliyense wa iwo mnofu wa ana ake amene akudyawo. Kadzakhala kali komweko basi kamene kamutsalira chifukwa cha msautso umene mdani wanu adzagwetsa pa nthawi yothira nkhondo mizinda yanu yonse.
56 И юная в вас (жена) и млада зело, еяже не обыче нога ея ходити по земли юности ради и младости, позавидит оком своим мужу своему иже на лоне ея, и сыну и дщери своей,
Mayi woleza mtima ndi wachifundo kwambiri pakati panu, uja woti sangayerekeze kuponda pansi, adzabisira mwamuna wake amene amamukonda ndi ana ake omwe aamuna ndi aakazi
57 и блоне своей изшедшей из чресл ея, и чаду своему еже аще родит: снест бо я тайно, скудости ради всех в тесноте и скорби своей, еюже оскорбит тя враг твой во всех градех твоих.
zotsalira za uchembere zochoka mʼmimba mwake ndi ana amene wabereka. Pakuti adzafuna kuti adye zimenezi yekha mobisa pa nthawi yothiridwa nkhondo chifukwa cha masautso amene mdani wanu adzagwetsa pa inu mʼmizinda yanu.
58 Аще не послушаете творити вся словеса закона сего, написанная в книзе сей, еже боятися имене чуднаго и чуднаго сего, Господа Бога твоего,
Ngati simutsata mosamalitsa mawu onse a malamulo awa amene alembedwa mʼbuku lino, komanso ngati simuopa dzina la ulemerero ndi loopsa, dzina la Yehova Mulungu wanu,
59 и удивит Господь язвы твоя и язвы семене твоего, язвы великия и дивныя, и болезни злыя и известныя,
Yehova adzatumiza pa inu ndi zidzukulu zanu miliri yoopsa, zosautsa zowawa ndi zokhalitsa, ndi matenda aakulu ndi ovuta kuchiritsika.
60 и обратит на тя всю болезнь Египетскую злую, еяже ты боялся еси от лица их, и прилепятся к тебе:
Adzakubweretserani matenda onse a ku Igupto aja mumawaopawa ndipo adzakukanirirani.
61 и все разслабление, и всю язву ненаписанную и всю писаную в книзе закона сего наведет Господь на тя, дондеже потребит тя:
Yehova adzakubweretseraninso mtundu uliwonse wa matenda ndi zosautsa zimene sizinalembedwe mʼbuku la malamulo lino, mpaka mutawonongeka.
62 и останетеся в числе малем, вместо того егда бысте яко звезды небесныя множеством, яко не послушасте гласа Господа Бога вашего.
Inu aja munali ochuluka ngati nyenyezi zakumwamba mudzatsala ochepa chabe chifukwa simunamvere Yehova Mulungu wanu.
63 И будет, якоже возвеселися Господь о вас благотворити вам и умножити вас, тако возвеселится Господь о вас потребити вас: и возметеся от земли, в нюже вы входите тамо наследити ю,
Monga kunamukomera Yehova kukulemeretsani ndi kukuchulukitsani, momwemonso kudzamukondweretsa kukunthani ndi kukuwonongani. Inu mudzazulidwa kukuchotsani mʼdziko limene mukulowa kukalitengali.
64 и разсеет тя Господь Бог твой во вся языки, от края земли даже до края ея, и послужиши тамо богом иным, древу и камению, ихже не знал еси ты и отцы твои:
Kenaka Yehova adzakubalalitsani pakati pa anthu a mitundu yonse, kuchokera ku mapeto a dziko kufika ku mapeto ena. Kumeneko mudzapembedza milungu ina, milungu ya mitengo ndi ya miyala, imene inu eni kapena makolo anu sanayidziwepo.
65 но и во языцех онех не упокоит тя, ниже будет стояния стопе ноги твоея: и даст тебе Господь тамо сердце печальное и оскудевающая очеса и истаявающую душу:
Pakati pa mitundu ya anthu imeneyi simudzapeza mpata, popanda malo woti nʼkuyikapo phazi. Kumeneko Yehova adzakupatsani moyo wa nkhawa, maso otopa ndi chiyembekezo, ndi mtima wosakhazikika.
66 и будет живот твой висящь пред очима твоима, и убоишися во дни и в нощи, и не будеши веры яти житию твоему:
Inu mudzakhala osakhazikika mopitirira, odzazidwa ndi mantha usiku ndi usana womwe, osowa chitsimikizo cha pa moyo wanu.
67 заутра речеши: како будет вечер? И в вечер речеши: како будет утро? От страха сердца твоего, имже убоишися, и от видении очес твоих, имиже узриши:
Mmawa muzidzati, “Chikhala anali madzulo!” ndipo madzulo mudzati, “Chikhala unali mmawa!” Mudzanena zimenezi chifukwa cha mantha amene adzakhale mu mtima mwanu ndi chifukwa cha zomwe muzidzaziona.
68 и возвратит тя Господь Бог во Египет в кораблех, и на пути егоже рекох, не приложите ксему видети его: и продани будете тамо врагом вашым в рабы и в рабыни, и не будет купующаго.
Yehova adzakubwezani ku Igupto pa sitima zapamadzi paulendo umene Ine ndinati musawuyendenso. Kumeneko mudzadzitsatsa nokha kwa adani anu monga akapolo aamuna ndi aakazi, koma palibe amene adzakuguleni.

< Второзаконие 28 >