< Книга пророка Даниила 5 >

1 Валтасар царь сотвори вечерю велию вельможам своим тысящи мужем,
Tsiku lina mfumu Belisazara anakonza phwando lalikulu la akalonga ake 1,000 ndipo anamwa vinyo pamodzi ndi iwo.
2 пред тысящею же вино, и пия Валтасар рече при вкушении вина, еже принести сосуды златы и сребряны, яже изнесе Навуходоносор отец его из храма (Господа Бога), иже во Иерусалиме, и да пиют в них царь и вельможи его, и наложницы его и возлежащыя (окрест) его.
Pamene Belisazara ankamwa vinyo, analamula kuti ziwiya zagolide ndi zasiliva zimene Nebukadinezara abambo ake anakatenga mʼNyumba ya Mulungu ku Yerusalemu zikatengedwe kuti mfumu ndi akalonga ake, akazi ake ndi azikazi amweremo.
3 И принесоша сосуды златыя и сребряныя, яже изнесе (Навуходоносор царь) из храма Господа Бога, иже во Иерусалиме: и пияху ими царь и вельможи его, и наложницы его и возлежащыя (окрест) его:
Choncho anabweretsa ziwiya zagolide zimene anazitenga mʼNyumba ya Mulungu; ndipo mfumu ndi akalonga ake, akazi ake ndi azikazi ake anamweramo.
4 пияху вино и похвалиша боги златыя и сребряныя, и медяныя и железныя, и древяныя и каменныя, а Бога вечнаго не благословиша, имущаго власть духа их.
Akumwa vinyo, anatamanda milungu yagolide ndi siliva, yamkuwa, chitsulo, yamtengo ndi mwala.
5 В той час изыдоша персты руки человечи и писаху противу лампады на поваплении стены дому царева, и царь видяше персты руки пишущия.
Mwadzidzidzi zala za dzanja la munthu zinaonekera ndi kulemba pa khoma, pafupi ndi choyikapo nyale mʼnyumba yaufumu. Mfumu inapenyetsetsa dzanjalo pamene limalemba.
6 Тогда царю зрак изменися, и размышления его смущаху его, и соузы чресл его разслабляхуся, и колена его сражастася:
Nkhope yake inasandulika ndipo inachita mantha, nkhongono zii, mawondo gwedegwede.
7 и возопи царь силою, еже ввести волхвов, Халдеев, газаринов: и рече царь мудрым Вавилонским: иже прочтет писание сие и разум его возвестит мне, той в багряницу облечется, и гривна златая на выю его, и третий во царстве моем обладати начнет.
Mfumu inafuwula kuyitana owombeza, alawuli ndi amawula kuti abwere. Ndipo anawawuza anthu anzeru a ku Babuloni kuti, “Aliyense amene awerenge malembawa ndi kundiwuza tanthauzo lake adzavekedwa chovala cha pepo ndi mkanda wa golide udzavekedwa mʼkhosi mwake, ndipo adzakhala wolamulira wachitatu mu ufumuwu.”
8 И вхождаху вси мудрии ко царю и не можаху писания прочести, ни разума царю возвестити.
Pamenepo anzeru onse a mfumu anabwera, koma sanakwanitse kuwerenga malembawo kapena kumutanthauzira mfumu.
9 Царь же Валтасар возмятеся, и зрак его изменися на нем, и вельможи его смущахуся.
Choncho mfumu Belisazara anachita mantha koposa ndipo nkhope yake inapitirira kusinthika. Akalonga ake anathedwa nzeru.
10 И вниде царица в дом пирный, и рече царица: царю во веки живи: да не смущают тебе размышления твоя, и зрак твой да не изменяется:
Mfumukazi, pakumva mawu a mfumu ndi akalonga ake, analowa mʼchipinda cha phwando ndipo anati, “Mfumu mukhale ndi moyo wautali! Musavutike! Nkhope yanu isasinthike!
11 есть муж во царстве твоем, в немже дух Божий: и во дни отца твоего бодрость и смысл обретеся в нем, и царь Навуходоносор отец твой князя постави его волхвом, обаятелем, Халдеем, газарином,
Pali munthu wina mu ufumu wanu uno amene mwa iye muli mzimu wa milungu yoyera. Pa nthawi ya ulamuliro wa abambo anu iye anapezeka kuti ali ndi chidziwitso, luntha ndi nzeru zonga za milungu. Mfumu Nebukadinezara, abambo anu, Ine ndikukuwuzani anamusankha iye kukhala mkulu wa amatsenga, owombeza, alawuli ndi amawula.
12 яко дух преизюбилный (бяше) в нем, и премудрость и смысл (обретеся) в нем, сказуя сны и возвещая сокровенная и разрешая соузы, Даниил, и царь нарече имя ему Валтасар: ныне убо да призовется, и сказание его возвестит тебе.
Munthu ameneyu dzina lake ndi Danieli, koma mfumu inamutcha Belitesezara ndipo ali ndi nzeru zapadera, ndi wodziwa ndi kuzindikira zinthu, ndiponso luso lakutanthauzira maloto, kufotokozera miyambi ndi kuthetsa mavuto osautsa. Muyitaneni Danieli, ndipo adzakuwuzani chomwe mawuwa akutanthauza.”
13 Тогда Даниил введен бысть пред царя. И рече царь Даниилу: ты лиеси Даниил, от сынов пленник Иудейских, ихже приведе Навуходоносор царь отец мой?
Choncho anabwera naye Danieli pamaso pa mfumu ndipo inati kwa iye, “Kodi ndiwe Danieli, mmodzi mwa akapolo omwe abambo anga mfumu anabwera nawo kuchoka ku Yuda?
14 Слышах о тебе, яко дух Божий в тебе, и бодрость и смысл и премудрость изюбилна обретеся в тебе:
Ndamva kuti mzimu wa milungu uli mwa iwe ndi kuti uli ndi chidziwitso, luntha ndi nzeru zapadera.
15 и ныне внидоша пред мя мудрии, волсви, газарини, да писание сие прочтут и сказания его возвестят ми, и не могоша возвестити мне:
Anzeru ndi owombeza anabwera pamaso panga kuti awerenge zolembedwazi ndi kundiwuza tanthauzo lake koma sanakwanitse kundifotokozera.
16 аз же слышах о тебе, яко можеши суды сказати: ныне убо аще возможеши ппсание сие прочести и сказание его возвестити мне, в багряницу облечешися, и гривна златая на выи твоей будет, и третий во царстве моем обладати будеши.
Tsopano ndamva kuti iwe ukhoza kupereka matanthauzo ndi kuthetsa mavuto. Ngati ungawerenge zolembedwazi ndi kundiwuza tanthauzo lake, udzavekedwa chovala cha pepo ndi kuyikidwa mkanda wa golide mʼkhosi mwako, ndipo udzakhala wolamulira wachitatu mu ufumu uno.”
17 Тогда отвеща Даниил и рече пред царем: даяния: твоя с тобою да будут, и дар дому твоего иному даждь, аз же писание прочту царю и сказание его возвещу тебе.
Pamenepo Danieli anayankha mfumu kuti, “Inu musunge mphatso zanuzo kwa inu nokha ndipo mupereke mphothoyo kwa wina aliyense. Komabe ine ndi kuwerengerani malembawa mfumu; ndikukuwuzani tanthauzo lake.
18 Царю! Бог Вышний царство и величество, и честь и славу даде Навуходоносору отцу твоему,
“Inu mfumu, Mulungu Wammwambamwamba anapatsa abambo anu Nebukadinezara mphamvu ndi ukulu ndi ulemerero ndi ufumu.
19 и от величества, еже ему даде, вси людие, племена, языцы бяху трепещуще и боящеся от лица его: ихже хотяше убиваше, и ихже хотяше бияше, и ихже хотяше возвышаше, и ихже хотяше, той смиряше:
Chifukwa cha udindo waukulu umene anapatsidwanso, anthu onse ndi mitundu ndi anthu aziyankhulo zosiyanasiyana ankanjenjemera ndikumuopa iye. Amene mfumu inafuna anawaphadi; amene inafuna kuwasunga, inawasunga; amene inafuna kuwakweza, inawakweza; ndipo amene inafuna kuwatsitsa, inawatsitsa.
20 и егда вознесеся сердце его и утвердися дух его еже презорствовати, сведеся от престола царства, и слава и честь отяся от него,
Koma pamene inayamba kudzitama ndi kuwumitsa mtima wake ndi kuyamba kunyada, inachotsedwa pa mpando wake waufumu ndi kulandidwa ulemerero wake.
21 и от человек отгнася, и сердце его со зверьми отдася, и житие его со дивиими ослы, и травою аки вола питаху его, и от росы небесныя оросися тело его, дондеже уразуме, яко владеет Бог Вышний царством человеческим, и емуже хощет, даст е.
Iyo inachotsedwa pakati pa anthu ndi kupatsidwa mtima ngati wa nyama; inakhala pamodzi ndi abulu akutchire ndi kudya udzu ngati ngʼombe; ndipo thupi lake linanyowa ndi mame akumwamba, mpaka pamene anavomereza kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye wolamulira maufumu a anthu ndipo amawupereka kwa aliyense amene Iye wafuna.
22 И ты убо, сыне его Валтасаре, не смирил еси сердца твоего пред Господем: не вся ли сия ведал еси?
“Koma inu mwana wake, Belisazara, simunadzichepetse, ngakhale kuti mumadziwa zonsezi.
23 Но на Господа Бога небеснаго вознеслся еси, и сосуды храма Его принесоша пред тебе, ты же и вельможи твои, и наложницы твоя и возлежащыя (окрест) тебе, вино пиясте ими: и боги златыя и сребряныя, и медяныя и железныя, и каменныя и древяныя, иже ни видят, ни слышат, ни разумеют, похвалил еси, а Бога, у Негоже дыхание твое в руце Его, и вси путие твои, Того не прославил еси.
Mʼmalo mwake, mwadzikweza nokha kutsutsana ndi Ambuye wakumwamba. Inu mwatenga ziwiya za mʼNyumba mwake, ndipo inu ndi akalonga anu, akazi anu ndi azikazi anu mwamwera vinyo mu zimenezi. Inu munatamanda milungu yasiliva ndi golide, yamkuwa, chitsulo, mtengo ndi mwala, imene singaone kapena kumva kapena kuzindikira. Koma simunamupatse ulemu Mulungu amene asunga mʼmanja mwake moyo wanu ndi njira zanu zonse.
24 Сего ради от лица Его послани быша персты ручнии и писание сие вчиниша.
Choncho Iye watumiza dzanja limene lalemba mawu amenewa.
25 Се же есть писание вчиненое: мани, фекел, фарес.
“Mawu amene analembedwa ndi awa: MENE, MENE, TEKELI, PARASINI.
26 Се сказание глагола: мани, измери Бог царство твое и сконча е:
“Zimene mawuwa akutanthauza ndi izi:
27 фекел, поставися в мерилех и обретеся лишаемо:
Tekeli: Inu mwayesedwa pa sikelo ndipo mwapezeka kuti mukuperewera.
28 фарес, разделися царство твое и дадеся Мидом и Персом.
Parasini: Ufumu wanu wagawidwa ndi kupatsidwa kwa Amedi ndi Aperezi.”
29 И рече Валтасар: (облецыте и). И облекоша Даниила в багряницу, и гривну златую возложиша на выю его, и проповеда о нем, еже быти ему князю третиему во царстве его.
Mwa lamulo la Belisazara, Danieli anavekedwa chovala cha pepo, mkanda wagolide unayikidwa mʼkhosi mwake, ndipo analengeza kuti anali wachitatu mu ulamuliro mu ufumuwo.
30 Валтасара царя Халдейска убиша в ту нощь,
Usiku womwewo Belisazara, mfumu ya anthu a ku Babuloni, inaphedwa,
31 Дарий же Мидянин прия царство, сый шестидесяти и двою лет.
ndipo Dariyo Mmedi analanda ufumuwo ali ndi zaka 62.

< Книга пророка Даниила 5 >