< Четвертая книга Царств 1 >
1 И отступи Моав от Израиля, по умертвии Ахаавли.
Atamwalira Ahabu, Mowabu anawukira Israeli.
2 Охозиа же паде из окна, еже в горнице его в Самарии, и разболеся, и посла послы и рече к ним: идите и вопросите у Ваала сквернаго бога Аккаронска, аще жив буду от болезни моея сея? И идоша вопрошати его ради.
Ndipo Ahaziya anagwa kuchokera pa khonde la chipinda chake chammwamba ku Samariya, ndipo anavulala kwambiri. Choncho iye anatuma amithenga nawawuza kuti, “Pitani mukafunse kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni, ngati ndichire matendawa.”
3 И Ангел Господень рече ко Илии Фесвитянину, глаголя: востав, иди на сретение послом Охозии царя Самарийска и речеши к ним: или несть Бога во Израили, яко грядете вопрошати Ваала сквернаго бога во Аккароне?
Koma mngelo wa Yehova anawuza Eliya wa ku Tisibe kuti, “Nyamuka, pita ukakumane ndi amithenga a mfumu ya ku Samariya ndipo ukawafunse kuti, ‘Kodi popeza kulibe Mulungu ku Israeli, nʼchifukwa chake inu mukupita kukafunsa nzeru kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni?’
4 И сего ради сице глаголет Господь одр, на негоже возшел еси ту, не имаши слезти с него, яко ту смертию умреши, и иде Илиа и рече к ним.
Tsono Yehova akuti, ‘Iweyo sudzadzuka pa bedi wagonapo. Udzafa ndithu!’” Ndipo Eliya ananyamuka.
5 И возвратишася послы к нему, и рече к ним: что яко возвратистеся?
Amithenga aja atabwerera kwa mfumu, mfumuyo inawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani mwabwerera?”
6 И реша к нему: муж изыде в сретение нам и рече к нам: идите возвратитеся к царю пославшему вы и глаголите к нему: сице глаголет Господь: или нему Бога во Израили, яко вы грядете вопрошати Ваала сквернаго бога во Аккароне? Сего ради от одра, на негоже возшел еси, не имаши слезти с него, яко ту смертию умреши.
Iwo anayankha kuti, “Munthu wina anabwera kudzakumana nafe, ndipo anatiwuza kuti, bwererani kwa mfumu imene inakutumani ndipo mukayiwuze kuti, ‘Yehova akuti, kodi popeza kulibe Mulungu ku Israeli, nʼchifukwa chake mukupita kukafunsa nzeru kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni? Tsono sudzadzuka pa bedi wagonapo. Udzafa ndithu!’”
7 И рече к ним царь, глаголя: каков взором бяше муж той вшедый в сретение вам и глаголавый вам словеса сия?
Mfumu inafunsa amithengawo kuti, “Kodi munthu amene anabwera kudzakumana nanuyo ndi kukuwuzani zimenezi amaoneka bwanji?”
8 И реша к нему: муж космат и поясом усменным препоясан о чреслех своих. И рече царь: Илиа Фесвитянин сей есть.
Iwo anayankha kuti, “Munthuyo anavala zovala zaubweya ndi lamba wachikopa mʼchiwuno mwake.” Mfumu inati, “Munthu ameneyo ndi Eliya wa ku Tisibe.”
9 И посла к нему стареишину пятьдесятника и пятьдесят мужей его. И взыде и прииде к нему: и се, Илиа бе седя верху горы. И глагола пятьдесятник к нему и рече: человече Божии, царь зовет тя, сниди.
Pamenepo mfumu inatuma mtsogoleri wa ankhondo ndi anthu ake makumi asanu kwa Eliya. Mtsogoleriyo anapita kwa Eliya, amene anali atakhala pamwamba pa phiri, ndipo anati, “Munthu wa Mulungu, mfumu ikuti, ‘Tsikani!’”
10 И отвеща Илиа и рече к пятьдесятнику: аще есмь человек Божий аз, то да снидет огнь с небесе и снест тя и пятьдесят твоих (с тобою). И сниде огнь с небесе и снеде его и пятьдесят мужей его.
Eliya anayankha mtsogoleriyo kuti, “Ngati ndine munthu wa Mulungu, moto utsike kuchokera kumwamba, ukupsereze iwe pamodzi ndi anthu makumi asanu akowo!” Pomwepo moto unatsikadi kuchokera kumwamba ndipo unapsereza mtsogoleriyo pamodzi ndi anthu akewo.
11 И приложи царь послати к нему другаго пятьдесятника и пятьдесят (мужей) с ним. И возшед, и глагола пятьдесятник к нему и рече: человече Божий, сице глаголет царь: потщався сниди.
Zitachitika izi, mfumu inatumanso mtsogoleri wina pamodzi ndi asilikali ake makumi asanu. Mtsogoleriyo anati kwa Eliya, “Munthu wa Mulungu, zimene mfumu ikunena ndi izi, ‘Tsikani msangamsanga!’”
12 И отвеща Илиа и глагола к нему и рече: аще человек Божий аз есмь, то да снидет огнь с небесе, и да снест тя и пятьдесят (мужей) с тобою. И сниде огнь с небесе и снеде его и пятьдесят мужей его.
Eliya anayankha kuti, “Ngati ndine munthu wa Mulungu, moto utsike kuchokera kumwamba, ukupsereze iwe pamodzi ndi anthu ako makumi asanuwo!” Pomwepo moto unatsikadi kuchokera kumwamba ndipo unapsereza mtsogoleriyo pamodzi ndi anthu akewo.
13 И приложи царь еще послати стареишину, пятьдесятника третияго, и пятьдесят мужей с ним. И прииде к нему пятьдесятник третий, и поклонися на колена своя пред Илиею, и моли его, и глагола к нему и рече: человече Божий, пощади душу мою и душу раб твоих сих пятьдесят пред очима твоима:
Ndipo mfumu inatumanso mtsogoleri wachitatu pamodzi ndi asilikali ake makumi asanu. Mtsogoleri wachitatuyu anakwera pa phiripo ndi kugwada pamaso pa Eliya. Iye anayankhula mopemba kuti, “Munthu wa Mulungu, chonde musandiwononge ineyo pamodzi ndi atumiki makumi asanu anuwa!
14 се, сниде огнь с небесе и пояде два пятьдесятника первыя с пятиюдесятми их: и ныне да пощадится душа рабов твоих пред очима твоима.
Taonani, moto unatsika kuchokera kumwamba ndi kupsereza atsogoleri awiri pamodzi ndi anthu awo onse. Koma tsopano musawononge moyo wanga!”
15 И глагола Ангел Господень ко Илии и рече: сниди с ним, не убойся от лица их. И воста Илиа и сниде с ним к царю,
Mngelo wa Yehova anati kwa Eliya, “Pita naye, usamuope.” Choncho Eliya ananyamuka natsika naye limodzi kupita kwa mfumu.
16 и глагола к нему и рече: сице глаголет Господь: что яко послал еси послы вопрошати Ваала сквернаго бога во Аккароне, аки бы не был Бог во Израиле, еже вопросити от Него словесе? Сего ради от одра, наньже возшел еси ту, не имаши слезти с него яко смертию умреши.
Eliya anawuza mfumu kuti, “Yehova akuti, ‘Chifukwa chiyani munatumiza amithenga kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni, kukafunsa ngati muti muchire? Kodi mu Israeli mulibe Mulungu woti nʼkukuyankhani funso lanu? Choncho, popeza mwachita izi, simudzadzuka pamene mwagonapo; mudzafa ndithu.’”
17 И умре по глаголу Господню, егоже глаголгола Илиа. И царствова Иорам брат Охозиин вместо его, понеже не име сына Охозиа, в лето второе Иорама сына Иосафата царя Иудина.
Motero Ahaziya anafadi, monga mwa mawu a Yehova amene Eliya anayankhula. Tsono popeza Ahaziya analibe mwana, Yoramu analowa ufumu mʼmalo mwake mʼchaka chachiwiri cha Yehoramu mwana wa Yehosafati mfumu ya ku Yuda.
18 И прочая словес Охозииных, елика сотвори, не се ли, сия писана в книгах словес дний царей Израилевых?
Ntchito zina zonse zimene Ahaziya anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Israeli?