< Mapisarema 111 >
1 Rumbidzai Jehovha. Ndicharumbidza Jehovha nomwoyo wangu wose, padare ravakarurama nepagungano.
Tamandani Yehova. Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.
2 Mabasa aJehovha makuru; anorangarirwa navose vanofara maari.
Ntchito za Yehova nʼzazikulu; onse amene amakondwera nazo amazilingalira.
3 Mabasa ake ndeokukudzwa noumambo, uye kururama kwake kunogara nokusingaperi.
Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
4 Akaita kuti zvishamiso zvake zvirangarirwe; Jehovha ane nyasha nengoni.
Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike; Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.
5 Anopa zvokudya kuna avo vanomutya; anorangarira sungano yake nokusingaperi.
Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye; amakumbukira pangano lake kwamuyaya.
6 Akaratidza vanhu vake simba ramabasa ake, achivapa nyika dzedzimwe ndudzi.
Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake, kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.
7 Mabasa amaoko ake akatendeka uye akarurama, mitemo yake yose yakavimbika.
Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama; malangizo ake onse ndi odalirika.
8 Yakasimba kusvika nokusingaperi-peri, yakaitwa mukutendeka nokururama.
Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi, ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.
9 Akapa dzikinuro kuvanhu vake; akasimbisa sungano yake nokusingaperi, zita rake idzvene uye rinotyisa.
Iyeyo amawombola anthu ake; anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya dzina lake ndi loyera ndi loopsa.
10 Kutya Jehovha ndiwo mavambo enjere; vose vanotevera mitemo yake vanonzwisisa. Kurumbidzwa ndokwake nokusingaperi.
Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru; onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu. Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.