< Књига пророка Захарије 9 >
1 Бреме речи Господње земљи Адраху и Дамаску, где ће починути, јер је Господње око на људима и на свим племенима Израиљевим.
Mawu a Yehova odzudzula dziko la Hadiraki ndi mzinda wa Damasiko pakuti maso a anthu ndiponso mafuko onse a Israeli ali pa Yehova—
2 И Емат ће захватити, и Тир и Сидон, ако и јесу веома мудри,
ndiponso mzinda wa Hamati, umene ukuchita malire ndi dzikoli, komanso pa Turo ndi Sidoni, ngakhale kuti iwo ndi anzeru kwambiri.
3 И Тир сагради себи град, и сабра сребра као праха, и злата као кала по путу.
Ndipo Turo anadzimangira linga; wadziwunjikira siliva ngati fumbi, ndi golide ngati zinyalala za mʼmisewu.
4 Гле, Господ ће га отерати и врћи ће у море силу његову, и он ће огњем изгорети.
Taonani Ambuye adzamulanda chuma chakecho ndi kuwononga mphamvu zake mʼnyanja, ndipo adzapserera ndi moto.
5 Аскалон ће видети и уплашиће се, и Газа ће се врло узмучити, и Акарон, што га осрамоти надање његово, и погинуће цар у Гази; и Аскалон се неће населити.
Mzinda wa Asikeloni udzaona zimenezi, nʼkuchita mantha; Gaza adzanjenjemera ndi ululu, chimodzimodzinso Ekroni, chifukwa chiyembekezo chake chidzatheratu. Mfumu ya ku Gaza idzaphedwa ndipo Asikeloni adzakhala opanda anthu.
6 И у Азоту ће седети туђин, и понос ћу филистејски затрти.
Mu Asidodi mudzakhala mlendo, ndipo ndidzathetsa kunyada kwa Afilisti.
7 И уклонићу крв њихову од уста њихових, и гадове њихове из зуба њихових, и ко остане биће и он Бога нашег и биће као поглавар у Јуди, а Акарон као Јевусејац.
Ndidzachotsa nyama ya magazi mʼkamwa mwawo, chakudya choletsedwa mʼmano mwawo. Amene atsala adzakhala anthu a Mulungu wathu, adzasanduka atsogoleri mu Yuda, ndipo Ekroni adzakhala ngati Ayebusi.
8 И поставићу логор код дома свог супрот војсци, супрот онима који одлазе и долазе, и настојник неће више пролазити кроз њих, јер сада погледах својим очима.
Koma Ine ndidzalondera Nyumba yanga ndi kuyiteteza kwa ankhondo osakaza. Palibenso mdani amene adzagonjetse anthu anga, pakuti tsopano ndikuwayangʼanira.
9 Радуј се много, кћери сионска, подвикуј, кћери јерусалимска; ево, Цар твој иде к теби, праведан је и спасава, кротак и јаше на магарцу, и на магарету, младету магаричином.
Sangalala kwambiri, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni! Fuwula, mwana wamkazi wa Yerusalemu! Taona, mfumu yako ikubwera kwa iwe, yolungama ndi yogonjetsa adani, yodzichepetsa ndi yokwera pa bulu, pa mwana wamphongo wa bulu.
10 Јер ћу истребити из Јефрема кола и из Јерусалима коње; и истребиће се лук убојити; и Он ће казивати мир народима, и власт ће му бити од мора до мора и од реке до крајева земаљских.
Ndidzachotsa magaleta ankhondo ku Efereimu ndi akavalo ankhondo ku Yerusalemu, ndipo uta wankhondo udzathyoka. Mfumuyo idzabweretsa mtendere pakati pa mitundu ya anthu. Ulamuliro wake udzayambira ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina, ndipo kuchokera ku Mtsinje (Yufurate) mpaka ku malekezero a dziko lapansi.
11 А ти, за крв завета твог пустих сужње твоје из јаме, где нема воде.
Tsono kunena za iwe, chifukwa cha magazi a pangano lako ndi Ine, ndidzamasula amʼndende ako, ndidzawatulutsa mʼdzenje lopanda madzi.
12 Вратите се ка граду, сужњи, који се надате, још ти и данас јављам да ћу ти платити двојином.
Bwererani ku malo anu otetezedwa, inu amʼndende achiyembekezo; ngakhale tsopano ndikulengeza kuti ndidzakubwezerani zabwino mowirikiza.
13 Јер запех себи Јуду као лук, и напуних Јефрема, и подигох синове твоје, Сионе, на синове твоје, Јаване, и учиних те да си као мач јуначки.
Ndidzakoka Yuda monga ndimakokera uta wanga, ndipo Efereimu ndiye muvi wake. Ndidzadzutsa ana ako iwe Ziyoni, kulimbana ndi ana ako iwe Grisi, ndipo ndidzakusandutsa iwe lupanga la munthu wankhondo.
14 И Господ ће се показати над њима, и стрела ће Његова изаћи као муња, и Господ ће Господ затрубити у трубу и поћи ће с вихорима јужним.
Pamenepo Yehova adzaonekera kwa anthu ake; mivi yake idzangʼanima ngati chingʼaningʼani. Ambuye Yehova adzaliza lipenga; ndipo adzayenda mu mkuntho wochokera kummwera,
15 Господ над војскама заклањаће их, и они ће јести погазивши из праће, и пиће подвикујући као од вина, и биће пуни као чаша, као углови од олтара.
ndipo Yehova Wamphamvuzonse adzawateteza. Iwo adzawononga ndipo adzagonjetsa ndi miyala ya legeni. Adzamwa magazi ndi kubangula ngati amwa vinyo; magazi adzayenderera ngati a mʼmbale yowazira magazi pa ngodya za guwa lansembe.
16 И Господ Бог њихов избавиће их у тај дан као стадо свог народа, јер ће се камење у венцу подигнути у земљи његовој.
Tsiku limenelo Yehova Mulungu wawo adzawapulumutsa pakuti anthu ake ali ngati nkhosa. Adzanyezimira mʼdziko lake ngati miyala yokongola pa chipewa chaufumu.
17 Јер колико ће бити добро његово и колика лепота његова! Од жита ће расти момци, а од слатког вина девојке.
Taonani chikoka ndi kukongola kwawo! Tirigu adzasangalatsa anyamata, ndi vinyo watsopano anamwali.