< Псалми 95 >

1 Ходите, запевајмо Господу, покликнимо Богу, граду спасења свог!
Bwerani, tiyeni timuyimbire Yehova mwachimwemwe, tiyeni tifuwule kwa Thanthwe la chipulumutso chathu
2 Изађимо пред лице Његово с хвалом, у песмама покликнимо Му!
Tiyeni tibwere pamaso pake ndi chiyamiko ndipo mupembedzeni Iyeyo ndi zida zoyimbira ndi nyimbo.
3 Јер је Господ велик Бог и велик Цар над свим боговима.
Pakuti Yehova ndi Mulungu wamkulu, mfumu yayikulu pamwamba pa milungu yonse.
4 У Његовој су руци дубине земаљске, и висине горске Његове су.
Mʼmanja mwake muli maziko ozama a dziko lapansi, ndipo msonga za mapiri ndi zake.
5 Његово је море и Он га је створио, и сухоту руке су Његове начиниле.
Nyanja ndi yake, pakuti anayilenga ndi Iye, ndipo manja ake anawumba mtunda wowuma.
6 Ходите, поклонимо се, припаднимо, клекнимо пред Господом, Творцем својим.
Bwerani, tiyeni tiwerame pomulambira, tiyeni tigwade pamaso pa Yehova Mlengi wathu;
7 Јер је Он Бог наш, и ми народ паше Његове и овце руке Његове. Сад кад бисте послушали глас Његов:
pakuti Iye ndiye Mulungu wathu ndipo ife ndife anthu a pabusa pake, ndi nkhosa za mʼdzanja lake. Lero ngati inu mumva mawu ake,
8 "Немојте да вам одрвени срце ваше као у Мериви, као у дан кушања у пустињи,
musawumitse mitima yanu monga momwe munachitira pa Meriba, monga munachitira tsiku lija pa Masa mʼchipululu.
9 Где ме кушаше оци ваши, испиташе и видеше дело моје.
Kumene makolo anu anandiyesa ndi kundiputa, ngakhale anaona zimene Ine ndinazichita.
10 Четрдесет година срдих се на род онај, и рекох: Ови људи тумарају срцем, и не знају путеве моје;
Kwa zaka makumi anayi ndinali wokwiya ndi mʼbado umenewo; ndipo ndinati, “Iwo ndi anthu amene mitima yawo imasochera ndipo sanadziwe njira zanga.”
11 И зато се заклех у гневу свом да неће ући у мир мој."
Choncho ndili chikwiyire, ndinalumbira kuti, “Iwowa sadzalowa ku malo anga a mpumulo.”

< Псалми 95 >