< Псалми 88 >
1 Господе Боже, Спаситељу мој, дању вичем и ноћу пред Тобом.
Salimo la ana a Kora. Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a nyimbo yoti: “Pa Matenda ndi pa Mazunzo.” Ndakatulo ya Hemani, wa banja la Ezara. Inu Yehova, Mulungu amene mumandipulumutsa, usana ndi usiku ndimalira pamaso panu.
2 Нек изађе преда Те молитва моја, пригни ухо своје к јауку мом;
Pemphero langa lifike pamaso panu; tcherani khutu lanu kuti mumve kulira kwanga.
3 Јер је душа моја пуна јада, и живот се мој примаче паклу. (Sheol )
Pakuti ndili ndi mavuto ambiri ndipo moyo wanga ukuyandikira ku manda. (Sheol )
4 Изједначих се с онима који у гроб одлазе, постадох као човек без силе,
Ndikuwerengedwa pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje; ndine munthu wopanda mphamvu.
5 Као међу мртве бачен, као убијени, који леже у гробу, којих се више не сећаш, и који су од руке Твоје далеко.
Ndayikidwa pambali pamodzi ndi anthu akufa, monga ophedwa amene agona mʼmanda, amene Inu simuwakumbukiranso, amene achotsedwa pa chisamaliro chanu.
6 Метнуо си ме у јаму најдоњу, у таму, у бездану.
Mwandiyika pansi pa dzenje penipeni, mʼmalo akuya a mdima waukulu.
7 Отежа ми гнев Твој, и свима валима својим удараш ме.
Ukali wanu ukundipsinja kwambiri, mwandiopseza kwambiri ndi mafunde anu onse. (Sela)
8 Удаљио си од мене познанике моје, њима си ме омразио; затворен сам, и не могу изаћи.
Mwandichotsa pakati pa abwenzi anga enieni ndipo mwachititsa kuti ndikhale chonyansa kwa iwo. Ndatsekerezedwa ndipo sindingathe kuthawa;
9 Око моје усахну од јада, вичем Те, Господе, сав дан, пружам к Теби руке своје.
maso anga ada ndi chisoni. Ndimayitana Inu Yehova tsiku lililonse; ndimakweza manja anga kwa Inu.
10 Еда ли ћеш на мртвима чинити чудеса? Или ће мртви устати и Тебе славити?
Kodi mumaonetsa zozizwitsa zanu kwa anthu akufa? Kodi iwo amene afa amaukanso ndi kutamanda Inu? (Sela)
11 Еда ли ће се у гробу приповедати милост Твоја, и истина Твоја у труљењу?
Kodi chikondi chanu chimalalikidwa mʼmanda, za kukhulupirika kwanu ku malo a chiwonongeko?
12 Еда ли ће у тами познати чудеса Твоја, и правду Твоју где се све заборавља?
Kodi zozizwitsa zanu zimadziwika ku malo a mdima, kapena ntchito zanu zolungama ku dziko la anthu oyiwalika?
13 Али ја, Господе, к Теби вичем, и јутром молитва моја срета Те.
Inu Yehova, Ine ndimalirira thandizo; mmawa mapemphero anga amafika pamaso panu.
14 Зашто, Господе, одбацујеш душу моју, и одвраћаш лице своје од мене?
Inu Yehova nʼchifukwa chiyani mukundikana ndi kundibisira nkhope yanu?
15 Мучим се и издишем од удараца, подносим страхоте Твоје, без надања сам.
Kuyambira ubwana wanga ndakhala ndikuzunzika pafupi kufa; ndakhala ndikuchita mantha ndipo ndine wothedwa nzeru.
16 Гнев Твој стиже ме, страхоте Твоје раздиру ме.
Ukali wanu wandimiza; zoopsa zanu zandiwononga.
17 Оптечу ме сваки дан као вода, стежу ме одсвуда.
Tsiku lonse zimandizungulira ngati chigumula; zandimiza kwathunthu.
18 Удаљио си од мене друга и пријатеља; познаници моји сакрили су се у мрак.
Inu mwatenga anzanga ndi okondedwa anga kuwachotsa pamaso panga; mdima ndiye bwenzi langa lenileni.