< Псалми 65 >
1 У Теби је уздање, Боже, Теби припада хвала на Сиону, и Теби се извршују завети.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Nyimbo. Matamando akudikira Inu Mulungu mu Ziyoni; kwa inu malumbiro athu adzakwaniritsidwa.
2 Ти слушаш молитву; к Теби долази свако тело.
Inu amene mumamva pemphero, kwa inu anthu onse adzafika.
3 Безакоња ме притискају, Ти ћеш очистити грехе наше.
Pamene tinathedwa nzeru ndi machimo, Inu munakhululukira mphulupulu zathu.
4 Благо ономе кога изабираш и примаш, да живи у двору Твом! Наситићемо се добром дома Твог, светињом цркве Твоје.
Odala iwo amene inu muwasankha ndi kuwabweretsa pafupi kukhala mʼmabwalo anu! Ife tadzazidwa ndi zinthu zabwino za mʼNyumba mwanu, za mʼNyumba yanu yoyera.
5 Дивно нам одговараш по правди својој, Боже, Спаситељу наш, узданицо свих крајева земаљских, и народа преко мора далеко.
Mumatiyankha ife ndi ntchito zodabwitsa zachilungamo, Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, chiyembekezo cha mathero onse a dziko lapansi ndi cha nyanja zomwe zili kutali kwambiri,
6 Који си поставио горе својом силом, опасао се јачином,
amene munapanga mapiri ndi mphamvu zanu, mutadziveka nokha ndi mphamvu.
7 Који утишаваш хуку морску, хуку вала њихових и буну по народима!
Amene munakhalitsa bata nyanja kukokoma kwa mafunde ake, ndi phokoso la anthu a mitundu ina.
8 Боје се Твојих чудеса који живе на крајевима земаљским; све што се јавља јутром и вечером Ти будиш да слави Тебе.
Iwo amene akukhala kutali amaopa zizindikiro zozizwitsa zanu; kumene dzuwa limatulukira ndi kumene dzuwa limalowera. Inu mumafuna nyimbo zachimwemwe.
9 Надгледаш земљу и заливаш је, обилно је обогаћаваш; поток је Божји пун воде, спремаш за њих жито, јер си тако уредио.
Inu mumasamalira dziko lapansi ndi kulithirira; Inuyo mumalilemeretsa kwambiri. Mtsinje wa Mulungu ndi wodzaza ndi madzi kuti upereke tirigu kwa anthu, pakuti Inu munakhazikitsa zimenezi.
10 Бразде њене напајаш, равниш груде њене, кишним капљама размекшаваш је, благосиљаш је да рађа.
Mwadzaza nthaka yake ndi madzi ndi kusalaza migula yake, mwayifewetsa ndi mvula yamawawa ndi kudalitsa mbewu zake.
11 Ти венчаваш годину, којој добро чиниш; стопе су Твоје пуне масти.
Inu mumaveka chaka ndi zinthu zochuluka, ndipo ngolo zanu zimasefukira ndi zinthu zochuluka.
12 Тију паше по пустињама, и хумови се опасују радошћу.
Malo a udzu a mʼchipululu amasefukira; mapiri avekedwa ndi chisangalalo.
13 Луке се осипају стадима, и поља се заодевају пшеницом; веселе се и певају.
Madambo akutidwa ndi zoweta ndi zigwa zavekedwa ndi tirigu; izo pamodzi zikufuwula ndi kuyimba mwachimwemwe.