< Псалми 59 >
1 Избави ме од непријатеља мојих, Боже мој, и од оних, што устају на ме, заклони ме.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide. Pamene Sauli anatumiza anthu kuti akalondere nyumba ya Davide ndi cholinga choti amuphe. Landitseni kwa adani anga, Inu Mulungu; munditeteze kwa anthu amene auka kutsutsana nane.
2 Избави ме од оних који чине безакоње, и од крвопија сачувај ме.
Landitseni kwa anthu ochita zoyipa ndipo mundipulumutse kwa anthu okhetsa magazi.
3 Ево, зло намишљају души мојој, скупљају се на ме силни, без кривице моје и без греха мог, Господе.
Onani momwe iwo akundibisalira! Anthu owopsa agwirizana zolimbana nane; osati chifukwa cha mlandu kapena tchimo langa, Inu Yehova.
4 Без кривице моје стечу се и оружају се; устани за мене, и гледај.
Ine sindinachite cholakwa, koma iwo ndi okonzeka kundithira nkhondo. Dzukani kuti mundithandize; penyani mavuto anga!
5 Ти, Господе, Боже над војскама, Боже Израиљев, пробуди се, обиђи све ове народе, немој пожалити одметника.
Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, dzidzutseni nokha kuti mulange anthu a mitundu ina yonse; musaonetse chifundo chanu kwa anthu oyipa achinyengowa.
6 Нек се врате увече, лају као пси и иду око града.
Iwo amabweranso madzulo akuchita phokoso ngati agalu ndi kumangoyendayenda mu mzinda.
7 Ево руже језиком својим, мач им је у устима, јер, веле, ко ће чути?
Onani zomwe amalavula mʼkamwa mwawo; iwo amalavula malupanga kuchokera pa milomo yawo, ndipo amanena kuti, “Ndani angatimve?”
8 Али Ти ћеш се, Господе, смејати њима и посрамити све ове народе.
Koma Inu Yehova, mumawaseka, mumayinyoza mitundu yonseyo.
9 Они су јаки, али ја на Тебе погледам, јер си Ти Бог, чувар мој.
Inu mphamvu yanga, ine ndiyangʼana kwa inu; Inu Mulungu, ndinu linga langa.
10 Бог, који ме милује, иде преда мном, Бог ми даје без страха да гледам непријатеље своје.
Mulungu wanga wachikondi. Mulungu adzapita patsogolo panga ndipo adzandilola kunyada pa iwo amene amandinyoza.
11 Немој их побити, да не би заборавио народ мој; распи их силом својом и обори их, Господе, браничу наш,
Koma musawaphe, Inu Ambuye chishango chathu, kuopa kuti anthu anga angayiwale. Mwa mphamvu zanu, lolani kuti azingoyendayenda ndipo muwatsitse.
12 За грех уста њихових; за речи језика њиховог; нек се ухвате у охолости својој за клетву и лаж коју су говорили.
Chifukwa cha machimo a pakamwa pawo chifukwa cha mawu a milomo yawo, iwo akodwe mʼkunyada kwawo. Chifukwa cha matemberero ndi mabodza amene ayankhula
13 Распи у гневу, распи, да их нема; и нека познају да Бог влада над Јаковом и до крајева земаљских.
muwawononge mu ukali (wanu) muwawononge mpaka atheretu. Pamenepo zidzadziwika ku malekezero a dziko lapansi kuti Mulungu amalamulira Yakobo.
14 Нек се врате увече, лају као пси, и иду око града.
Iwo amabweranso madzulo, akuchita phokoso ngati agalu ndi kumangoyenda mu mzinda.
15 Нека тумарају тражећи хране, и не наситивши се нека ноћи проводе.
Iwo amayendayenda kufuna chakudya ndipo amawuwa ngati sanakhute.
16 А ја ћу певати силу Твоју, рано ујутру гласити милост Твоју; јер си ми био одбрана и уточиште у дан невоље моје.
Koma ine ndidzayimba za mphamvu yanu, mmawa ndidzayimba zachikondi chanu; pakuti ndinu linga langa, pothawirapo panga mʼnthawi ya mavuto.
17 Сило моја! Теби ћу певати, јер си Ти Бог чувар мој, Бог који ме милује.
Inu mphamvu yanga, ndiyimba matamando kwa inu; Inu Mulungu, ndinu linga langa, Mulungu wanga wachikondi.