< Псалми 53 >
1 Рече безумник у срцу свом: Нема Бога; проневаљалише се и загрдеше у безакоњу, нема никога добро да твори.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Mahalati. Ndakatulo ya Davide. Chitsiru chimati mu mtima mwake, “Kulibe Mulungu.” Iwo ndi oyipa ndipo njira zawo ndi zonyansa; palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino.
2 Бог с неба погледа на синове човечије да види има ли који разуман, и тражи ли који Бога.
Mulungu kumwamba amayangʼana pansi pano pa ana a anthu kuti aone ngati alipo wina wanzeru, wofunafuna Mulungu.
3 Сви застранише, сви се покварише, нема никога добро да твори, нема ни једног.
Aliyense wabwerera, iwo onse pamodzi akhala oyipa; palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino, ngakhale mmodzi.
4 Зар неће да се оразуме који год чине безакоње, једу народ мој као што једу хлеб, и не призивају Бога?
Kodi anthu ochita zoyipawa adzaphunziradi; anthu amene amadya anthu anga monga mmene anthu amadyera buledi, ndipo sapemphera kwa Mulungu?
5 Дрхтаће од страха где страха нема. Јер ће Бог расути кости оних који устају на тебе. Ти ћеш их посрамити, јер их Бог одврже.
Iwo anali pamenepo atathedwa nzeru ndi mantha aakulu pamene panalibe kanthu kochititsa mantha. Mulungu anamwazamwaza mafupa a anthu amene anakuthirani nkhondo; inuyo munawachititsa manyazi, pakuti Mulungu anawanyoza.
6 Ко ће послати са Сиона спасење Израиљу? Кад Бог поврати заробљени народ свој, радоваће се Јаков, веселиће се Израиљ.
Ndithu, chipulumutso cha Israeli nʼchochokera ku Ziyoni! Pamene Mulungu adzabwezeretsanso ulemerero wa anthu ake, lolani Yakobo akondwere ndi Israeli asangalale!