< Псалми 34 >
1 Благосиљам Господа у свако доба, хвала је Његова свагда у устима мојим.
Salimo la Davide. Pamene iye ananyengezera misala pamaso pa Abimeleki, amene anamupirikitsa, iyeyo nʼkuchoka. Ndidzayamika Yehova nthawi zonse; matamando ake adzakhala pa milomo yanga nthawi zonse.
2 Господом се хвали душа моја; нека чују који страдају, па нека се радују.
Moyo wanga udzanyadira Yehova; anthu osautsidwa amve ndi kukondwera.
3 Величајте Господа са мном, узвишујмо име Његово заједно.
Lemekezani Yehova pamodzi ndi ine; tiyeni pamodzi tikuze dzina lake.
4 Тражих Господа, и чу ме, и свих невоља мојих опрости ме.
Ine ndinafunafuna Yehova ndipo Iye anandiyankha; anandilanditsa ku mantha anga onse.
5 Који у Њега гледају просветљују се, и лица се њихова неће постидети.
Iwo amene amayangʼana kwa Iye, nkhope zawo zimanyezimira; nkhope zawo sizikhala zophimbidwa ndi manyazi.
6 Овај страдалац завика, и Господ га чу, и опрости га свих невоља његових.
Munthu wosauka uno anayitana, ndipo Yehova anamumva; Yehova anamupulumutsa ku mavuto ake onse.
7 Анђели Господњи станом стоје око оних који се Њега боје, и избављају их.
Mngelo wa Yehova amatchinjiriza amene amakonda Iye ndi kuwalanditsa.
8 Испитајте и видите како је добар Господ; благо човеку који се узда у Њ.
Lawani ndipo onani kuti Yehova ndi wabwino; wodala munthu amene amathawira kwa Iye.
9 Бојте се Господа, свети Његови; јер који се Њега боје, њима нема оскудице.
Wopani Yehova inu oyera mtima ake, pakuti iwo amene amaopa Iye sasowa kanthu.
10 Лавови су убоги и гладни, а који траже Господа, не недостаје им ниједног добра.
Mikango itha kulefuka ndi kumva njala koma iwo amene amafunafuna Yehova sasowa kanthu kalikonse kabwino.
11 Ходите, децо, послушајте ме; научићу вас страху Господњем.
Bwerani ana anga, mundimvere; ndidzakuphunzitsani kuopa Yehova.
12 Који човек жели живот, љуби дане да би видео добро?
Aliyense wa inu amene amakonda moyo wake ndi kukhumba kuti aone masiku abwino ambiri,
13 Устављај језик свој ода зла, и уста своја од преварне речи.
asunge lilime lake ku zoyipa ndi milomo yake kuti isayankhule zonama.
14 Клони се ода зла, и чини добро, тражи мир и иди за њим.
Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; funafuna mtendere ndi kuwulondola.
15 Очи су Господње обраћене на праведнике, и уши Његове на јаук њихов.
Maso a Yehova ali pa olungama ndipo makutu ake ali tcheru kumva kulira kwawo;
16 Али је страшно лице Господње за оне који чине зло, да би истребио на земљи спомен њихов.
nkhope ya Yehova ikutsutsana ndi amene amachita zoyipa, kuwachotsa kuti asawakumbukirenso pa dziko lapansi.
17 Вичу праведни, и Господ их чује, и избавља их од свих невоља њихових.
Olungama amafuwula, ndipo Yehova amawamva; Iye amawalanditsa ku mavuto awo onse.
18 Господ је близу оних који су скрушеног срца, и помаже онима који су смерног духа.
Yehova ali pafupi kwa osweka mtima ndipo amapulumutsa iwo amene asweka mu mzimu.
19 Много невоље има праведник, али га од свих избавља Господ.
Munthu wolungama atha kukhala ndi mavuto ambiri, Koma Yehova amamulanditsa ku mavuto onsewo,
20 Чува Господ све кости његове, ни једна се од њих неће сломити.
Iye amateteza mafupa ake onse, palibe limodzi la mafupawo limene lidzathyoledwa.
21 Безбожника убиће зло, и који ненавиде праведника превариће се.
Choyipa chidzapha anthu oyipa; adani a olungama adzapezeka olakwa.
22 Господ искупљује душу слуга својих, и који се год у Њега уздају, неће се преварити.
Yehova amawombola atumiki ake; aliyense amene amathawira kwa Iye sadzapezeka wolakwa.