< Псалми 27 >
1 Господ је видело моје и спасење моје; кога да се бојим? Господ је крепост живота мог; кога да се страшим?
Salimo la Davide. Yehova ndiye kuwunika kwanga ndi chipulumutso changa; ndidzaopa yani? Yehova ndi linga la moyo wanga; ndidzachita mantha ndi yani?
2 Ако навале на ме зликовци да поједу тело моје, противници и непријатељи моји, спотаћи ће се и пашће.
Pamene anthu oyipa abwera kudzalimbana nane kudzadya mnofu wanga, pamene adani anga ndi achiwembu andithira nkhondo, iwo adzapunthwa ndi kugwa.
3 Ако против мене војска у логор стане, неће се уплашити срце моје; ако се на ме рат дигне, ја се ни онда нећу бојати.
Ngakhale gulu lankhondo lindizinge, mtima wanga sudzaopa. Ngakhale nkhondo itayambika kulimbana nane, ngakhale nthawi imeneyo, ine ndidzalimbika mtima.
4 За једно само молим Господа, само то иштем, да живим у дому Господњем све дане живота свог, да гледам красоту Господњу и раним у цркву Његову.
Chinthu chimodzi chokha chimene ndipempha kwa Yehova, ichi ndi chimene ndidzachifunafuna: kuti ndikhale mʼNyumba ya Yehova masiku onse a moyo wanga, ndi kuyangʼana kukongola kwa Yehova, ndi kumufunafuna Iye mʼNyumba yake.
5 Јер би ме сакрио у колиби својој у зло доба; склонио би ме под кровом шатора свог; на камену гору попео би ме.
Pakuti pa tsiku la msautso Iye adzanditeteza mʼmalo ake okhalamo; adzandibisa mʼkati mwa Nyumba yake ndi kukhazika ine pamwamba pa thanthwe.
6 Тада бих подигао главу своју пред непријатељима који би ме опколили; принео бих у Његовом шатору жртву хвале; запевао бих и хвалио Господа.
Kotero mutu wanga udzakwezedwa kuposa adani anga amene andizungulira; pa Nyumba yake ndidzapereka nsembe ndi mfuwu wachimwemwe; ndidzayimba nyimbo kwa Yehova.
7 Чуј, Господе, глас мој, Тебе призивам, смилуј се на ме и услиши ме.
Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu Yehova mundichitire chifundo ndipo mundiyankhe.
8 Срце моје говори пред Тобом што си рекао: "Тражите лице моје." Тражим лице Твоје, Господе!
Mtima wanga ukuti kwa Inu, “Funafuna nkhope yake!” Nkhope yanu Yehova ndidzayifunafuna.
9 Немој одвратити од мене лице своје, немој у гневу оставити слугу свог; буди Помоћник мој; немој ме одбити, и немој ме оставити, Боже, Спаситељу мој!
Musandibisire nkhope yanu, musamubweze mtumiki wanu mwamkwiyo; mwakhala muli thandizo langa. Musandikane kapena kunditaya, Inu Mulungu Mpulumutsi wanga.
10 Јер отац мој и мати моја оставише ме; али Господ нека ме прихвати.
Ngakhale abambo ndi amayi anga anditaya Yehova adzandisamala.
11 Упути ме, Господе, на пут свој и води ме правом стазом поради оних који ме вребају.
Phunzitseni njira yanu Inu Yehova, munditsogolere mʼnjira yowongoka chifukwa cha ondizunza.
12 Немој ме дати на вољу непријатељима мојим; јер усташе на ме лажни сведоци; али злоба говори сама против себе.
Musandipereke ku zokhumba za adani anga, pakuti mboni zambiri zauka kutsutsana nane ndipo zikundiopseza.
13 Верујем да ћу видети доброту Господњу на земљи живих.
Ine ndikutsimikiza mtima za zimenezi; ndidzaona ubwino wa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
14 Уздај се у Господа, буди слободан; нека буде срце твоје крепко, уздај се у Господа.
Dikirani pa Yehova; khalani anyonga ndipo limbani mtima nimudikire Yehova.