< Псалми 135 >

1 Хвалите име Господње, хвалите, слуге Господње,
Tamandani Yehova. Tamandani dzina la Yehova; mutamandeni, inu atumiki a Yehova,
2 Који стојите у дому Господњем; у дворима дома Бога нашег.
amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova, mʼmabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.
3 Хвалите Господа, јер је добар Господ; појте имену Његовом, јер је слатко.
Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino; imbani nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nʼkokoma kutero,
4 Јер Јакова изабра себи Господ, Израиља за достојање своје.
Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake, Israeli kuti akhale chuma chake chapamtima.
5 Јер познах да је велик Господ, и Господ наш сврх свих богова.
Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu, kuti Ambuye athu ndi wamkulu kuposa milungu yonse.
6 Шта год хоће, све Господ чини, на небесима и на земљи, у морима и у свим безданима.
Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera, kumwamba ndi dziko lapansi, ku nyanja zazikulu ndi ku malo ake onse akuya.
7 Изводи облаке од краја земље, муње чини усред дажда, изводи ветар из стаја његових.
Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi, amatumiza zingʼaningʼani pamodzi ndi mvula ndipo amatulutsa mphepo ku malo ake osungiramo.
8 Он поби првенце у Мисиру од човека до живинчета.
Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, ana oyamba kubadwa a anthu ndi nyama.
9 Показа знаке и чудеса усред тебе, Мисире, на Фараону и на свим слугама његовим.
Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto, kutsutsana ndi Farao pamodzi ndi atumiki ake onse.
10 Поби народе велике, и изгуби цареве јаке:
Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu ndi kupha mafumu amphamvu:
11 Сиона, цара аморејског и Ога, цара васанског, и сва царства хананска;
Sihoni mfumu ya Aamori, Ogi mfumu ya Basani, ndi maufumu onse a ku Kanaani;
12 И даде земљу њихову у достојање, у достојање Израиљу, народу свом.
ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa, cholowa cha anthu ake Aisraeli.
13 Господе! Име је Твоје вечно; Господе! Спомен је Твој од колена до колена.
Dzina lanu, Inu Yehova, ndi losatha mpaka muyaya, mbiri yanu, Inu Yehova, idziwika mibado yonse.
14 Јер ће судити Господ народу свом, и на слуге своје смиловаће се.
Pakuti Yehova adzaonetsa kuti anthu ake ngosalakwa, ndipo adzachitira chifundo atumiki ake.
15 Идоли су незнабожачки сребро и злато, дело руку човечијих;
Mafano a mitundu ya anthu ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
16 Уста имају, а не говоре; очи имају, а не виде;
Pakamwa ali napo koma sayankhula maso ali nawo, koma sapenya;
17 Уши имају, а не чују; нити има дихања у устима њиховим.
makutu ali nawo, koma sakumva ndipo mʼkamwa mwawo mulibe mpweya uliwonse.
18 Какви су они онакви су и они који их граде, и сви који се уздају у њих.
Iwo amene amapanga mafanowo adzakhala ngati mafanowo, chimodzimodzinso iwo amene amadalira mafanowo.
19 Доме Израиљев, благосиљај Господа; доме Аронов, благосиљај Господа;
Inu nyumba ya Israeli, tamandani Yehova; inu nyumba ya Aaroni, tamandani Yehova;
20 Доме Левијев, благосиљај Господа; који се бојите Господа, благосиљајте Господа.
Inu nyumba ya Levi, tamandani Yehova; Inu amene mumaopa Iye, tamandani Yehova.
21 Благословен Господ на Сиону, који живи у Јерусалиму! Алилуја!
Wodalitsika ndi Yehova kuchokera mʼZiyoni, amene amakhala mu Yerusalemu. Tamandani Yehova.

< Псалми 135 >