< Псалми 102 >

1 Господе! Чуј молитву моју, и вика моја нек изађе преда Те.
Pemphero la munthu wosautsidwa, pamene walefuka, nakhuthulira pamaso pa Yehova kulira kwakeko. Yehova imvani pemphero langa; kulira kwanga kopempha thandizo kufike kwa Inu.
2 Немој одвратити лице своје од мене; у дан кад сам у невољи пригни к мени ухо своје, у дан кад Те призивам, похитај, услиши ме.
Musandibisire nkhope yanu pamene ndili pa msautso. Munditcherere khutu; pamene ndiyitana ndiyankheni msanga.
3 Јер прођоше као дим дани моји, кости моје као топионица огореше.
Pakuti masiku anga akupita ngati utsi; mafupa anga akunyeka ngati nkhuni zoyaka.
4 Покошено је као трава и посахло срце моје, да заборавих јести хлеб свој.
Mtima wanga wakanthidwa ndipo ukufota ngati udzu; ndipo ndimayiwala kudya chakudya changa.
5 Од уздисања мог приону кост моја за месо моје.
Chifukwa cha kubuwula kwanga kofuwula ndatsala chikopa ndi mafupa okhaokha.
6 Постадох као гем у пустињи; ја сам као сова на зидинама.
Ndili ngati kadzidzi wa ku chipululu, monga kadzidzi pakati pa mabwinja.
7 Не спавам, и седим као птица без друга на крову.
Ndimagona osapeza tulo; ndakhala ngati mbalame yokhala yokha pa denga.
8 Сваки дан руже ме непријатељи моји, и који су се помамили на мене, мном се уклињу.
Tsiku lonse adani anga amandichita chipongwe; iwo amene amandinyoza, amagwiritsa ntchito dzina langa ngati temberero.
9 Једем пепео као хлеб, и пиће своје растварам сузама.
Pakuti ndimadya phulusa ngati chakudya changa ndi kusakaniza chakumwa changa ndi misozi
10 Од гнева Твог и срдње Твоје; јер подигавши ме бацио си ме.
chifukwa cha ukali wanu waukulu, popeza Inu mwandinyamula ndi kunditayira kumbali.
11 Дани су моји као сен, који пролази, и ја као трава осуших се.
Masiku anga ali ngati mthunzi wa kumadzulo; Ine ndikufota ngati udzu.
12 А Ти, Господе, остајеш довека, и спомен Твој од колена до колена.
Koma Inu Yehova, muli pa mpando wanu waufumu kwamuyaya; kudziwika kwanu ndi kokhazikika ku mibado yonse.
13 Ти ћеш устати, смиловаћеш се на Сион, јер је време смиловати се на њ, јер је дошло време;
Inu mudzadzuka ndi kuchitira chifundo Ziyoni pakuti ndi nthawi yoti muonetse kukoma mtima kwanu pa iyeyo; nthawi yoyikika yafika.
14 Јер слугама Твојим омиле и камење његово, и прах његов жале.
Pakuti miyala yake ndi yokondedwa kwa atumiki anu; fumbi lake lokha limawachititsa kuti amve chisoni.
15 Тада ће се незнабошци бојати имена Господњег, и сви цареви земаљски славе Његове;
Mitundu ya anthu idzaopa dzina la Yehova, mafumu onse a dziko lapansi adzalemekeza ulemerero wanu.
16 Јер ће Господ сазидати Сион, и јавити се у слави својој;
Pakuti Yehova adzamanganso Ziyoni ndi kuonekera mu ulemerero wake.
17 Погледаће на молитву оних који немају помоћи, и неће се оглушити молбе њихове.
Iye adzayankha pemphero la anthu otayika; sadzanyoza kupempha kwawo.
18 Написаће се ово потоњем роду, и народ наново створен хвалиће Господа.
Zimenezi zilembedwe chifukwa cha mibado ya mʼtsogolo, kuti anthu amene sanabadwe adzatamande Yehova:
19 Што је приникао са свете висине своје, Господ погледао с неба на земљу.
“Yehova anayangʼana pansi kuchokera ku malo ake opatulika mmwamba, kuchokera kumwamba anayangʼana dziko lapansi,
20 Да чује уздисање сужњево, и одреши синове смртне;
kuti amve kubuwula kwa anthu a mʼndende, kuti apulumutse amene anayenera kuphedwa.”
21 Да би казивали на Сиону име Господње и хвалу Његову у Јерусалиму,
Kotero dzina la Yehova lidzalengezedwa mu Ziyoni ndi matamando ake mu Yerusalemu,
22 Кад се скупе народи и царства да служе Господу.
pamene mitundu ya anthu ndi maufumu adzasonkhana kuti alambire Yehova.
23 Строшио је на путу крепост моју, скратио дане моје.
Iye anathyola mphamvu zanga pa nthawi ya moyo wanga; Iyeyo anafupikitsa masiku anga.
24 Рекох: Боже мој! Немој ме узети у половини дана мојих. Твоје су године од колена до колена.
Choncho Ine ndinati: “Musandichotse, Inu Mulungu wanga, pakati pa masiku a moyo wanga; zaka zanu zimakhalabe pa mibado yonse.
25 Давно си поставио земљу, и небеса су дело руку Твојих.
Pachiyambi Inu munakhazikitsa maziko a dziko lapansi ndipo mayiko akumwamba ndi ntchito ya manja anu.
26 То ће проћи, а Ти ћеш остати; све ће то као хаљина оветшати, као хаљину променићеш их и промениће се.
Izi zidzatha, koma Inu mudzakhalapo; zidzatha ngati chovala. Mudzazisintha ngati chovala ndipo zidzatayidwa.
27 Али Ти си тај исти и године Твоје неће истећи.
Koma Inu simusintha, ndipo zaka zanu sizidzatha.
28 Синови ће слуга Твојих живети, и семе ће се њихово утврдити пред лицем Твојим.
Ana a atumiki anu adzakhala pamaso panu; zidzukulu zawo zidzakhazikika pamaso panu.”

< Псалми 102 >