< Псалми 101 >
1 Милост и правду певам; Тебе, Господе, славим.
Salimo la Davide. Ndidzayimba za chikondi ndi chiweruzo chanu cholungama; kwa Inu Yehova ndidzayimba matamando.
2 Размишљам о путу правом, кад би год дошао к мени, ходим у безазлености срца свог у дому свом.
Ndidzatsata njira yolungama; nanga mudzabwera liti kwa ine? Ndidzayenda mʼnyumba mwanga ndi mtima wosalakwa.
3 Не стављам пред очи своје речи непотребне, мрзим на дела која су против закона, не пристајем за њима.
Sindidzayika chinthu chilichonse choyipa pamaso panga. Ine ndimadana ndi zochita za anthu opanda chikhulupiriro; iwo sadzadziphatika kwa ine.
4 Срце покварено далеко је од мене; злих не знам.
Anthu a mtima wokhota adzakhala kutali ndi ine; ine sindidzalola choyipa chilichonse kulowa mwa ine.
5 Ко тајно опада ближњег свог, тог изгоним; ко је охолог ока и надутог срца, тог не трпим.
Aliyense wosinjirira mnansi wake mseri ameneyo ndidzamuletsa; aliyense amene ali ndi maso amwano ndi mtima wodzikuza, ameneyo sindidzamulekerera.
6 Очи су моје обраћене на верне на земљи, да би седели са мном. Ко ходи путем правим, тај служи мени.
Maso anga adzakhala pa okhulupirika mʼdziko, kuti akhale pamodzi ndi ine; iye amene mayendedwe ake ndi wosalakwa adzanditumikira.
7 Не живи у дому мом који ради лукаво; који говори лаж, не стоји пред очима мојим.
Aliyense wochita chinyengo sadzakhala mʼnyumba mwanga. Aliyense woyankhula mwachinyengo sadzayima pamaso panga.
8 Јутром затирем све безбожнике на земљи, да бих истребио из града Господњег све који чине безакоње.
Mmawa uliwonse ndidzatontholetsa anthu onse oyipa mʼdziko; ndidzachotsa aliyense wochita zoyipa mu mzinda wa Yehova.