< Приче Соломонове 18 >

1 Човек самовољан тражи шта је њему мило и меша се у свашта.
Munthu wokonda kukhala yekha amafunafuna zomukomera yekha; iye amatsutsana ndi malangizo onse anzeru.
2 Безумнику није мио разум него да се јавља срце његово.
Chitsiru chilibe chidwi chomvetsa zinthu, koma chimakondwera ndi kuyankhula maganizo ake okha.
3 Кад дође безбожник, дође и руг, и прекор са срамотом.
Kuyipa mtima kukabwera, manyozonso amabwera. Manyazi amabwera pamodzi ndi kunyozeka.
4 Речи су из уста човечијих дубока вода, извор је мудрости поток који се разлива.
Mawu a munthu ali ngati madzi akuya, kasupe wa nzeru ndiye mtsinje wotumphuka.
5 Није добро гледати безбожнику ко је, да се учини криво правом на суду.
Si kwabwino kukondera munthu woyipa pa milandu; kapena kupondereza munthu wosalakwa.
6 Усне безумникове пристају у свађу, и уста његова дозивају бој.
Mawu a chitsiru amautsa mkangano; pakamwa pake pamayitana mkwapulo.
7 Безумнику су уста његова погибао, и усне његове пругло души његовој.
Pakamwa pa chitsiru ndipo pamabweretsa chiwonongeko chake, ndipo milomo yake ili ngati msampha wa moyo wake.
8 Речи су опадачеве као избијених, али силазе унутра у трбух.
Mawu a miseche ali ngati chakudya chokoma; amalowa mʼmimba mwa munthu.
9 И ко је немаран у послу свом брат је распикући.
Munthu waulesi pa ntchito yake ali pachibale ndi munthu amene amawononga zinthu.
10 Тврда је кула име Господње. К Њему ће побећи праведник, и биће у високом заклону.
Dzina la Yehova lili ngati nsanja yolimba; wolungama amathawiramo napulumuka.
11 Богатство је богатом јак град и као висок зид у његовој мисли.
Chuma cha anthu olemera chili ngati mzinda wake wolimba; chili ngati khoma lalitali limene amaganiza kuti limutchinjiriza.
12 Пред пропаст подиже се срце човека, а пре славе иде смерност.
Chiwonongeko chisanafike, mtima wa munthu umakhala wonyada, koma ulemu umatsatira kudzichepetsa.
13 Ко одговара пре него чује, томе је лудост и срамота.
Ukayankha usanamvetse bwino nkhani, umenewo ndi uchitsiru ndipo umachita manyazi.
14 Дух човечији сноси бол свој; а дух оборен ко ће подигнути?
Mtima wa munthu utha kupirira pa matenda, koma munthu akataya mtima ndani angathe kumulimbitsanso.
15 Срце разумног човека добавља знање, и ухо мудрих тражи знање.
Munthu wanzeru amawonjezera nzeru zina; amafunafuna kudziwa bwino zinthu.
16 Дар човеку шири место и води га пред властеље.
Mphatso ya munthu imamutsekulira njira yomufikitsa pamaso pa anthu akuluakulu.
17 Праведан се чини ко је први у својој распри, али кад дође ближњи његов, испитује се.
Amene amayamba kufotokoza mlandu wake amaoneka ngati wolungama ndiye mpaka mnzake atabwera ndi kumufunsa bwino.
18 Распре прекида жреб, и између силних расуђује.
Kuchita maere kumathetsa mikangano; amalekanitsa okangana amphamvu.
19 Увређен је брат као тврд град, и свађа је као преворница на двору.
Mʼbale amene wamuthandiza amakhala ngati mzinda wolimba, koma kukangana naye kumatsekereza thandizo.
20 Сваком се трбух сити плодом уста његових, дохотком од усна својих сити се.
Munthu amapeza bwino malingana ndi zoyankhula zake. Adzakhuta ndi zipatso za pakamwa pake.
21 Смрт је и живот у власти језику, и ко га милује, јешће плод његов.
Mawu ako angathe kukuphetsa kapena kukukhalitsa moyo. Wokonda kuyankhulayankhula adzadya zipatso zake.
22 Ко је нашао жену, нашао је добро и добио љубав од Господа.
Wapeza mkazi wapeza chinthu chabwino ndipo Yehova amamukomera mtima.
23 Сиромах говори молећи, а богат одговара оштро.
Munthu wosauka amapempha koma munthu wolemera amayankha mwaukali.
24 Ко има пријатеља, ваља да поступа пријатељски, јер има пријатеља вернијих од брата.
Pali abwenzi amene chibwenzi chawo nʼchapamaso, koma pali bwenzi limene limakukangamira kuposa mʼbale wako.

< Приче Соломонове 18 >