< 4 Мојсијева 15 >

1 Опет рече Господ Мојсију говорећи:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Реци синовима Израиљевим и кажи им: Кад дођете у земљу где ћете наставати, коју ћу вам ја дати,
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Mukakalowa mʼdziko limene ndikukupatsanilo,
3 И станете приносити жртву огњену Господу, жртву паљеницу или жртву завета ради или од драге воље, или о празницима својим, готовећи мирис угодни Господу од крупне или од ситне стоке,
ndipo mukamadzapereka kwa Yehova, nsembe yotentha pa moto ya ngʼombe kapena nkhosa monga fungo lokoma kwa Yehova, kaya ndi nsembe yopsereza kapena nsembe zina, nsembe yapadera chifukwa cha lumbiro kapena nsembe yoperekedwa mwaufulu kapenanso yoperekedwa pa chikondwerero,
4 Тада ко принесе принос свој Господу, нека донесе уза њ дар, десетину ефе белог брашна помешаног с четвртином ина уља.
munthu amene akubweretsa zopereka zake, azikapereka kwa Yehova chopereka chachakudya cholemera kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta wokwana lita imodzi.
5 И вина четврт ина за налив донеси уз жртву паљеницу или уз другу жртву, на свако јагње.
Pamodzi ndi mwana wankhosa aliyense wa nsembe yopsereza kapena nsembe ina, muzikakonzanso lita imodzi la vinyo ngati chopereka cha chakumwa.’”
6 А уз овна донеси дар, две десетине белог брашна помешаног са трећином ина уља,
“Pamodzi ndi nkhosa yayimuna, muzikakonzanso chopereka cha chakudya cholemera makilogalamu awiri a ufa wosalala, wosakaniza ndi mafuta okwanira lita imodzi ndi theka,
7 И вина за налив трећину ина принећеш за мирис угодни Господу.
ndi vinyo wokwanira lita imodzi ndi theka ngati chopereka cha chakumwa. Muzikapereka monga nsembe yopereka fungo lokoma kwa Yehova.
8 А кад приносиш теле на жртву паљеницу или на жртву ради завета или на жртву захвалну Господу,
“‘Pamene mukukonza mwana wangʼombe wamwamuna kuti akhale nsembe yopsereza kapena nsembe ina iliyonse: ya lumbiro lapadera kapena nsembe yachiyanjano kwa Yehova,
9 Онда нека се донесе уз теле дар, три десетине ефе белог брашна помешаног с по ина уља,
pamodzi ndi mwana wangʼombe wamwamunayo muzibweretsa nsembe yachakudya yolemera makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta okwana malita awiri.
10 И вина донеси за налив по ина; то је жртва огњена за мирис угодни Господу.
Komanso muzibweretsa vinyo wokwanira malita awiri monga chopereka chachakumwa. Imeneyi idzakhala chopereka chotentha pa moto kuti likhale fungo lokoma kwa Yehova.
11 Тако нека буде уза сваког вола и уза сваког овна и уза свако живинче између оваца или коза.
Ngʼombe yayimuna iliyonse kapena nkhosa yayimuna iliyonse, mwana wankhosa aliyense kapena mbuzi yayingʼono, zizikonzedwa motere.
12 Према броју колико принесете, учините тако уза свако, колико их буде.
Ngakhale zingachuluke chotani, chitani izi kwa iliyonse ya nyamazo.
13 Сваки домородац тако нека чини приносећи жртву паљеницу за мирис угодни Господу.
“‘Mbadwa iliyonse ya mu Israeli izichita zimenezi pamene ibweretsa nsembe yotentha pa moto kuti ikhale fungo lokoma kwa Yehova.
14 Тако ако буде међу вама и дошљак или ко би се бавио међу вама, па би принео жртву огњену за мирис угодни Господу, нека чини онако како ви чините.
Ku mibado yanu yonse ya mʼtsogolo, pamene mlendo kapena wina aliyense wokhala pakati panu apereka chopereka chotentha pa moto kuti chikhale fungo lokoma kwa Yehova, azichita mofanana ndi momwe inu mumachitira.
15 Зборе! Вама и дошљаку који је међу вама један да је закон, закон вечан од колена на колено; дошљак ће бити као и ви пред Господом.
Gulu lonse likhale ndi malamulo ofanana a inu kapena mlendo wokhala pakati panu. Limeneli ndi lamulo lamuyaya kwa mibado imene ikubwera. Inuyo ndi mlendo mudzakhala wofanana pamaso pa Yehova.
16 Један закон и једна уредба да буде вама и дошљаку, који је међу вама.
Mudzakhale ndi malamulo ndi miyambo yofanana, inuyo ndi mlendo wokhala pakati panu.’”
17 Још рече Господ Мојсију говорећи:
Yehova anawuza Mose kuti,
18 Кажи синовима Израиљевим и реци им: Кад дођете у земљу, у коју ћу вас ја одвести,
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo unene kuti, ‘Mukakalowa mʼdziko limene ndikukutengeraniko
19 Па станете јести хлеб оне земље, тада принесите принос Господу.
ndipo mukakadya chakudya cha mʼdzikolo, mukapereke gawo lina kwa Yehova monga chopereka.
20 Од првина теста свог приносите у принос колач, као принос од гумна тако га приносите.
Pa buledi wanu woyamba, mukapereke mmodzi monga nsembe, ngati chopereka chochokera ku malo wopunthira tirigu.
21 Од првина теста свог дајте Господу принос од колена до колена.
Pa mibado yanu yonse muzidzapereka chopereka ichi kwa Yehova kuchokera ku zakudya zanu zoyamba za mʼnthaka.
22 А кад бисте погрешили, те не бисте учинили свих ових заповести, које каза Господ Мојсију,
“‘Ndipo ngati muchimwa mosadziwa posasunga ena mwa malamulo awa amene Yehova wapereka kwa Mose,
23 Све што вам је заповедио Господ преко Мојсија, од дана кад заповеди Господ и после од колена до колена,
lina lililonse mwa malamulo a Yehova amene wapereka kwa inu kudzera mwa Mose, kuyambira tsiku limene Yehova anawapereka mpaka mibado ya mʼtsogolo,
24 Ако се буде учинило погрешком, да збор не зна, онда сав збор нека принесе на жртву паљеницу за мирис угодни Господу теле с даром његовим и с наливом његовим по уредби, и једно јаре на жртву за грех.
ndipo ngati zimenezi zachitika osati mwadala ndipo gulu lonse silinadziwe, zikatero gulu lonselo lipereke mwana wangʼombe wamwamuna monga nsembe yopsereza kuti likhale fungo lokoma kwa Yehova pamodzinso ndi chopereka chachakudya ndi chopereka cha chakumwa ndi mbuzi yayimuna ngati nsembe yopepesera machimo potsata zimene zinalamulidwa.
25 И свештеник нека очисти сав збор синова Израиљевих, и опростиће им се, јер је погрешка и они донесоше пред Господа свој принос за жртву огњену Господу и принос за грех свој ради погрешке своје.
Wansembe apereke nsembe yopepesera machimo a gulu lonse la Aisraeli, ndipo adzakhululukidwa, pakuti linali tchimo lochita mosadziwa. Ndipo chifukwa cha tchimo lawolo, abweretse kwa Yehova nsembe yotentha pa moto ndi nsembe yopepesera machimo.
26 Опростиће се свему збору синова Израиљевих и дошљаку који се бави међу њима, јер је погрешка свега народа.
Gulu lonse la Aisraeli ndi alendo okhala pakati pawo adzakhululukidwa chifukwa anthu onsewo anachimwa mosadziwa.
27 Ако ли једна душа згреши не знајући, нека принесе козу од године на жртву за грех.
“‘Koma ngati munthu mmodzi achimwa mosadziwa, ayenera kubweretsa mbuzi yayikazi ya chaka chimodzi kuti ikhale nsembe yopepesera machimo.
28 И свештеник нека очисти душу која буде згрешила не знајући пред Господом, и кад је очисти опростиће јој се.
Wansembe apereke nsembe yopepesera machimowo pamaso pa Yehova chifukwa cha munthu yemwe anachimwa mosadziwayo. Nsembe yopepesera tchimo lakelo ikaperekedwa, munthuyo adzakhululukidwa.
29 И за рођеног у земљи синова Израиљевих и за дошљака, који се бави међу вама, један закон нека буде кад ко згреши не знајући.
Lamulo lomweli ligwiritsidwe ntchito kwa aliyense wochimwa mosadziwa, kaya ndi mbadwa ya mu Israeli kapena mlendo.
30 Али ко од силе згреши између рођених у земљи или између дошљака, он ружи Господа; нека се истреби душа она из народа свог.
“‘Koma aliyense amene achimwa mwadala, kaya ndi mbadwa kapena mlendo, nachitira chipongwe Yehova, ameneyo achotsedwe ndithu pakati pa anthu ake.
31 Јер презре реч Господњу, и заповест Његову погази; нека се истреби она душа; безакоње је њено на њој.
Popeza wanyoza mawu a Yehova ndi kuphwanya malamulo ake. Munthu ameneyo achotsedwe ndithu, kuchimwa kwake kudzakhala pa iyeyo.’”
32 А кад беху синови Израиљеви у пустињи, нађоше једног где купи дрва у суботу.
Aisraeli ali mʼchipululu, munthu wina anapezeka akutola nkhuni tsiku la Sabata.
33 И који га нађоше где купи дрва, доведоше га к Мојсију и к Арону и ка свему збору.
Amene anamupeza akutola nkhunizo anabwera naye kwa Mose ndi Aaroni ndi kwa gulu lonse
34 И метнуше га под стражу, јер не беше казано шта ће се чинити с њим.
ndipo anamutsekera mʼndende chifukwa sankadziwa choti achite naye.
35 А Господ рече Мојсију: Нека се погуби тај човек; нека га заспе камењем сав збор иза логора.
Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti, “Munthu ameneyu ayenera kuphedwa. Gulu lonse liyenera kumugenda ndi miyala kunja kwa msasa.”
36 И сав збор изведе га иза логора и засуше га камењем, и умре, као што заповеди Господ Мојсију.
Choncho gululo linamutengera kunja kwa msasa ndi kumupha pomugenda ndi miyala, monga momwe Yehova analamulira Mose.
37 Још рече Господ Мојсију говорећи:
Yehova anawuza Mose kuti,
38 Реци синовима Израиљевим и кажи им, нека ударају ресе по скутовима од хаљина својих од колена до колена, и над ресе нека мећу врпцу плаву.
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Pa mibado yanu yonse muzisokerera mphonje pa ngodya za zovala zanu ndipo pa ngodya ya mphonje iliyonse azisokererapo chingwe chobiriwira.
39 И имаћете ресе зато да се гледајући их опомињете свих заповести Господњих и творите их, и да се не заносите за срцем својим и за очима својим, за којима чините прељубу;
Mudzakhala ndi mphonje zimenezi kuti mukaziona muzikakumbukira malamulo onse a Yehova ndi kuwamvera kuti musamatsatenso zilakolako za mʼmitima mwanu ndi za maso anu.
40 Него да памтите и творите све заповести моје, и будете свети Богу свом.
Motero mudzakumbukira kumvera malamulo anga ndipo mudzakhala opatulikira a Mulungu wanu.
41 Ја сам Господ Бог ваш, који сам вас извео из земље мисирске, да вам будем Бог. Ја сам Господ Бог ваш.
Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto kuti ndikhale Mulungu wanu. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”

< 4 Мојсијева 15 >