< 4 Мојсијева 10 >
1 Још рече Господ Мојсију говорећи:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Начини себи две трубе од сребра, коване да буду; њима ћеш сазивати збор и заповедати да полази војска.
“Sula malipenga awiri a siliva, ndipo uziwagwiritsa ntchito posonkhanitsa anthu pamodzi ndiponso powasamutsa mʼmisasa.
3 Кад обе затрубе, тада нека се скупља к теби сав збор на врата шатора од састанка.
Pamene akuliza malipenga onse awiri, anthu onse asonkhane kwa iwe pa khomo la tenti ya msonkhano.
4 А кад једна затруби, тада нека се скупљају к теби кнезови, главари од хиљада Израиљевих.
Akaliza limodzi lokha, atsogoleri, akulu a mafuko a Aisraeli, asonkhane kwa iwe.
5 А кад затрубе потресајући, тада нека се креће логор који лежи према истоку.
Akaliza lipenga lochenjeza, misasa yomwe ili kummawa iyambe kusamuka.
6 А кад затрубите други пут потресајући, онда нека се креће логор који је на југу; потресајући нека се труби кад треба да пођу.
Akaliza lipenga lochenjeza lachiwiri, misasa yakummwera iyambe kusamuka. Kuliza kwa lipenga lochenjeza kudzakhala chizindikiro choyamba ulendo.
7 А кад сазивате збор, трубите, али не потресајући.
Pofuna kusonkhanitsa anthu, muziliza malipenga, koma mosiyana ndi mmene malipenga ochenjeza amalizidwira.
8 А нека трубе у трубе синови Аронови свештеници; то да вам је уредба вечна од колена до колена.
“Ana a Aaroni, ansembe aja, ndiwo aziliza malipengawo. Zimenezi zikhale zokhazikika kwa inu ndi ku mibado yanu yonse.
9 И кад пођете на војску у земљи својој на непријатеља који удари на вас, трубите у трубе потресајући; и Господ Бог ваш опоменуће вас се, и сачуваћете се од непријатеља својих.
Pamene mukupita ku nkhondo mʼdziko lanu lomwe, kulimbana ndi mdani amene akukuzunzani, muziliza malipenga ochenjeza ndipo Yehova Mulungu wanu adzakukumbukirani ndi kukulanditsani mʼmanja mwa adani anu.
10 Тако и у дан весеља свог и на празнике своје и почетке месеца својих трубите у трубе приносећи жртве своје паљенице и жртве своје захвалне, и биће вам спомен пред Богом вашим. Ја сам Господ Бог ваш.
Komanso pa nthawi yanu ya chisangalalo, pa maphwando anu oyikika ndi maphwando a mwezi watsopano, muziliza malipenga pa nsembe zanu zopsereza ndi nsembe zanu za chiyanjano, ndipo zidzakhala chikumbutso chanu pamaso pa Mulungu. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.”
11 И у двадесети дан другог месеца друге године подиже се облак изнад шатора од сведочанства.
Pa chaka chachiwiri, mwezi wachiwiri, tsiku la 20, mtambo unachoka pamwamba pa chihema cha umboni.
12 И пођоше синови Израиљеви својим редом из пустиње Синајске, и устави се облак у пустињи Фаранској.
Ndipo Aisraeli ananyamuka kuchoka mʼchipululu cha Sinai ndipo anayenda malo osiyanasiyana mpaka pamene mtambo unayima mʼchipululu cha Parani.
13 Тако пођоше први пут, као што Господ заповеди преко Мојсија.
Kameneka kanali koyamba kuti Aisraeli anyamuke monga momwe Yehova analamulira Mose.
14 И пође напред застава војске синова Јудиних у четама својим; и над војском њиховом беше Насон, син Аминадавов;
Magulu a msasa wa Yuda ndiwo anayamba kunyamuka potsata mbendera yawo. Mtsogoleri wa gulu lawo anali Naasoni mwana wa Aminadabu.
15 А над војском племена синова Исахарових Натанаило, син Согаров;
Mtsogoleri wa gulu la fuko la Isakara anali Netanieli mwana wa Zuwara,
16 А над војском племена синова Завулонових Елијав, син Хелонов.
Eliabu mwana wa Heloni ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Zebuloni.
17 И сложише шатор, па пођоше синови Гирсонови и синови Мераријеви носећи шатор.
Kenaka anagwetsa chihema, ndipo Ageresoni ndi Amerari amene ananyamula chihemacho, ananyamuka.
18 Потом пође застава војске синова Рувимових, а над њиховом војском беше Елисур, син Седијуров,
Kenaka magulu a msasa wa fuko la Rubeni ananyamuka potsatira mbendera yawo. Mtsogoleri wawo anali Elizuri mwana wa Sedeuri.
19 А над војском племена синова Симеунових Саламило, син Сурисадајев,
Mtsogoleri wa fuko la Simeoni anali Selumieli mwana wa Zurisadai,
20 А над војском племена синова Гадових Елисаф син Рагуилов.
ndipo Eliyasafu mwana wa Deuweli ndiye ankatsogolera fuko la Gadi.
21 И пођоше синови Катови носећи светињу, да би они подигли шатор докле ови дођу.
Kenaka Akohati ananyamuka atanyamula zinthu zopatulika. Chihema chinkayenera kuyimikidwa iwo asanafike.
22 Потом пође застава војске синова Јефремових у четама својим, а над војском њиховом беше Елисама, син Емијудов,
Magulu a msasa wa Aefereimu anatsatira potsatira mbendera yawo. Elisama mwana wa Amihudi ndiye anali mtsogoleri wawo.
23 А над војском племена синова Манасијиних Гамалило син Фадасуров,
Gamalieli mwana wa Pedazuri ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Manase.
24 А над војском племена синова Венијаминових Авидан син Гадеонијев.
Abidani mwana wa Gideoni ndiye anali mtsogoleri wa mtundu wa Benjamini.
25 Најпосле пође застава војске синова Данових у четама својим, задња војска, и над војском њиховом беше Ахијезер, син Амисадајев,
Pambuyo pa magulu onse panali magulu a msasa wa Dani, omwe ankateteza magulu onsewa ndipo ananyamuka potsatira mbendera yawo. Mtsogoleri wawo anali Ahiyezeri mwana wa Amisadai.
26 А над војском племена синова Асирових Фагаило, син Ехранов,
Pagieli mwana wa Okirani ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Aseri,
27 А над војском племена синова Нефталимових Ахиреј, син Енанов.
ndipo mtsogoleri wa mtundu wa Nafutali anali Ahira mwana wa Enani.
28 Тим редом пођоше синови Израиљеви у четама својим, и тако иђаху.
Umenewu ndiwo unali mndandanda wa kayendedwe ka magulu a Aisraeli pamene ankanyamuka ulendo wawo mʼmagulumagulu.
29 А Мојсије рече Јоваву, сину Рагуиловом Мадијанину тасту свом: Идемо на место за које рече Господ: Вама ћу га дати. Хајде с нама, и добро ћемо ти учинити, јер је Господ обећао Израиљу много добра.
Ndipo Mose anawuza Hobabu mwana wa Reueli Mmidiyani, mpongozi wa Mose kuti, “Tikunyamuka kupita ku malo amene Yehova anati, ‘Ndidzakupatsani.’ Tiye upite nafe ndipo tidzakusamalira bwino, pakuti Yehova analonjeza zinthu zabwino kwa Israeli.”
30 А он му рече: Нећу ићи, него идем у своју земљу и у род свој.
Hobabu anayankha kuti, “Ayi, sindipita nanu, ndibwerera ku dziko la kwathu ndi kwa abale anga.”
31 А Мојсије рече: Немој нас оставити, јер знаш места у пустињи где бисмо могли стајати, па нам буди вођ.
Ndipo Mose anati, “Pepa usatisiye popeza ukudziwa kumene tingamange misasa mʼchipululu muno ndipo udzakhala maso athu.
32 И ако пођеш с нама кад дође добро које ће нам учинити Господ, учинићемо ти добро.
Iweyo ukapita nafe, tidzagawana nawe zinthu zabwino zomwe Yehova adzatipatsa.”
33 И тако пођоше од горе Господње, и иђаху три дана, и ковчег завета Господњег иђаше пред њима три дана тражећи место где би починули.
Motero ananyamuka ku Phiri la Yehova nayenda ulendo wa masiku atatu. Bokosi la Chipangano cha Yehova linkayenda patsogolo pawo pa masiku atatuwo kuti apeze malo woti apumulepo.
34 И облак Господњи беше над њима сваки дан кад полажаху с места, где беху у логору.
Mtambo wa Yehova unkawaphimba masana pamene ankasamuka pa misasa yawo.
35 И кад полажаше ковчег, говораше Мојсије: Устани Господе, и нека се разаспу непријатељи Твоји, и нека беже испред Тебе који мрзе на Те.
Nthawi iliyonse imene Bokosi la Chipangano likunyamuka, Mose ankanena kuti, “Dzukani, Inu Yehova! Adani anu abalalike; Odana nanu athawe pamaso panu.
36 А кад се устављаше, говораше: Уврати се, Господе, к мноштву хиљада Израиљевих.
“Pamene likupumula, ankanena kuti, “Bwererani, Inu Yehova, ku chinamtindi cha Aisraeli.”