< Књига о судијама 1 >

1 А по смрти Исусовој упиташе синови Израиљеви Господа говорећи: Ко ће између нас ићи први на Хананеје да се бије с њима?
Atamwalira Yoswa Aisraeli anafunsa Yehova kuti, “Ndani mwa ife ayambe nkhondo yomenyana ndi Akanaani?”
2 И Господ рече: Јуда нека иде; ето дао сам му земљу у руке.
Yehova anayankha kuti, “Fuko la Yuda ndilo liyambe kupita. Ndawapatsa dzikolo mʼmanja mwawo.”
3 А Јуда рече Симеуну брату свом: Хајде са мном на мој део да се бијемо с Хананејима; пак ћу и ја ићи с тобом на твој део. И пође Симеун с њим.
Choncho Ayuda anawuza abale awo a fuko la Simeoni kuti, “Bwerani tipitire limodzi mʼdziko limene tapatsidwa kuti tikamenyane ndi Akanaani. Ifenso tidzapita nanu mʼdziko limene anakugawirani.” Ndipo Asimeoni anapita nawo.
4 И изиђе Јуда; и даде им Господ Хананеје и Ферезеје у руке, и побише их у Везеку десет хиљада људи.
Choncho Ayuda ananyamuka, ndipo Yehova anapereka Akanaani ndi Aperezi mʼmanja mwawo. Ndipo anapha anthu 10,000 ku Bezeki.
5 Јер нађоше Адони-Везека у Везеку, и ударише на њ, и побише Хананеје и Ферезеје.
Ku Bezekiko anakumana ndi ankhondo a mfumu Adoni-Bezeki ndipo anamenyana nawo, ndipo Ayudawo anagonjetsa Akanaani ndi Aperezi.
6 И побеже Адони-Везек, а они га потераше и ухвативши га одсекоше му палце у руку и у ногу.
Adoni-Bezekiyo anathawa, koma anamuthamangira ndi kumupeza, namugwira. Atamugwira anamudula zala zake zazikulu za ku manja ndi miyendo.
7 Тада рече Адони-Везек: Седамдесет царева одсечених палаца у руку и у ногу купише шта беше под мојим столом; како сам чинио, тако ми плати Бог. И одведоше га у Јерусалим, и онде умре.
Tsono Adoni-Bezeki anati, “Mafumu 70 omwe anadulidwa zala zazikulu za ku manja ndi miyendo yawo ankatola nyenyeswa pansi pa tebulo langa. Mulungu tsopano wandibwezera zomwe ndinawachita.” Kenaka anapita naye ku Yerusalemu ndipo anafera komweko.
8 Јер синови Јудини ударише на Јерусалим и узеше га, и исекоше грађане оштрим мачем, а град сажегоше огњем.
Pambuyo pake Ayuda anakathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu ndipo anawulanda. Anapha anthu ambiri ndi kutentha mzinda wonse.
9 Потом изиђоше синови Јудини да војују на Хананеје, који живљаху у гори и на југу и у равни.
Kenaka Ayuda anapita kukamenyana ndi Akanaani omwe amakhala ku dziko la ku mapiri, dziko la Negevi kummwera ndiponso mu zigwa.
10 И Јуда изиђе на Хананеје који живљаху у Хеврону, а Хеврону беше пре име Киријат-Арва; и побише Сесаја и Ахимана и Талмаја.
Anakalimbananso ndi Akanaani amene ankakhala ku Hebroni (mzinda womwe kale unkatchedwa Kiriyati-Araba). Kumeneko anagonjetsa Sesai, Ahimani ndi Talimai.
11 А одатле отидоше на Давиране, а Давиру пре беше име Киријат-Сефер.
Kuchokera kumeneko, iwo anakathira nkhondo anthu amene ankakhala ku Debri (mzindawu poyamba unkatchedwa Kiriati Seferi).
12 И рече Халев: Ко савлада Киријат-Сефер и узме га, даћу му Ахсу кћер своју за жену.
Tsono Kalebe anati, “Munthu amene angathire nkhondo mzinda wa Kiriati Seferi ndi kuwulanda, ndidzamupatsa mwana wanga Akisa kuti akhale mkazi wake.”
13 И узе га Готонило, син Кенезов, млађи брат Халевов; и даде му Ахсу кћер своју за жену.
Otanieli mwana wa Kenazi, mngʼono wake wa Kalebe, ndiye anawulanda. Choncho Kalebe anamupatsa mwana wake Akisa kuti akhale mkazi wake.
14 И кад полажаше, наговараше је да иште у оца њеног поље: Па скочи с магарца. А Халев јој рече: Шта ти је?
Tsiku lina atafika Akisayo, Otanieli anamuwumiriza mkazi wakeyo kuti apemphe munda kwa Kalebe abambo ake. Pamene Akisa anatsika pa bulu wake, Kalebe anamufunsa kuti, “Kodi ukufuna ndikuchitire chiyani?”
15 А она му рече: Дај ми дар; кад си ми дао суву земљу, дај ми и изворе водене. И даде јој Халев изворе горње и изворе доње.
Iye anayankha kuti, “Mundikomere mtima. Popeza mwandipatsa ku Negevi, kumalo kumene kulibe madzi, mundipatsenso akasupe amadzi.” Choncho Kalebe anamupatsa akasupe a kumtunda ndi a kumunsi.
16 А и синови Кенеја таста Мојсијевог изиђоше из града палмовог са синовима Јудиним у пустињу Јудину, која је на југу од Арада. И дошавши живљаху с народом.
Tsono zidzukulu za Hobabu, Mkeni uja, mpongozi wa Mose, zinachoka ku Yeriko mzinda wa migwalangwa pamodzi ndi anthu a fuko la Yuda mpaka ku chipululu chimene chili kummwera kwa Aradi ndi kukakhala ndi Aamaleki.
17 Потом изиђе Јуда са Симеуном братом својим, и побише Хананеје који живљаху у Сефату, и раскопаше га, и прозва се град Орма.
Kenaka anthu a fuko la Yuda anapita pamodzi ndi abale awo a fuko la Simeoni ndi kukagonjetsa Akanaani amene amakhala ku Zefati, ndipo mzindawo anawuwononga kwambiri. Choncho mzindawo anawutcha Horima.
18 И Газу узе Јуда с међама њеним, и Аскалон с међама његовим, и Акарон с међама његовим.
Anthu a fuko la Yuda analandanso mzinda wa Gaza ndi dziko lonse lozungulira, mzinda wa Asikeloni pamodzi ndi dziko lake lonse lozungulira, ndi mzinda wa Ekroni pamodzi ndi dziko lonse lozungulira.
19 Јер Господ беше с Јудом, те освоји гору; али не изагна оне који живљаху у долини, јер имаху гвоздена кола.
Yehova anathandiza anthu a fuko la Yuda. Iwo analanda dziko la kumapiri, koma sanathe kuwachotsa anthu ku zigwa, chifukwa anali ndi magaleta azitsulo.
20 И дадоше Халеву Хеврон, као што беше заповедио Мојсије, а он изагна оданде три сина Енакова.
Monga analonjezera Mose, Kalebe anapatsidwa Hebroni. Kalebe anapirikitsa mafuko atatu a Anaki mu mzindamo.
21 А синови Венијаминови не изагнаше Јевусеја који живљаху у Јерусалиму; него Јевусеји осташе у Јерусалиму са синовима Венијаминовим до овог дана.
Koma fuko la Benjamini linalephera kuwachotsa Ayebusi, amene amakhala mu Yerusalemu. Choncho Ayebusiwo akukhalabe ndi fuko la Benjamini mu Yerusalemu mpaka lero.
22 Изиђоше и синови Јосифови на Ветиљ, и Господ беше с њима.
A banja la Yosefe nawonso anathira nkhondo mzinda wa Beteli, ndipo Yehova anali nawo.
23 И уходише Ветиљ синови Јосифови, а име граду беше пре Луз.
Anatumiza anthu kuti akazonde Beteli. Mzindawo kale unkatchedwa Luzi.
24 И уходе видеше човека који иђаше из града и рекоше му: Хајде покажи нам куда ћемо ући у град, па ћемо ти учинити милост.
Anthu okazondawo anaona munthu akutuluka mu mzindamo ndipo anamuwuza kuti, “Tisonyeze njira yolowera mu mzindamu, ndipo ife tidzakuchitira chifundo.”
25 А он им показа куда ће ући у град: и исекоше у граду све оштрим мачем, а оног човека пустише са свом породицом његовом.
Choncho iye anawaonetsa njirayo, ndipo iwo anapha anthu onse mu mzindamo ndi lupanga koma munthu uja pamodzi ndi banja lake sanawaphe.
26 И отиде онај човек у земљу хетејску, и онде сазида град, и прозва га Луз; то му је име до данас.
Ndipo iye anapita ku dziko la Ahiti, kumene anamangako mzinda nawutcha dzina lake Luzi. Mpaka lero lino mzindawo dzina lake ndi lomwelo.
27 А Манасија не изагна становнике из Вет-Сана и села његових, ни из Танаха и села његових, ни становнике из Дора и села његових, ни становнике из Ивлеама и села његових, ни становнике из Мегида и села његових; и Хананеји стадоше живети у тој земљи.
Koma a fuko la Manase sanachotse nzika za mzinda wa Beti-Seani pamodzi ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapena nzika za mzinda wa Taanaki ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapenanso nzika za mzinda wa Dori ndi mʼmidzi yake yozungulira. Iwo sanapirikitse nzika za mzinda wa Ibuleamu ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapena mzinda wa Megido ndi mʼmidzi yake yozungulira. Choncho Akanaani anapitirirabe kukhala mʼdzikomo.
28 А кад ојача Израиљ, удари на Хананеје данак, али их не изагна.
Aisraeli atakhala amphamvu, anawagwiritsa Akanaaniwo ntchito yakalavulagaga, koma sanawapirikitse.
29 Ни Јефрем не изагна Хананеје који живљаху у Гезеру; него осташе Хананеји с њим у Гезеру.
Nawonso Aefereimu sanathamangitse Akanaani amene amakhala mu Gezeri, choncho Akanaaniwo ankakhalabe pakati pawo ku Gezeriko.
30 Завулон не изагна становнике из Китрона, ни становнике из Налола; него осташе Хананеји с њим, и плаћаху данак.
Azebuloni sanathamangitse Akanaani amene amakhala mu Kitironi kapena a ku Nahaloli. Iwo ankakhala pakati pawo ndipo ankawagwiritsa ntchito yakalavulagaga.
31 Асир не изагна становнике из Акона, ни становнике из Сидона ни из Алава, ни из Ахазива, ни из Хелве, ни из Афика, ни из Реова;
A fuko la Aseri nawo sanathamangitse amene amakhala mu Ako, Sidoni, Ahilabu, Akizibu, Heliba, Afiki, ndi Rehobu.
32 Него Асир живљаше међу Хананејима, становницима оне земље, јер их не изагна.
Choncho anthu a fuko la Aseri anakhala pakati pa Akanaani amene ankakhala mʼdzikomo popeza sanawapirikitse.
33 Нефталим не изагна становнике из Вет-Семеса, ни становнике из Вет-Аната; него живљаше међу Хананејима становницима оне земље; и становници у Вет-Семесу и у Вет-Анату плаћаху им данак.
Nalonso fuko la Nafutali silinathamangitse anthu amene ankakhala ku Beti Semesi kapena ku Beti Anati. Koma Anafutaliwo ankakhala pakati pa Akanaaniwo mʼdzikomo. Koma anthu amene ankakhala ku Beti Semesi ndi ku Beti Anati anawasandutsa kukhala ogwira ntchito yathangata.
34 А Амореји притешњаваху синове Данове у гори, и не даваху им силазити у долину.
Aamori anapirikitsira anthu a fuko la Dani ku dziko la ku mapiri popeza sanawalole kuti atsikire ku chigwa.
35 И Амореји стадоше живети у гори Ересу, у Ајалону и у Салвиму; а кад осили рука дома Јосифовог, плаћаше данак.
Aamori anatsimikiza mtima zokhalabe ku phiri la Hara-Heresi, ku Ayaloni, ndiponso ku Saalibimu. Koma a fuko la Yosefe anakula mphamvu ndipo anagwiritsa Aamoriwo ntchito yakalavulagaga.
36 А међа Аморејима беше од горе акравимске, од стене па навише.
Malire a Aamori anayambira ku chikweza cha Akirabimu nʼkulowera ku Sela napitirira kumapita chakumapiri ndithu.

< Књига о судијама 1 >