< Књига о судијама 21 >
1 А синови Израиљеви беху се заклели у Миспи рекавши: Ниједан између нас да не да кћери своје за жену сину Венијаминовом.
Aisraeli anali atalumbira ku Mizipa kuti, “Palibe mmodzi wa ife adzapereke mwana wake wamkazi kuti akwatiwe ndi mwamuna wa fuko la Benjamini.”
2 Зато отиде народ к дому Божјем, и осташе онде до вечери пред Богом, и подигавши глас свој плакаше врло,
Anthu anapita ku Beteli kumene anakakhala pansi pamaso pa Mulungu mpaka madzulo. Iwo anakweza mawu nalira kwambiri.
3 И рекоше: Зашто се, Господе Боже Израиљев, догоди ово у Израиљу, данас да нестане једног племена из Израиља?
Iwo ankanena kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli, nʼchifukwa chiyani izi zachitika mʼdziko la Israeli kuti lero fuko limodzi lisowe mu Israeli?”
4 И сутра дан урани народ, и начини онде олтар, и принесоше жртве паљенице и жртве захвалне.
Mmawa mwake anthu anadzuka namanga guwa lansembe ndi kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano.
5 Тада рекоше синови Израиљеви: Има ли ко да није дошао на збор из свих племена Израиљевих ка Господу? Јер се беху тешко заклели за оног ко не дође у Миспу ка Господу рекавши: Да се погуби.
Kenaka Aisraeli anafunsa kuti, “Kodi ndani pakati pa mafuko a Israeli sanafike ku msonkhano wa Yehova?” Anatero chifukwa anachita malumbiro aakulu okhudza munthu amene alephere kupita ku Mizipa ndi kuti woteroyo ayenera kuphedwa.
6 Јер се синовима Израиљевим сажали за Венијамином братом њиховим, и рекоше: Данас се истреби једно племе из Израиља.
Tsono Aisraeli anamva chisoni chifukwa cha abale awo, Abenjamini. Iwo anati, “Lero fuko limodzi lachotsedwa mu Israeli.
7 Шта ћемо чинити с онима што су остали да би имали жене, кад се заклесмо Господом да им не дамо кћери својих за жене?
Kodi tingawapezere bwanji anthu otsalawa akazi woti awakwatire? Paja ife tinalumbira kwa Yehova kuti sitidzapereka ana anthu aakazi kuti awakwatire.
8 Па рекоше: Има ли ко из племена Израиљевих да није дошао у Миспу ка Господу? И гле, не беше дошао на војску, на збор, нико из Јависа Галадовог.
Kenaka anafunsa kuti, ‘Kodi mu fuko la Israeli ndani amene sanabwere pamaso pa Yehova ku Mizipa?’” Tsono panapezeka kuti panalibe ndi mmodzi yemwe wochokera ku Yabesi Giliyadi amene anapita ku msonkhano ku misasa kuja.
9 Јер кад се народ преброја, гле, не беше онде ниједног од оних који живе у Јавису Галадовом.
Pamene anthu anawerengana anangoona kuti anthu a ku Yabesi Giliyadi palibe.
10 Зато посла збор онамо дванаест хиљада храбрих људи, и заповеди им говорећи: Идите и побијте становнике у Јавису Галадовом оштрим мачем и жене и децу.
Choncho msonkhano unatumiza anthu ankhondo 12,000 ndi kuwalamula kuti, “Mukaphe anthu onse okhala ku Yabesi Giliyadi, kuphatikizapo akazi ndi ana.”
11 Ово ћете дакле учинити: све мушкиње и све женскиње што је познало човека побијте.
Izi ndi zimene mukachite. “Mukaphe mwamuna aliyense ndi mkazi aliyense amene anadziwapo mwamuna.”
12 И нађоше међу становницима Јависа Галадовог четири стотине девојака, које не беху познале човека, и доведоше их у логор у Силом, који је у земљи хананској.
Iwo anapeza atsikana 400 pakati pa anthu okhala mu Yabesi Giliyadi amene anali asanadziwepo mwamuna ndipo anabwera nawo ku misasa ku Silo mʼdziko la Kanaani.
13 Тада посла сав збор, те говорише синовима Венијаминовим који беху у стени Римону, и објавише им мир.
Kenaka msonkhano wonse unatumiza uthenga kwa Abenjamini amene ankakhala ku thanthwe la Rimoni kuwawuza kuti nkhondo yatha.
14 Тако се вратише синови Венијаминови у то време, и дадоше им жене које оставише у животу између жена из Јависа Галадовог; али их не беше доста за њих.
Choncho Abenjamini anabwera nthawi imeneyo ndipo Aisraeli anawapatsa akazi a ku Yabesi Giliyadi amene sanaphedwe. Koma sanapezeke owakwanira.
15 А народу беше жао Венијамина што Господ окрњи племена Израиљева.
Aisraeli anamvera chisoni Abenjamini, chifukwa Yehova anachita ngati waligwerula dzino fuko la Israeli.
16 Па рекоше старешине од збора: Шта ћемо чинити с овима што су остали да би имали жене? Јер су изгинуле жене у племену Венијаминовом.
Choncho akuluakulu a msonkhano anati, “Kodi tikawapezera kuti akazi anthu otsalirawa kuti awakwatire popeza kuti akazi a fuko la Benjamini anaphedwa?”
17 Потом рекоше: Наследство Венијаминово припада онима што су остали, да се не би затрло племе из Израиља.
Iwo anati, “Abenjamini amene anapulumukawa ayenera kukhala ndi zidzukulu, kuti mtundu wa Israeli usafafanizike.
18 А ми им не можемо дати жена између кћери својих; јер су се заклели синови Израиљеви рекавши: Да је проклет ко да жену синовима Венијаминовим.
Ife sitingathe kuwapatsa ana anthu aakazi kuti akwatire. Paja tinalumbira kuti, ‘Akhale wotembereredwa aliyense amene adzapereka mwana wake wamkazi kwa mwamuna wa fuko la Benjamini kuti akwatire.’
19 Потом рекоше: Ево, годишњи је празник Господњи у Силому, који је са севера Ветиљу, к истоку, на путу који иде од Ветиља у Сихем, и с југа Левони.
Ndipo anati, ‘Paja ku Silo kuli chikondwerero cha chaka ndi chaka cholemekeza Yehova. Tsono Silo ali kumpoto kwa Beteli, kummawa kwa msewu wochokera ku Beteli kupita ku Sekemu, ndiponso kummwera kwa Lebona.’”
20 И заповедише синовима Венијаминовим говорећи: Идите, и заседите по виноградима.
Choncho anawalamulira Abenjamini aja kuti, “Pitani mukabisale mʼminda ya mpesa
21 И пазите: Па кад изиђу кћери силомске да играју, изиђите из винограда и отмите сваки себи жену између кћери силомских; и идите у земљу Венијаминову.
ndipo mukakhale tcheru. Ana aakazi a ku Silo akadzatulukira kudzavina nawo magule, pomwepo inu mutuluke minda ya mpesa ndi kukawagwira aliyense wake ndi kupita nawo ku dziko la Benjamini.
22 А кад дођу оци њихови или браћа њихова к нама да се суде, ми ћемо им казати: Смилујте им се нас ради, јер у овом рату нисмо заробили жене за сваког њих; а ви им нисте дали, и тако нећете бити криви.
Ngati abambo awo kapena alongo awo adzabwera kudzadandaula kwa ife, tidzawawuza kuti, ‘Chonde, tikomereni mtima powalola kuti atenga ana anu aakaziwo popeza kuti ife sitinawapezere akazi pomenya nkhondo. Inunso simunachite kuwapatsa. Mukanatero ndiye mukanapalamula.’”
23 Тада синови Венијаминови учинише тако, и доведоше жене према броју свом између играчица које отеше, и отишавши вратише се на наследство своје, и сазидаше опет градове и населише се у њима.
Abenjamini anachitadi zimenezi. Mwa akazi amene ankavina aja anagwirapo ena, malingana ndi chiwerengero chawo, nawatenga kuti akhale akazi awo. Kenaka ananyamuka kubwerera ku dziko la kwawo, nakamanganso mizinda yawo ndi kumakhalamo.
24 И тако разиђоше се синови Израиљеви оданде у оно време сваки у своје племе и у породицу своју, и отидоше оданде сваки на своје наследство.
Pambuyo pake Aisraeli anachoka kumeneko ndi kubwerera kwawo, ku mafuko ndi ku mabanja awo, aliyense ku dera la cholowa chake.
25 У оно време не беше цара у Израиљу; сваки чињаше шта му беше драго.
Masiku amenewo kunalibe mfumu ku Israeli. Aliyense ankangochita zimene zomukomera yekha.