< Књига о судијама 18 >

1 У то време не беше цара у Израиљу, и у то време племе Даново тражаше себи наследство где би наставало, јер му дотада не беше допало наследство међу племенима Израиљевим.
Masiku amenewo munalibe mfumu mu Israeli. Ndipo anthu a fuko la Dani amafunafuna malo okhalamo ngati cholowa chawo, chifukwa kufikira nthawi imeneyo anali asanalandire cholowa chawo pakati pa mafuko a Israeli.
2 Зато послаше синови Данови из породице своје пет људи између себе, храбре људе од Сараје и Естаола, да уходе земљу и добро размотре, и рекоше им: Идите, размотрите земљу. И они отидоше у гору Јефремову у кућу Мишину и заноћише онде.
Choncho fuko la Dani linatumiza kuchokera ku mabanja awo onse anthu olimba mtima asanu. Anthuwa anachokera ku Zora ndi ku Esitaoli ndipo anatumidwa kukazonda ndi kuliyendera dzikolo. Anthu amenewa ankayimira fuko lonse la Dani. Anthuwa anawawuza kuti, “Pitani mukazonde dzikolo.” Anthuwa anafika ku dziko la mapiri la Efereimu ndi kupita ku nyumba ya Mika komwe anakagona.
3 И кад беху код куће Мишине, познаше глас оног младића Левита, и свративши се онамо рекоше му: Ко те доведе овамо? И шта радиш ту? И шта ћеш ту?
Ali ku nyumba ya Mika anazindikira mawu a mnyamata, Mlevi uja. Choncho anapita kwa iye namufunsa kuti, “Unabwera ndi ndani kuno? Nanga ukuchita chiyani ku malo ano? Komanso nʼchifukwa chiyani uli kuno?”
4 А он им рече: Тако и тако учини ми Миха, и најми ме да му будем свештеник.
Iye anawawuza zimene Mika anamuchitira ndipo anati, “Iye anandilemba ntchito ndipo ndine wansembe wake.”
5 А они му рекоше: Упитај Бога да знамо хоће ли нам бити срећан пут на који пођосмо.
Kenaka iwo anati kwa iye, “Chonde tifunsire kwa Mulungu kuti tidziwe ngati ulendo wathuwu tiyende bwino.”
6 А свештеник им рече: Идите с миром; по вољи је Господу пут којим идете.
Wansembeyo anawayankha kuti, “Pitani mu mtendere, Yehova ali ndi inu pa ulendo wanuwu.”
7 И тако пошавши оних пет људи дођоше у Лаис, и видеше тамошњи народ где живи без страха по обичају сидонском, мирно и без страха, и да нема никога у земљи ко би им чим год досађивао или отимао власт, и да су далеко од Сидоњана нити имају шта с ким.
Choncho anthu asanuwo ananyamuka ndipo anafika ku Laisi, kumene anaona kuti anthu ankakhala mwabata monga anthu a ku Sidoni. Anali anthu opanda chowavuta ndiponso aphee. Tsono popeza mʼdziko mwawo analibe chosowa, iwo anali a chuma. Anaonanso kuti anthuwo ankakhala kutali ndi Sidoni ndipo analibe ubale ndi wina aliyense.
8 Па кад се вратише к браћи својој у Сарају и Естаол, рекоше им браћа: Шта је?
Ozonda dziko aja atabwerera kwa abale awo ku Zora ndi Esitaoli, abale awowo anawafunsa kuti, “Mwaonako zotani?”
9 А они рекоше: Устајте да идемо на њих; јер видесмо земљу, и врло је добра. И ви не марите? Немојте се ленити, него похитајте да узмете земљу.
“Tiyeni tikamenyane nawo nkhondo popeza taliona dziko lawolo kuti ndi lachonde kwambiri. Kodi simuchitapo kanthu? Musachite mphwayi kupita mʼdzikomo ndi kukalilanda.
10 Кад дођете, доћи ћете к народу безбрижном и у земљу пространу; јер је предаде Бог у наше руке; то је место где нема недостатака ни у чем што има на земљи.
Mukalowa, mukapeza anthu amene ali osatekeseka ndi dziko lalikulu. Yehova wakupatsani dziko limeneli. Malowo ngosasowa kanthu kalikonse kopezeka pa dziko lapansi.”
11 Тада пођоше оданде из Сараје и Естаола шест стотина људи од породице Данове наоружаних.
Kenaka anthu 600 a fuko la Dani ananyamuka ku Zora ndi Esitaoli atanyamula zida za nkhondo.
12 И отишавши стадоше у логор код Киријат-Јарима у Јуди; зато се прозва оно место Махане-Дан до данас, и јесте иза Киријат-Јарима.
Tsono anakamanga msasa ku Kiriati-Yearimu mʼdziko la Yuda. Malowa ali kumadzulo kwa Kiriati-Yearimu. Ichi ndi chifukwa chake malowo akutchedwa Mahane Dani mpaka lero.
13 А оданде пошавши у гору Јефремову дођоше у кућу Мишину.
Kuchokera kumeneko anapita ku dziko lamapiri la Efereimu ndipo anafika ku nyumba ya Mika.
14 Тада проговорише петорица што беху ишли да уходе земљу лаиску, и рекоше браћи својој: Знате ли да у овим кућама има оплећак и ликови, и лик резан и лик ливен? Сада дакле гледајте шта ћете радити.
Anthu asanu amene anakazonda dziko la Laisi anati kwa abale awo, “Kodi mukudziwa kuti imodzi mwa nyumba izi muli efodi, mafano a mʼnyumba otchedwa terafimu, fano losema ndiponso fano lokuta ndi siliva? Ndiye mudziwe chochita.”
15 А они свративши се онамо уђоше у кућу где беше младић Левит, у кућу Мишину, и упиташе га за здравље.
Choncho anthuwa anapatuka napita ku nyumba ya Mika kumene mnyamata, Mlevi uja ankakhala ndipo anamufunsa za mmene zinthu zilili.
16 А шест стотина људи наоружаних од синова Данових стадоше пред вратима.
Nthawi imeneyi nʼkuti anthu 600 a fuko la Dani aja atayima pa chipata atanyamula zida za nkhondo.
17 А пет људи што беху ишли да уходе земљу отишавши уђоше и узеше лик резан и оплећак и ликове и лик ливен; а свештеник стајаше на вратима са шест стотина људи наоружаних.
Anthu asanu amene anakazonda dziko aja analowa ndi kukatenga fano losema, efodi, fano la mʼnyumba lotchedwa terafimu, ndi fano lokutidwa ndi siliva. Nthawiyi nʼkuti wansembe uja ndi anthu 600 okhala ndi zida za nkhondo aja ali chiyimire pa chipata.
18 И они што уђоше у кућу Мишину кад узеше лик резани, оплећак, ликове и лик ливени, свештеник им рече: Шта радите?
Anthuwo atalowa mʼnyumba ya Mika ndi kutenga fano losema, efodi, fano la mʼnyumba, ndi fano lokutidwa ndi siliva, wansembeyo anawafunsa kuti, “Kodi mukuchita chiyani?”
19 А они му рекоше: Ћути, метни руку на уста, па хајде с нама, и буди нам отац и свештеник. Шта ти је боље, бити свештеник кући једног човека или бити свештеник племену и породици у Израиљу?
Iwo anamuyankha kuti, “Khala chete usayankhule. Tsagana nafe ndipo udzakhala mlangizi wathu ndi wansembe wathu. Kodi si kwabwino kwa iwe kukhala wansembe wa fuko lonse la Israeli mʼmalo mokhala wansembe wa munthu mmodzi yekha?”
20 И свештеник се обрадова у срцу, и узе оплећак и ликове и лик резани, и уђе међу народ.
Wansembeyo anakondwera ndipo anatenga efodi, fano la mʼnyumba ndi fano losema natsagana nawo.
21 И окренувши се пођоше пустивши децу и стоку и закладе напред.
Choncho iwo anatembenuka nachoka, atatsogoza ana, zoweta ndi katundu wawo yense.
22 А кад беху далеко од куће Мишине, онда људи који живљаху у кућама близу куће Мишине скупише се и пођоше у потеру за синовима Дановим.
Atayenda mtunda pangʼono kuchokera pa nyumba ya Mika, anthu amene amakhala pafupi ndi nyumba ya Mika anasonkhana kulondola a fuko la Dani aja, ndipo anawapeza.
23 И викаше за синовима Дановим, а они обазревши се рекоше Миши: Шта ти је, те си скупио толике људе?
Atawafuwulira, a fuko la Dani aja anachewuka ndipo anafunsa Mika kuti, “Chavuta nʼchiyani kuti usonkhanitse anthu chotere?”
24 А он рече: Узели сте моје богове које сам начинио, и свештеника, па отидосте. Шта још имам? Па још кажете: Шта ти је?
Iye anayankha kuti, “Inu mwanditengera milungu imene ndinapanga pamodzi ndi wansembe nʼkumapita. Tsono ine ndatsala ndi chiyani? Ndiye inu mungafunse kuti chavuta nʼchiyani?”
25 А синови Данови рекоше му: Немој да ти се чује глас за нама, да не би ударили на вас људи гневни, те ћеш изгубити душу своју и душу дома свог.
Anthu a fuko la Dani aja anayankha kuti, “Usayankhuleponso kanthu chifukwa anthu awa angapse mtima nakumenya ndipo iwe ndi banja lako lonse nʼkutayapo miyoyo yanu.”
26 И синови Данови отидоше својим путем, а Миха, видећи да су јачи од њега врати се и отиде кући својој.
Choncho anthu a fuko la Dani anapitiriza ulendo wawo. Mika ataona kuti anthuwo anali amphamvu kuposa iye, anangotembenuka kubwerera kwawo.
27 И они узевши шта беше начинио Миха, и свештеника, ког имаше, дођоше у Лаис к народу мирном и безбрижном; па их исекоше оштрим мачем, а град упалише огњем.
Anthu a fuko la Dani aja anatenga zinthu zimene Mika anapanga pamodzi ndi wansembe uja. Iwo anakafika ku Laisi kwa anthu a phee, osatekeseka aja ndipo anawathira nkhondo, nawapha ndi kutentha mzindawo ndi moto.
28 И не беше никога да их избави; јер беху далеко од Сидона и не имаху ништа ни с ким; а град беше у долини која је код Вет-Реова. После сазидаше град и населише се у њему.
Panalibe wowapulumutsa chifukwa anali kutali ndi Sidoni ndiponso sanali pa ubale ndi wina aliyense. Mzindawo unali mʼchigwa cha Beti-Rehobu. Anthu a fuko la Adaniwo anawumanganso mzindawo ndi kumakhalamo.
29 И назваше град Дан по имену Дана оца свог, који се роди Израиљу; а пре се град зваше Лаис.
Iwo anawutcha mzindawo Dani, kutengera dzina la kholo lawo Dani, amene anali mwana wa Israeli, ngakhale kuti mzindawo poyamba unali Laisi.
30 И синови Данови наместише себи онај лик резани; а Јонатан син Гирсона Манасијиног и синови његови беху свештеници племену Дановом докле се год не исели из земље.
Anthu a fuko la Dani anayimiritsa fano losema lija. Yonatani mwana wa Geresomu, mwana wa Mose pamodzi ndi ana ake onse anakhala ansembe a fuko la Dani mpaka pa tsiku la ukapolo wa dzikolo.
31 И намештен им стајаше онај лик резани, који начини Миха, за све време докле дом Божји беше у Силому.
Choncho anthu a fuko la Dani ankapembedza fano limene Mika anapanga nthawi yonse pamene nyumba ya Mulungu inali ku Silo.

< Књига о судијама 18 >