< Књига Исуса Навина 1 >
1 А по смрти Мојсија, слуге Господњег, рече Господ Исусу сину Навином, слузи Мојсијевом, говорећи:
Atamwalira Mose mtumiki wa Mulungu, Yehova anati kwa Yoswa mwana wa Nuni mthandizi wa Mose:
2 Мојсије, слуга мој, умре; зато сада устани, пређи преко тог Јордана ти и сав тај народ у земљу коју ја дајем синовима Израиљевим.
“Mose mtumiki wanga wamwalira. Ndipo iwe ndi anthu onsewa, tsopano konzekani kuwoloka mtsinje wa Yorodani kupita ku dziko limene ndiwapatse Aisraeli onse.
3 Свако место на које ступите стопама својим дао сам вам, као што рекох Мојсију.
Paliponse pamene phazi lanu liponde, ndikupatsani monga momwe ndinalonjezera Mose.
4 Од пустиње и од овог Ливана до реке велике, реке Ефрата, сва земља хетејска до великог мора на западу биће међа ваша.
Dziko lanu lidzayambira ku chipululu kummwera mpaka ku mapiri a Lebanoni kumpoto, kuchokeranso ku mtsinje waukulu wa Yufurate kummawa, mpaka dziko lonse la Ahiti, kukafika ku Nyanja Yayikulu ya kumadzulo.
5 Нико се неће одржати пред тобом свега века твог; са тобом ћу бити као што сам био са Мојсијем, нећу одступити од тебе нити ћу те оставити.
Palibe munthu amene adzatha kukugonjetsa masiku onse a moyo wako. Monga Ine ndinakhalira ndi Mose, chomwechonso ndidzakhala nawe. Sindidzakusiya kapena kukataya.
6 Буди слободан и храбар, јер ћеш ти предати том народу у наследство земљу за коју сам се заклео оцима њиховим да ћу им је дати.
“Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima, chifukwa iwe udzatsogolera anthu awa kukalandira dziko limene Ine ndinalonjeza makolo awo kuti ndidzawapatsa.
7 Само буди слободан и храбар да држиш и твориш све по закону који ти је заповедио Мојсије слуга мој, не одступај од њега ни надесно ни налево, да би напредовао куда год пођеш.
Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima kwambiri. Usamale ndithu kuti umvere malamulo onse amene mtumiki wanga Mose anakupatsa. Usachoke pa malamulo anga ndipo kulikonse kumene udzapite udzapambana.
8 Нека се не раставља од уста твојих књига овог закона, него размишљај о њему дан и ноћ, да држиш и твориш све како је у њему написано; јер ћеш тада бити срећан на путевима својим и тада ћеш напредовати.
Uziwerenga Buku la Malamuloli, uzilingalira zolembedwa mʼmenemo usana ndi usiku, kuti uchite zonse zimene zinalembedwamo. Ukamatero udzapeza bwino ndi kupambana.
9 Нисам ли ти заповедио: Буди слободан и храбар! Не бој се и не плаши се, јер је с тобом Господ Бог твој куда год идеш.
Paja ndinakulamula kuti ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima. Choncho usamachite mantha kapena kutaya mtima popeza Ine Yehova Mulungu wako ndidzakhala nawe kulikonse kumene udzapite.”
10 Тада заповеди Исус управитељима народним говорећи:
Tsono Yoswa analamula atsogoleri a Aisraeli nawawuza kuti,
11 Прођите кроз логор и заповедите народу говорећи: Спремите себи погаче, јер ћете за три дана прећи преко Јордана па уђите и узмите земљу коју вам Господ Бог ваш даје у наследство.
“Pitani ku misasa yonse ndipo muwuze anthu kuti, ‘Konzekani, mangani katundu wanu, popeza pakapita masiku atatu kuyambira lero mudzawoloka Yorodani kupita kukatenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.’”
12 А племену Рувимовом и Гадову и половини племена Манасијиног рече Исус говорећи:
Koma Yoswa anawuza fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase kuti,
13 Сетите се шта вам је заповедио Мојсије, слуга Господњи, рекавши: Господ Бог ваш смири вас и даде вам ову земљу.
“Kumbukirani zimene Mose mtumiki wa Yehova anakulamulani kuti, ‘Yehova Mulungu wanu akukupatsani mpumulo, ndi dziko ili kuti likhale lanu.’
14 Жене ваше, деца ваша и стока ваша нека остану у земљи коју вам даде Мојсије с ове стране Јордана; ви пак прођите под оружјем пред браћом својом, који сте год за војску, и помозите им,
Tsono akazi anu, ana anu ndi ziweto zanu zitsale mʼdziko lino limene Mose anakupatsani kummawa kwa Yorodani. Koma ankhondo anu okha ndiwo awoloke atatenga zida zawo ndi kupita patsogolo pa abale anu kukawathandiza.
15 Докле не смири Господ и браћу вашу као вас, и наследе и они земљу коју им даје Господ Бог ваш; па се онда вратите на наследство своје које вам је дао Мојсије, слуга Господњи, с оне стране Јордана, ка истоку, и држите га.
Abale anuwo akadzalandira dziko limene Yehova Mulungu wanu akuwapatsa monga inu mwachitira, inu mudzabwerera kudzakhazikika mʼdziko lanu limene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani tsidya la kummawa kwa Yorodani.”
16 А они одговорише Исусу говорећи: Шта си нам год заповедио чинићемо, и куда нас год пошаљеш ићи ћемо.
Kenaka iwo anayankha Yoswa kuti, “Ife tidzachita chilichonse chimene mwatilamula, ndipo kulikonse kumene mudzatitume tidzapita.
17 Слушаћемо те како смо слушали Мојсија; само нека Господ Бог твој буде с тобом као што је био с Мојсијем.
Monga momwe tinamvera Mose kwathunthu, chomwechonso tidzakumvera iwe. Yehova Mulungu wanu akhale nanu monga momwe anachitira ndi Mose.
18 Ко би се противио твојој заповести и не би слушао речи твоје у свему што му заповедиш, нека се погуби; само буди слободан и храбар.
Aliyense wotsutsana ndi inu kapena wosamvera zimene mutilamula adzaphedwa. Inu mukhale wamphamvu ndi wolimba mtima!”