< Књига о Јову 19 >
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 Докле ћете мучити душу моју и сатирати ме речима?
“Kodi mudzakhala mukundizunza mpaka liti, ndi kundilasa ndi mawu anuwo?
3 Већ сте ме десет пута наружили; није вас стид што тако наваљујете на ме?
Inuyo mwandinyoza kwambiri; mwanditsutsa mopanda manyazi.
4 Али ако сам доиста погрешио, погрешка ће моја остати код мене.
Ngati ndi zoona kuti ine ndasochera, cholakwachotu nʼchanga.
5 Ако ли се још хоћете да дижете на ме и да ме корите мојом срамотом,
Ngati ndithudi mukudziyika nokha pamwamba panga, ndi kugwiritsa ntchito kunyozedwa kwanga polimbana nane,
6 Онда знајте да ме је Бог оборио и мрежу своју разапео око мене.
pamenepa dziwani kuti Mulungu wandilakwira ndipo wandizinga ukonde wake.
7 Ето, вичем на неправду, али се не слушам; вапим, али нема суда.
“Ngakhale ndifuwule kuti, ‘Akundizunza!’ Palibe wondiyankha; ngakhale ndipemphe thandizo, palibe wondichitira zolungama.
8 Заградио је пут мој да не могу проћи; на стазе моје метнуо је мрак.
Mulungu wanditsekera njira yanga kotero sindingathe kudutsa; waphimba njira zanga ndi mdima.
9 Свукао је с мене славу моју и скинуо венац с главе моје.
Iye wandilanda ulemu wanga ndipo wandivula chipewa chaufumu pamutu panga.
10 Порушио ме је од свуда, да ме нема; и као дрво ишчупао је надање моје.
Wandiphwanyaphwanya mbali zonse ndipo ndatheratu; Iye wazula chiyembekezo changa ngati mtengo.
11 Распалио се на ме гнев Његов, и узео ме је међу непријатеље своје.
Wandikwiyira ndipo akundiyesa mmodzi mwa adani ake.
12 Војске Његове дођоше све заједно и насуше к себи пут к мени, стадоше у логор около шатора мог.
Ankhondo ake akubwera kwa ine mwamphamvu, akonzekera zodzalimbana nane ndipo azungulira nyumba yanga.
13 Браћу моју удаљио је од мене, и знанци моји туђе се од мене.
“Mulungu wandisiyanitsa ndi abale anga; wasandutsa odziwana nane kukhala achilendo kwa ine.
14 Ближњи моји оставише ме, и знанци моји заборавише ме.
Abale anga andithawa; abwenzi anga andiyiwala.
15 Домашњи моји и моје слушкиње гледају ме као туђина; странац сам у очима њиховим.
Anthu odzacheza ku nyumba kwanga ndiponso antchito anga aakazi andisandutsa mlendo; ndasanduka mlendo mʼmaso mwawo.
16 Зовем слугу свог, а он се не одзива, а молим га устима својим.
Ndikayitana wa ntchito wanga, iye sandiyankha, ngakhale ndikapempha ndi pakamwa panga sandichitira kanthu.
17 Дах је мој мрзак жени мојој, а преклињем је синовима утробе своје.
Mpweya wanga umamunyansa mkazi wanga; ndine chinthu chonyansa kwa abale anga a mimba imodzi.
18 Ни деца не хају за ме; кад устанем, руже ме.
Inde, ngakhale ana amandinyoza; akandiona amandinyodola.
19 Мрзак сам свима неверним својим, и које љубљах посташе ми противници.
Anzanga onse apamtima amanyansidwa nane; iwo amene ndinkawakonda andiwukira.
20 За кожу моју као за месо моје прионуше кости моје; једва оста кожа око зуба мојих.
Ndangotsala khungu ndi mafupa okhaokha; ndapulumuka lokumbakumba.
21 Смилујте се на ме, смилујте се на ме, пријатељи моји, јер се рука Божија дотакла мене.
“Mvereni chisoni, inu abwenzi anga, mvereni chisoni, pakuti dzanja la Mulungu landikantha.
22 Зашто ме гоните као Бог, и меса мог не можете да се наситите?
Chifukwa chiyani mukundilondola ngati Mulungu? Kodi simunatope nalo thupi langa?
23 О кад би се написале речи моје! Кад би се ставиле у књигу!
“Aa, achikhala mawu anga analembedwa, achikhala analembedwa mʼbuku,
24 Писаљком гвозденом и оловом на камену за вечни спомен кад би се урезале!
akanalembedwa pa mwala ndi chitsulo, akanalembedwa pa thanthwe kuti sangathe kufufutidwa!
25 Али знам да је жив мој Искупитељ, и на последак да ће стати над прахом.
Koma ndikudziwa kuti mpulumutsi wanga ali ndi moyo, ndipo pa nthawi yomaliza adzabwera kudzanditeteza.
26 И ако се ова кожа моја и рашчини, опет ћу у телу свом видети Бога.
Ndipo khungu langa litatha nʼkuwonongeka, mʼthupi langa lomweli ndidzamuona Mulungu.
27 Ја исти видећу Га, и очи моје гледаће Га, а не друге. А бубрега мојих нестаје у мени.
Ine ndemwe ndidzamuona Iye ndi maso angawa, ineyo, osati wina ayi. Ndithu mtima wanga ukufunitsitsadi!
28 Него би требало да кажете: Зашто га гонимо? Кад је корен беседе у мени.
“Koma inu mukuti, ‘Haa! Tingamuzunze bwanji, popeza kuti zonsezi zaoneka chifukwa cha iye yemweyo?’
29 Бојте се мача; јер је мач освета за безакоње; и знајте да има суд.
Inu muyenera kuopa lupanga; pakuti mkwiyo wake umalangadi ndi lupanga; zikadzatero muzadziwa kuti chiweruzo chilipo ndithu.”