< Књига пророка Јеремије 8 >

1 У то време, говори Господ, извадиће се из гробова кости царева Јудиних и кости кнезова његових и кости свештеничке и кости пророчке, и кости становника јерусалимских;
Yehova akuti, “‘Pa nthawi imeneyo, mafupa a mafumu ndi a akuluakulu a ku Yuda, mafupa a ansembe ndi a aneneri, ndiponso mafupa a anthu a ku Yerusalemu adzafukulidwa.
2 И разметнуће се према сунцу и месецу и свој војсци небеској, које љубише и којима служише и за којима идоше и које тражише и којима се клањаше; неће се покупити ни погрепсти, него ће бити гној по земљи.
Adzawamwaza pa nthaka kuyangʼana dzuwa, mwezi ndi nyenyezi zonse zamlengalenga, zimene ankazikonda, kuzitumikira ndi kuzitsatira, kupemphako nzeru ndiponso kuzilambira. Mafupawo sadzawasonkhanitsa kapena kuwakwirira, koma adzakhala ngati ndowe pamwamba pa nthaka.
3 И волеће смрт него живот, сав остатак што их остане од овог рода злог, што их остане по свим местима куда их раселим, говори Господ над војскама.
Otsala onse a mtundu woyipawu adzafuna imfa kopambana moyo kulikonse kumene ndidzawapirikitsirako, akutero Yehova Wamphamvuzonse.’”
4 Још им реци: Овако вели Господ: Ко падне, не устаје ли? Ко зађе, не враћа ли се?
“Tsono awuze anthuwa, ‘Yehova akuti: “‘Kodi anthu akagwa sangadzukenso? Munthu akasochera kodi sangathe kubwereranso?
5 Зашто је зашао тај народ јерусалимски за свагда? Држе се преваре, неће да се обрате.
Chifukwa chiyani nanga anthu awa akupitirirabe kuchimwa, osabwerera? Chifukwa chiyani Yerusalemu akubwerera mʼmbuyo? Iwo akangamira chinyengo; akukana kubwerera.
6 Пазио сам и слушао, не говоре право, нема никога да се каје за зло своје, да рече: Шта учиних? Сваки је окренуо својим трком, као коњ кад нагне у бој.
Ine ndinatchera khutu kumvetsera koma iwo sanayankhulepo zoona. Palibe woyipa amene analapapo zoyipa zake, nʼkumati, ‘Ine ndachita chiyani?’ Aliyense akutsatira njira yake ngati kavalo wothamangira nkhondo.
7 И рода под небом зна своје време, грлица и ждрал и ласта пазе на време кад долазе; а народ мој не зна суд Господњи.
Mbalame yotchedwa kakowa ija imadziwa nthawi yake mlengalenga. Koma nkhunda, namzeze ndi chingalu zimadziwa nthawi yonyamukira ulendo, koma anthu anga sadziwa malamulo a Yehova.
8 Како говорите: Мудри смо, и закон је Господњи у нас? Доиста, гле, лаж учини лажљива писаљка књижевничка.
“‘Inu mukunena bwanji kuti, ‘Ndife anzeru ndipo timasunga malamulo a Yehova?’ Koma ndi alembi anu amene akulemba zabodza.
9 Мудраци се осрамотише, уплашише се и ухватише се; ето, одбацише реч Господњу, па каква им је мудрост?
Anthu anzeru achita manyazi; athedwa nzeru ndipo agwidwa. Iwo anakana mawu a Yehova. Nanga tsono nzeru zawo ziwapinduliranji?
10 Зато ћу дати жене њихове другима, њиве њихове онима који ће их наследити, јер од малог до великог сви се дадоше на лакомство, и пророци и свештеници, сви су варалице.
Nʼchifukwa chake akazi awo ndidzawapereka kwa amuna ena ndipo minda yawo ndidzayipereka kwa amene adzawagonjetse. Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, onse ali ndi khalidwe lofuna kupeza chuma mwakuba. Aneneri pamodzi ndi ansembe omwe, onse amachita zachinyengo.
11 Јер лече ране кћери народа мог овлаш говорећи: Мир, мир; а мира нема.
Iwo amapoletsa zilonda za anthu anga pamwamba chabe nʼkumati, ‘Mtendere, mtendere,’ pamene palibe mtendere.
12 Еда ли се постидеше што чинише гад? Нити се постидеше нити знају за стид; за то ће попадати међу онима који падају; кад их походим, попадаће, вели Господ.
Kodi amachita manyazi akamachita zonyansazi? Ayi, alibe manyazi ndi pangʼono pomwe; iwo sadziwa nʼkugwetsa nkhope komwe. Choncho iwo adzagwera pakati pa anzawo amene agwa kale; adzagwa pansi tsiku limene ndidzawalanga, akutero Yehova.
13 Сасвим ћу их истребити, говори Господ, нема грозда на лози, ни смокве на дрвету, и лишће је опало; и шта сам им дао узеће им се.
“‘Ndidzatenga zokolola zawo, Sipadzakhalanso mphesa pa mpesa kapena nkhuyu pa mkuyu, ndipo masamba ake adzawuma. Zinthu zimene ndinawapatsa ndidzawachotsera.’”
14 Што стојимо? Скупите се и уђимо у тврде градове, и онде ћутимо; јер нас је Господ Бог наш ућуткао напојивши нас жучи, јер згрешисмо Господу.
Koma amati, “Tikukhala pano chifukwa chiyani? Tiyeni tonse pamodzi tithawire ku mizinda yotetezedwa ndi kukafera kumeneko. Pakuti Yehova Mulungu wathu watsimikiza kuti tiyenera kufa. Watipatsa madzi aululu kuti timwe, chifukwa tamuchimwira.
15 Чекасмо мир, али нема добра; и време да оздравимо, а гле, страх.
Tinkayembekezera mtendere koma palibe chabwino chomwe chinachitika, tinkayembekezera kuchira koma tinakumana ndi zoopsa zokhazokha.
16 Од Дана чу се фркање коња његових, од рзања пастуха његових сва се земља затресе, дођоше и поједоше земљу и све што беше у њој, градове и који живљаху у њима.
Kulira kwa ngʼombe zazimuna za mdani kukumveka kuchokera ku Dani; dziko lonse likunjenjemera chifukwa cha kulira kwa akavalowo. Akubwera kudzawononga dziko ndi zonse zimene zili mʼmenemo. Adzawononga mzinda ndi onse okhalamo.”
17 Јер, ево, ја ћу пустити на вас змије, аспиде, од којих нема бајања, те ће вас уједати, говори Господ.
Yehova akuti, “Onani, ndikukutumizirani njoka zaululu, mphiri zimene munthu sangathe kuzilodza, ndipo zidzakulumani,”
18 Окрепио бих се у жалости, али је срце у мени изнемогло.
Ndadzazidwa ndi chisoni kwambiri, mtima wanga walefukiratu.
19 Ето вике кћери народа мог из далеке земље: Зар Господ није у Сиону? Цар његов зар није у њему? Зашто ме разгневише својим ликовима резаним, туђим таштинама?
Imvani kulira kwa anthu anga kuchokera ku dziko lakutali: akuti, “Kodi Yehova sali ku Ziyoni? Kodi mfumu yake sili kumeneko?” “Chifukwa chiyani akundiputa ndi mafano awo osema, ndi milungu yawo yachilendo?”
20 Жетва је прошла, лето минуло, а ми се не избависмо.
“Nthawi yokolola yapita, chilimwe chapita, koma sitinapulumuke.”
21 Сатрвен сам што је кћи народа мог сатрвена, у жалости сам, чудо освоји ме.
Chifukwa cha mavuto a anthu anga, ine ndikumva kuwawa; ndikungolira ndipo mantha aakulu andigwira.
22 Нема ли балсама у Галаду? Нема ли онде лекара? Зашто се дакле не исцели кћи народа мог?
Kodi ku Giliyadi kulibe mankhwala ochiritsa? Kodi kumeneko kulibe singʼanga? Nanga chifukwa chiyani mabala a anthu anga sanapole?

< Књига пророка Јеремије 8 >