< Књига пророка Јеремије 52 >

1 Двадесет и једна година беше Седекији кад поче царовати, и царова једанаест година у Јерусалиму. Матери му беше име Амутала, кћи Јеремијина, из Ливне.
Zedekiya anali wa zaka 21 pamene analowa ufumu, ndipo analamulira zaka 11 ku Yerusalemu. Amayi ake anali Hamutali mwana wa Yeremiya wa ku Libina.
2 Он чињаше што је зло пред Господом сасвим како је чинио Јоаким.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Yehoyakimu.
3 Јер од гнева Господњег зби се Јерусалиму и Јуди, те их одбаци испред себе. А Седекија се одметну од цара вавилонског.
Chifukwa cha zonse zimene zinachitika ku Yerusalemu ndi ku Yuda Yehova anakwiyira anthu ake mpaka kuwachotsa pamaso pake. Tsono Zedekiya anawukira mfumu ya ku Babuloni.
4 И тако, девете године његова царовања, десетог дана дође Навуходоносор цар вавилонски са свом војском својом на Јерусалим; и стадоше у логор под њим, и начинише опкопе око њега.
Choncho mʼchaka cha chisanu ndi chinayi cha ulamuliro wa Zedekiya, mwezi wakhumi, pa tsiku la khumi, Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni anabwera ndi ankhondo ake onse kudzathira nkhondo Yerusalemu. Anamanga misasa ndi mitumbira yankhondo kunja kuzungulira mzindawo.
5 И град би опкољен до једанаесте године царовања Седекијиног.
Mzindawo unazingidwa mpaka chaka cha khumi ndi chimodzi cha ulamuliro wa Mfumu Zedekiya.
6 И деветог дана, четвртог месеца, наста велика глад у граду, те народ земаљски немаше хлеба.
Pa tsiku lachisanu ndi chinayi la mwezi wachinayi njala inakula kwambiri mu mzindamo kotero kuti munalibe chakudya choti anthu nʼkudya.
7 Тада град би проваљен, и војници сви побегоше и изиђоше из града ноћу на врата између два зида уз врт царев, а Халдејци беху свуда око града; и отидоше путем к пустињи.
Tsono linga la mzindawo linabowoledwa, ndipo ankhondo onse anathawa. Iwo anatuluka mu mzindamo usiku kudzera pa chipata cha pakati pa makoma awiri a pafupi ndi munda wa mfumu, ngakhale kuti Ababuloni anali atazinga mzindawo. Ndipo anathawira ku Araba,
8 Али војска халдејска потера цара, и стигоше Седекију у пољу јерихонском, а сва војска што беше с њим разбеже се од њега.
koma gulu la ankhondo la ku Babuloni linalondola mfumu Zedekiya ndi kumupeza mʼchigwa cha ku Yeriko. Ankhondo onse anamusiya yekha nabalalika.
9 И ухватише цара и одведоше га к цару вавилонском у Ривлу у земљи ематској; и онде му суди.
Anagwidwa napita naye kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula mʼdziko la Hamati, kumene anagamula mlandu wake.
10 И покла цар вавилонски синове Седекијине на његове очи, и све кнезове Јудине покла у Ривли.
Ku Ribulako mfumu ya ku Babuloni inapha ana aamuna a Zedekiya iyeyo akuona; ndiponso inapha akuluakulu onse a ku Yuda.
11 И Седекији ископа очи, и свезав га у двоје вериге бронзане одведе га цар вавилонски у Вавилон и метну га у тамницу где оста до смрти своје.
Ndipo inamukolowola maso Zedekiya, ndi kumumanga ndi maunyolo a mkuwa nʼkupita naye ku Babuloni kumene inakamuyika mʼndende kuti akhalemo moyo wake wonse.
12 А десетог дана петог месеца године деветнаесте царовања Навуходоносора цара вавилонског дође у Јерусалим Невузардан, заповедник стражарски, који служаше цару вавилонском.
Mwezi wachisanu, pa tsiku lakhumi, chaka cha 19 cha ulamuliro wa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo a mfumu, amene amatumikira mfumu ya ku Babuloni, anabwera ku Yerusalemu.
13 И попали дом Господњи и дом царски и све домове у јерусалиму; све велике куће попали огњем.
Ndipo anatentha Nyumba ya Yehova, nyumba ya mfumu ndi nyumba zonse za mu Yerusalemu. Anatentha nyumba iliyonse.
14 И све зидове јерусалимске у наоколо развали сва војска халдејска што беше са заповедником стражарским.
Tsono gulu lonse lankhondo la Ababuloni limene linali ndi mtsogoleri wa ankhondo a mfumu uja linagwetsa malinga onse ozungulira Yerusalemu.
15 А народ сиромашни и остатак народа што оста у граду, и пребеге што пребегоше к цару вавилонском, и остали прости народ, одведе Невузардан, заповедник стражарски.
Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo anatenga anthu amene anatsala mu mzindamo, anthu aluso pamodzi ndi amene anadzipereka kale kwa mfumu ya ku Babuloni kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
16 Само од сиромашног народа у земљи остави Невузардан заповедник стражарски који ће бити виноградари и ратари.
Komabe Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo anasiya anthu ena onse osaukitsitsa a mʼdzikomo kuti azigwira ntchito mʼminda ya mpesa ndi minda ina.
17 И ступове бронзане што беху у дому Господњем, и подножја и море бронзано које беше у дому Господњем, изломише Халдејци, и бронзу од њих однесоше у Вавилон.
Ababuloni anaphwanya nsanamira za mkuwa, maphaka ndi chimbiya chamkuwa zimene zinali mʼNyumba ya Yehova. Anatenga mkuwa wonsewo nʼkupita nazo ku Babuloni.
18 И лонце и лопате и виљушке и котлиће и кадионице и све све судове бронзане којима служаху, узеше.
Ankhondowo anatenganso mbiya, zochotsera phulusa, zozimitsira nyale, mbale zofukizira lubani, zikho pamodzi ndi ziwiya zina zonse za mkuwa zimene ankagwiritsira ntchito mʼNyumba ya Yehova.
19 И умиваонице и клешта с котлићима и лонцима и свећњацима и кадионицама и чашама, шта год беше златно и шта год беше сребрно, узе заповедник стражарски.
Nebuzaradani uja anatenganso mabeseni, ziwiya zosonkhapo moto, mbale zowazira madzi, zoyikapo nyale, zipande zofukizira lubani ndi zikho ndi zina zonse zagolide ndi siliva.
20 Два ступа, једно море, и дванаест волова бронзаних што беху под подножјима, што начини цар Соломун за дом Господњи, не беше мере бронзи од свих тих судова.
Nsanamira ziwiri zija, chimbiya, maphaka ndi ngʼombe khumi ndi ziwiri za mkuwa zochirikizira chimbiyacho zimene mfumu Solomoni anapangira Nyumba ya Yehova kulemera kwake kunali kosawerengeka.
21 А ступови беху сваки од осамнаест лаката у висину, а у наоколо од дванаест лаката, а четири прста беше сваки дебео и шупаљ;
Nsanamira imodzi kutalika kwake kunali mamita asanu ndi atatu, akazunguliza chingwe inali mamita asanu ndi theka; mʼkati mwake munali bowo ndipo kuchindikala kwake kunali zala zinayi.
22 И озго на њему беше оглавље бронзано, и оглавље беше високо пет лаката, и плетеница и шипци око оглавља, све од бронзе; такав беше и други ступ са шипцима.
Pamwamba pa nsanamira iliyonse panali mutu wamkuwa umene kutalika kwake kunali mamita awiri. Pozungulira pake panali ukonde ndi makangadza, zonsezo za mkuwa. Nsanamira inayo inalinso ndi makangadza ake ndipo inali yofanana ndi inzake ija.
23 И беше деведесет и шест шипака са сваке стране; свега шипака на плетеници у наоколо беше сто.
Mʼmbali mwake munali makangadza 96; makangadza onse pamodzi analipo 100 kuzungulira ukonde onse.
24 Узе заповедник стражарски и Серају, првог свештеника, и Софонију, другог свештеника, и три вратара.
Mtsogoleri wa ankhondo uja, anagwira Seraya mkulu wa ansembe ndi Zefaniya, wachiwiri wa mkulu wa ansembe ndi alonda atatu apachipata.
25 А из града узе једног дворанина, који беше над војницима, и седам људи који стајаху пред царем, који се нађоше у граду, и првог писара војничког, који пописиваше народ по земљи у војску, и шездесет људи из народа земаљског, који се нађоше у граду.
Mu mzindamo anagwiramo mkulu amene ankalamulira ankhondo, ndi alangizi amfumu asanu ndi awiri. Anagwiranso mlembi wa mtsogoleri wa ankhondo, amene ankalemba anthu mʼdzikomo, pamodzi ndi anthu ena 60 amene anali mu mzindamo.
26 Узе их Невузардан заповедник стражарски и одведе к цару вавилонском у Ривлу.
Nebuzaradani, mtsogoleri wa ankhondoyo anawatenga onse napita nawo kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula.
27 А цар их вавилонски поби и погуби у Ривли у земљи ематској. Тако би пресељен Јуда из земље своје.
Ku Ribulako, mʼdziko la Hamati, mfumu ya ku Babuloniyo inalamula kuti anthuwo aphedwe. Motero anthu a ku Yuda anapita ku ukapolo, kutali ndi dziko lawo.
28 Ово је народ што га пресели Навуходоносор: седме године три хиљаде и двадесет и три Јудејца;
Chiwerengero cha anthu amene Nebukadinezara anawatenga kupita nawo ku ukapolo ndi ichi: Mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri cha ulamuliro wake, anatenga Ayuda 3,023;
29 Године осамнаесте Навуходоносорове пресели из Јерусалима осам стотина и тридесет и две душе;
mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Nebukadinezara, anatenga anthu 832 kuchokera mu Yerusalemu;
30 Године двадесет треће Навуходоносорове пресели Невузардан заповедник стражарски Јудејаца седам стотина и четрдесет и пет душа; свега четири хиљаде и шест стотина душа.
mʼchaka cha 23 cha ulamuliro wa Nebukadinezara, Nebuzaradani, mtsogoleri wa ankhondo a mfumu anagwira Ayuda 745 kupita ku ukapolo. Onse pamodzi analipo anthu 4,600.
31 А тридесет седме године од како се зароби Јоахин цар Јудин, дванаестог месеца, двадесет петог дана, Евил-Меродах цар вавилонски исте године зацаривши се извади из тамнице Јоахина, цара Јудиног.
Mʼchaka chimene Evili-Merodaki analowa ufumu wa Babuloni, iye anakomera mtima Yehoyakini mfumu ya ku Yuda, namutulutsa mʼndende. Izi zinachitika pa tsiku la 25 la mwezi wa khumi ndi chiwiri zitatha zaka 37 chitengedwere Yehoyakimu ku ukapolo.
32 И лепо говори с њим, и намести му престо више престола других царева који беху код њега у Вавилону.
Evili-Merodaki anakomera mtima Yehoyakini, namupatsa malo aulemu kuposa mafumu ena amene anali naye ku Babuloni.
33 И промени му хаљине тамничке, и он јеђаше свагда с њим свега века свог.
Choncho Yehoyakini analoledwa kuvula zovala zake za ku ndende ndipo tsiku ndi tsiku ankadya ndi mfumu pa moyo wake wonse.
34 И храна му се једнако даваше од цара вавилонског, сваки дан, свега века његовог до смрти његове.
Tsiku ndi tsiku mfumu ya ku Babuloni inkamupatsa Yehoyakini phoso lake nthawi yonse ya moyo wake, mpaka pa nthawi ya imfa yake.

< Књига пророка Јеремије 52 >