< Књига пророка Исаије 63 >
1 Ко је оно што иде из Едома, из Восора, у црвеним хаљинама? Красно одевен, корачајући у величини силе своје? Ја сам, који говорим правду и вредан сам спасти.
Kodi ndani uyo akubwera kuchokera ku Edomu, atavala zovala za ku Bozira za madontho ofiira? Kodi uyu ndani, amene wavala zovala zokongola, akuyenda mwa mphamvu zake? “Ndi Ineyo, woyankhula zachilungamo ndiponso wamphamvu zopulumutsa.”
2 Зашто Ти је црвено одело и хаљине Ти као у оног који гази у каци?
Nanga bwanji zovala zanu zili psuu, ngati za munthu wofinya mphesa?
3 Газих сам у каци, и нико између народа не беше са мном; али их изгазих у гневу свом и потлачих у љутини својој; и крв њихова попрска ми хаљине и искаљах све одело своје.
“Ndapondereza ndekha anthu a mitundu ina ngati mphesa, palibe ndi mmodzi yemwe anali nane. Ndinawapondereza ndili wokwiya ndipo ndinawapondereza ndili ndi ukali; magazi awo anadothera pa zovala zanga, ndipo zovala zanga zonse zinathimbirira.
4 Јер је дан од освете у срцу мом, и дође година да се моји искупе.
Pakuti ndinatsimikiza mu mtima mwanga kuti lafika tsiku lolipsira anthu anga; ndipo chaka cha kuwomboledwa kwanga chafika.
5 Погледах, а никога не беше да помогне, и зачудих се што никога не беше да подупре; али ме десница моја избави и јарост моја подупре ме.
Ndinayangʼana ndipo panalibe munthu wondithandiza. Ndinadabwa kwambiri kuti panalibe wondichirikiza; choncho ndinapambana ndi mphamvu zanga, ndipo mkwiyo wanga unandilimbitsa.
6 И изгазих народе у гневу свом, и опојих их јарошћу својом, и пролих на земљу крв њихову.
Ndinapondereza mitundu ya anthu ndili wokwiya; ndipo ndinawasakaza ndipo ndinathira magazi awo pansi.”
7 Помињаћу доброту Господњу, хвалу Господњу за све што нам је учинио Господ, и мноштво добра што је учинио дому Израиљевом по милости својој и по великој доброти својој.
Ndidzafotokoza za kukoma mtima kwa Yehova, ntchito zimene Iye ayenera kutamandidwa. Ndidzatamanda Yehova chifukwa cha zonse zimene watichitira. Inde, mwa chifundo ndi kukoma mtima kwake Yehova wachitira nyumba ya Israeli zinthu zabwino zambiri.
8 Јер рече: Доиста су мој народ, синови, који неће изневерити. И би им Спаситељ.
Yehova anati, “Ndithu awa ndi anthu anga, ana anga amene sadzandinyenga Ine.” Choncho anawapulumutsa.
9 У свакој тузи њиховој Он беше тужан, и анђео, који је пред Њим, спасе их. Љубави своје ради и милости своје ради Он их избави, и подиже их и носи их све време.
Iyenso anasautsidwa mʼmasautso awo onse, ndipo mngelo wochokera kwa Iye anawapulumutsa. Mwa chikondi ndi chifundo chake iye anawapulumutsa, anawanyamula ndikuwatenga kuyambira kale lomwe.
10 Али се одметаше и жалостише Свети Дух Његов; зато им поста непријатељ, и ратова на њих.
Komabe iwo anawukira ndi kumvetsa chisoni Mzimu Woyera. Motero Yehova anatembenuka nakhala mdani wawo ndipo Iye mwini anamenyana nawo.
11 Али се опомену старих времена, Мојсија, народа свог: где је Онај који их изведе из мора с пастиром стада свог? Где је Онај што метну усред њих Свети Дух свој?
Pamenepo anthu ake anakumbukira masiku amakedzana, masiku a Mose mtumiki wake; ndipo anafunsa kuti, “Ali kuti Yehova amene anawawolotsa pa nyanja, pamodzi ndi Mose mʼbusa wawo? Ali kuti Iye amene anayika Mzimu Woyera pakati pawo?
12 Који их води славном мишицом својом за десницу Мојсијеву? Који раздвоји воду пред њима, да стече себи вечно име?
Ali kuti amene anachita zinthu zodabwitsa ndi mphamvu zake zazikulu kudzera mwa Mose? Ali kuti amene anagawa madzi pa nyanja anthu ake akuona, kuti dzina lake limveke mpaka muyaya,
13 Који их води преко бездана као коња преко пустиње, да се не спотакоше?
amene anawayendetsa pa nyanja yozama? Monga kavalo woyendayenda mʼchipululu, iwo sanapunthwe;
14 Дух Господњи води их тихо, као кад стока силази у долину; тако си водио свој народ да стечеш себи славно име.
Mzimu Woyera unawapumulitsa ngati mmene ngʼombe zimapumulira. Umu ndi mmene Inu munatsogolera anthu anu kuti dzina lanu lilemekezeke.”
15 Погледај с неба, и види из стана светиње своје и славе своје, где је ревност Твоја и сила Твоја, мноштво милосрђа Твог и милости Твоје? Еда ли ће се мени устегнути?
Inu Yehova amene muli kumwambako, pa mpando wanu wolemekezeka, wopatulika ndi waulemerero, tiyangʼaneni ife. Kodi changu chanu ndi mphamvu zanu zili kuti? Simukutionetsanso kukoma mtima kwanu ndi chifundo chanu.
16 Ти си заиста Отац наш, ако и не зна Аврам за нас, и Израиљ нас не познаје; Ти си, Господе, Отац наш, име Ти је, откако је века, Избавитељ наш.
Koma Inu ndinu Atate athu, ngakhale Abrahamu satidziwa kapena Israeli kutivomereza ife; Inu Yehova, ndinu Atate athu, kuyambira kale dzina lanu ndinu Mpulumutsi wathu.
17 Зашто си нам дао да зађемо, Господе, с путева Твојих? Да нам отврдне срце да Те се не бојимо? Врати се ради слуга својих, ради племена наследства свог.
Chifukwa chiyani, Inu Yehova, mukutisocheretsa pa njira zanu? Bwanji mukutilola kuti tikhale owuma mitima kotero kuti sitikukuopaninso? Bwererani chifukwa cha atumiki anu; mafuko a anthu amene ali cholowa chanu.
18 Замало наследи народ светости Твоје; непријатељи наши погазише светињу Твоју.
Anthu anu atangokhala pa malo anu opatulika pa kanthawi kochepa, adani athu anasakaza malo anu opatulika.
19 Постасмо као они којима ниси никада владао нити је призивано име Твоје над њима.
Ife tili ngati anthu amene simunawalamulirepo ngati iwo amene sanakhalepo anthu anu.