< Књига пророка Исаије 55 >

1 Ој жедни који сте год, ходите на воду, и који немате новца, ходите, купујте и једите; ходите, купујте без новца и без плате вино и млеко.
“Bwerani, inu nonse amene muli ndi ludzu, bwerani madzi alipo; ndipo inu amene mulibe ndalama bwerani, mudzagule chakudya kuti mudye! Bwerani mudzagule vinyo ndi mkaka osalipira ndalama, osalipira chilichonse.
2 Зашто трошите новце своје на оно што није храна, и труд свој на оно што не сити? Слушајте ме, па ћете јести шта је добро, и душа ће се ваша насладити претилине.
Chifukwa chiyani ndalama zanu mukuwonongera zinthu zimene samadya, ndipo mukuwononga malipiro anu pa zinthu zimene sizikhutitsa? Tamverani, mvetsetsani zimene ndikunena kuti mudye zimene zili zabwino; ndipo mudzisangalatse.
3 Пригните ухо своје и ходите к мени; послушајте, и жива ће бити душа ваша, и учинићу с вама завет вечан, милости Давидове истините.
Tcherani makutu ndipo mubwere kwa Ine; mvereni Ine, kuti mukhale ndi moyo. Ndidzachita nanu pangano losatha, chikondi changa chija chosasinthika ndi chodalirika ndinalonjeza Davide.
4 Ево, дадох га за сведока народима, за вођу и заповедника народима.
Taonani, ine ndamusankha kuti akhale mboni yanga kwa mitundu ya anthu, kuti akhale mtsogoleri ndi wolamulira mitundu ya anthu.
5 Ево, зваћеш народ који ниси знао, и народи који те нису знали стећи ће се к теби, ради Господа Бога твог и Свеца Израиљевог, јер те прослави.
Ndithu inu mudzayitanitsa mitundu ya anthu imene simuyidziwa, ndipo mitundu ya anthu imene sikudziwani idzabwera ndi liwiro kwa inu. Izi zidzatero chifukwa Yehova Mulungu wanu, Woyerayo wa Israeli, wakuvekani ulemerero.”
6 Тражите Господа, док се може наћи; призивајте Га, докле је близу.
Funafunani Yehova pamene Iye akupezeka. Mupemphere kwa Iye pamene ali pafupi.
7 Нека безбожник остави свој пут и неправедник мисли своје; и нека се врати ка Господу, и смиловаћу се на њ, и к Богу нашем, јер прашта много.
Woyipa asiye makhalidwe ake oyipa, ndipo wosalungama asinthe maganizo ake oyipa. Abwerere kwa Yehova, ndipo adzamuchitira chifundo, ndi kwa Mulungu wathu, pakuti adzamukhululukira koposa.
8 Јер мисли моје нису ваше мисли, нити су ваши путеви моји путеви, вели Господ;
“Pakuti maganizo anga siwofanana ndi maganizo anu, ngakhale njira zanu si njira zanga,” akutero Yehova.
9 Него колико су небеса више од земље, толико су путеви моји виши од ваших путева, и мисли моје од ваших мисли.
“Monga momwe mlengalenga muli kutali ndi dziko lapansi, momwemonso zochita zanga nʼzolekana kutali ndi zochita zanu, ndipo maganizo anga ndi osiyana kutali ndi maganizo anu.
10 Јер како пада дажд или снег с неба и не враћа се онамо, него натапа земљу и учини да рађа и да се зелени, да даје семе да се сеје и хлеб да се једе,
Monga mvula ndi chisanu chowundana zimatsika kuchokera kumwamba, ndipo sizibwerera komweko koma zimathirira dziko lapansi. Ndipo zimameretsa ndi kukulitsa zomera kenaka nʼkupatsa mlimi mbewu ndi chakudya.
11 Тако ће бити реч моја кад изађе из мојих уста: неће се вратити к мени празна, него ће учинити шта ми је драго, и срећно ће свршити на шта је пошаљем.
Ndi mmenenso amachitira mawu ochokera mʼkamwa mwanga. Sadzabwerera kwa Ine kopanda phindu lake, koma adzachita zonse zimene ndifuna, ndipo adzakwaniritsa cholinga chimene ndinawatumira.
12 Јер ћете с весељем изаћи, и у миру ћете бити вођени; горе и брегови певаће пред вама од радости, и сва ће дрвета пољска пљескати рукама.
Inu mudzatuluka mu mzindawo mwachimwemwe ndipo adzakutsogolerani mwamtendere; mapiri ndi zitunda zidzakuyimbirani nyimbo, ndipo mitengo yonse yamʼthengo idzakuwombereni mʼmanja.
13 Место трња никнуће јела, место коприве никнуће мирта; и то ће бити Господу у славу, за вечан знак, који неће нестати.
Mʼmalo mʼmene tsopano muli mitengo ya minga mudzamera mitengo ya payini, ndipo kumene kuli mkandankhuku kudzamera mchisu. Zimenezi zidzakhala chikumbutso cha Yehova, ngati chizindikiro chamuyaya, chimene sichidzafafanizika konse.”

< Књига пророка Исаије 55 >