< Књига пророка Исаије 46 >
1 Паде Вил, извали се Нево; ликови њихови метнуше се на животињу и на стоку; шта носите, тешко је, и умориће.
Beli wagwada pansi, Nebo wawerama; nyama zonyamula katundu za nyamula milungu yawo. Mafano awo asanduka katundu wolemera pa msana pa ngʼombe. Asandukadi ngati katundu pa msana pa nyama zotopa.
2 Извалише се, падоше сви, не могоше избавити товар, него и сами одоше у ропство.
Nyamazo zikuwerama ndi kufuna kugwa ndi milunguyo; sizikutha kupulumutsa katunduyo, izo zomwe zikupita ku ukapolo.
3 Слушајте ме, доме Јаковљев и сви који сте остали од дома Израиљевог, које носим од утробе, које држим од рођења.
Mverani Ine, Inu nyumba ya Yakobo, inu nonse otsala a mʼnyumba ya Israeli, Ine ndakhala ndi kukusamalirani kuyambira mʼmimba ya amayi anu, ndakhala ndikukunyamulani chibadwire chanu.
4 И до старости ваше ја ћу бити исти, и ја ћу вас носити до седог века; ја сам створио и ја ћу носити, ја ћу вас носити и избавићу.
Mpaka pamene mudzakalambe ndi kumera imvi ndidzakusamalirani ndithu. Ndinakulengani ndipo ndidzakunyamulani, ndidzakusamalirani ndi kukulanditsani.
5 С ким ћете ме изједначити и упоредити? Кога ћете ми узети за прилику да би био као ја?
“Kodi inu mudzandifanizira ndi yani, kapena mufananitsa ndi yani? Kodi mudzandiyerekeza kapena kundifanizitsa ndi yani?
6 Просипају злато из тобоца и мере сребро на мерила, плаћају златару да начини од њега бога, пред којим падају и клањају се.
Anthu ena amakhuthula golide mʼzikwama zawo ndipo amayeza siliva pa masikelo; amalemba ntchito mʼmisiri wosula kuti awapangire mulungu, kenaka iwo amagwada pansi ndikupembedza kamulunguko.
7 Мећу га на раме и носе га, и постављају га на место његово, те стоји и не миче се с места свог; ако га ко зове, не одзива се нити га избавља из невоље његове.
Amanyamula nʼkumayenda nayo milunguyo pa mapewa awo; amayikhazika pa malo pake ndipo imakhala pomwepo. Singathe kusuntha pamalo pakepo. Ngakhale wina apemphere kwa milunguyo singathe kuyankha; kapena kumupulumutsa ku mavuto ake.
8 Памтите то, и покажите се да сте људи, узмите на ум, преступници!
“Kumbukirani zimenezi ndipo muchite manyazi, Muzilingalire mu mtima, inu anthu owukira.
9 Памтите шта је било од старине; јер сам ја Бог, и нема другог Бога, и нико није као ја,
Kumbukirani zinthu zakale zinthu zamakedzana; chifukwa Ine ndine Mulungu ndipo palibe wina ofanana nane.
10 Који од почетка јављам крај и издалека шта још није било; који кажем: намера моја стоји и учинићу све што ми је воља.
Ndinaneneratu zakumathero kuchokera pachiyambi pomwe. Kuyambira nthawi yamakedzana ndinaloseratu zoti zidzachitike. Ndikanena zimene ndifuna kuchita ndipo zimachitikadi. Chilichonse chimene ndafuna ndimachichita.
11 Зовем с истока птицу и из далеке земље човека који ће извршити шта сам наумио. Рекох и довешћу то, наумих и учинићу.
Ndikuyitana chiwombankhanga kuchokera kummawa. Ndikuyitana kuchokera ku dziko lakutali munthu amene adzakwaniritsa cholinga changa. Zimene ndanena ndidzazikwaniritsadi; zimene ndafuna ndidzazichitadi.
12 Слушајте ме, који сте упорног срца, који сте далеко од правде.
Ndimvereni, inu anthu owuma mtima, inu amene muli kutali ndi chipulumutso.
13 Приближих правду своју, није далеко, и спасење моје неће одоцнити, јер ћу у Сиону поставити спасење, у Израиљу славу своју.
Ndikubweretsa pafupi tsiku la chipulumutso changa; sichili kutali. Tsikulo layandikira ndipo sindidzachedwa kukupulumutsani ndi kupereka ulemerero wanga kwa Israeli.