< 1 Мојсијева 6 >

1 А кад се људи почеше множити на земљи, и кћери им се народише.
Anthu atayamba kuchuluka pa dziko lapansi ndi kubereka ana aakazi,
2 Видећи синови Божји кћери човечије како су лепе узимаше их за жене које хтеше.
ana aamuna a Mulungu anaona kuti ana aakazi a anthuwo anali okongola. Ndipo anakwatira aliyense amene anamusankha.
3 А Господ рече: Неће се дух мој до века прети с људима, јер су тело; нека им још сто двадесет година.
Tsono Yehova anati, “Sindilola kuti chipwirikiti chikuchitikachi chipitirire mpaka muyaya, pakuti iye ndi munthu; masiku a moyo wake adzakhala zaka 120.”
4 А беше тада дивова на земљи; а и после, кад се синови Божји састајаху са кћерима човечијим, па им оне рађаху синове; то беху силни људи, од старине на гласу.
Masiku amenewo komanso pambuyo pake, pa dziko lapansi panali Anefili, anthu amphamvu ndiponso otchuka. Anthuwa ndi amene ankabadwa ana a Mulungu aja atakwatira ana aakazi a anthu.
5 И Господ видећи да је неваљалство људско велико на земљи, и да су све мисли срца њиховог свагда само зле,
Pamene Yehova anaona kuti kuyipa kwa munthu pa dziko lapansi kunali kwakukulu ndi kuti nthawi zonse amalingalira ndi kukhumbira kuchita zoyipa zokhazokha,
6 Покаја се Господ што је створио човека на земљи, и би му жао у срцу.
Yehova anamva chisoni kuti analenga munthu ndi kumuyika pa dziko lapansi, ndipo anawawidwa mtima.
7 И рече Господ: Хоћу да истребим са земље људе, које сам створио, од човека до стоке и до ситне животиње и до птица небеских; јер се кајем што сам их створио.
Choncho Yehova anati, “Ndidzafafaniza munthu, nyama, zonse zokwawa, ndi mbalame za mu mlengalenga pa dziko lapansi, pakuti ndikumva chisoni kuti ndinazilenga zimenezi.”
8 Али Ноје нађе милост пред Господом.
Koma Yehova anamukomera mtima Nowa.
9 Ово су догађаји Нојеви: Ноје беше човек праведан и безазлен свог века; по вољи Божјој свагда живљаше Ноје.
Mbiri ya Nowa inali yotere: Nowa anali munthu wolungama ndi wopanda tchimo pakati pa anthu a mʼbado wake. Ndipo anayenda ndi Mulungu.
10 И роди Ноје три сина: Сима, Хама и Јафета.
Nowa anabereka ana aamuna atatu: Semu, Hamu ndi Yafeti.
11 А земља се поквари пред Богом, и напуни се земља безакоња.
Chiwawa chinadzaza pa dziko lapansi kotero kuti dziko linakhala lowonongeka pamaso pa Mulungu.
12 И погледа Бог на земљу, а она беше покварена; јер свако тело поквари пут свој на земљи.
Mulungu atayangʼana, anaona kuti dziko layipadi chifukwa cha makhalidwe oyipa a anthu onse pa dziko lapansi.
13 И рече Бог Ноју: Крај сваком телу дође преда ме, јер напунише земљу безакоња; и ево хоћу да их затрем са земљом.
Ndipo Mulungu anati kwa Nowa, “Ndatsimikiza mtima kuti ndiwononge anthu onse, pakuti dziko lapansi ladzaza ndi ntchito zawo zoyipa. Ndithudi ndiwawononga pamodzi ndi zonse za pa dziko.
14 Начини себи ковчег од дрвета гофера, и начини прегратке у ковчегу; и затопи га смолом изнутра и споља.
Tsono udzipangire chombo cha matabwa a mtengo wanjale; mʼkati mwake upange zipinda ndipo upake phula mʼkati ndi kunja.
15 И начини га овако; у дужину нека буде триста лаката, у ширину педесет лаката, и у висину тридесет лаката;
Uchipange motere: Chombo chikhale mamita 140 mulitali, mamita 23 mulifupi ndi mamita 13 mu msinkhu wake.
16 Пусти доста светлости у ковчег; и кров му сведи озго од лакта; и удари врата ковчегу са стране; и начини га на три боја: доњи, други и трећи.
Uchipangire denga ndi kuchimaliza ndi zenera la masentimita makumi asanu. Uyike khomo mʼmbali mwa chombocho ndi kupanga zipinda zosanjikana; chapansi, chapakati ndi chapamwamba.
17 Јер ево пустићу потоп на земљу да истребим свако тело у коме има жива душа под небом; шта је год на земљи све ће изгинути.
Ndidzagwetsa mvula ya chigumula pa dziko lapansi kuti ndiwononge zamoyo zonse za pansi pa thambo ndipo chilichonse cha pa dziko lapansi chidzafa.
18 Али ћу с тобом учинити завет свој: и ући ћеш у ковчег ти и синови твоји и жена твоја и жене синова твојих с тобом.
Koma ndidzachita pangano langa ndi iwe. Iwe, ana ako aamuna, mkazi wako ndi akazi a ana ako nonse mudzalowa mʼchombocho.
19 И од свега живог, од сваког тела, узећеш у ковчег по двоје, да сачуваш у животу са собом, а мушко и женско нека буде.
Iwe udzalowa mʼchombocho ndi zolengedwa zamoyo zonse ziwiriziwiri, chachimuna ndi chachikazi, kuti zisungike ndi moyo pamodzi ndi iwe.
20 Од птица по врстама њиховим, од стоке по врстама њеним, и од свега што се миче на земљи по врстама његовим, од свега по двоје нека уђе с тобом, да их сачуваш у животу.
Udzatenga ziwiriziwiri za mitundu yonse ya mbalame, mitundu yonse ya nyama, ndi mitundu yonse ya zokwawa kuti zikhale ndi moyo.
21 И узми са собом свега што се једе, и чувај код себе, да буде хране теби и њима.
Udzatengenso chakudya cha mtundu uliwonse ndi kuchisunga kuti inu ndi nyamazo muzidzadya.”
22 И Ноје учини, како му заповеди Бог, све онако учини.
Nowa anachita zonse monga Mulungu anamulamulira.

< 1 Мојсијева 6 >

The World is Destroyed by Water
The World is Destroyed by Water