< 1 Мојсијева 45 >

1 Тада Јосиф не могући се уздржати пред осталима који стајаху око њега, повика: Изађите сви напоље. Тако не оста нико код њега кад се Јосиф показа браћи својој.
Tsono Yosefe sanathenso kuwugwira mtima kuti asalire pamaso pa antchito ake ndipo anafuwula kuti, “Aliyense achoke pamaso panga!” Motero panalibe wina aliyense pamene Yosefe anadziwulula kwa abale ake.
2 Па бризну плакати тако да чуше Мисирци, чу и дом Фараонов.
Ndipo analira mokweza mwakuti Aigupto anamva. Onse a ku nyumba kwa Farao anamvanso za zimenezi.
3 И рече Јосиф браћи својој: Ја сам Јосиф; је ли ми отац још у животу? Али му браћа не могаху одговорити, јер се препадоше од њега.
Yosefe anati kwa abale ake, “Ine ndine Yosefe! Kodi abambo anga akanali ndi moyo?” Koma abale ake sanathe kumuyankha chifukwa anali ndi mantha kwambiri pamaso pake.
4 А Јосиф рече браћи својој: Приступите ближе к мени. И приступише; а он рече ја сам Јосиф брат ваш, ког продадосте у Мисир.
Ndipo Yosefe anati kwa abale ake, “Senderani pafupi nane.” Atasendera iye anati, “Ine ndine mʼbale wanu Yosefe amene munamugulitsa ku Igupto!
5 А сада немојте жалити нити се кајати што ме продадосте овамо, јер Бог мене посла пред вама ради живота вашег.
Ndipo tsopano, musawawidwe mtima kapena kudzipsera mtima chifukwa choti munandigulitsa ine kuno, popeza Mulungu ananditsogoza ine kuti adzapulumutse miyoyo yanu.
6 Јер је већ две године дана глад у земљи, а биће још пет година, где неће бити ни орања ни жетве.
Kwa zaka ziwiri tsopano, kwakhala kuli njala mʼdziko muno, ndipo kwa zaka zisanu zikubwerazi, anthu sadzalima kapena kukolola.
7 А Бог ме посла пред вама, да вас сачува на земљи и да вам избави живот избављењем превеликим.
Koma Mulungu ananditsogoza kuti adzakusungeni ndi moyo ndi kuti mudzakhale ndi zidzukulu pa dziko lapansi.
8 И тако нисте ме ви оправили овамо него сам Бог, који ме постави оцем Фараону и господарем од свега дома његовог и старешином над свом земљом мисирском.
“Motero, si inu amene munanditumiza kuno koma Mulungu. Iye anandisandutsa kukhala nduna yayikulu ya Farao, ndipo zonse za mʼnyumba mwake zili mʼmanja mwangamu. Komanso amene akulamulira dziko lonse la Igupto ndi ine.
9 Вратите се брже к оцу мом и кажите му: Овако вели син твој Јосиф: Бог ме је поставио господарем свему Мисиру, ходи к мени, немој оклевати.
Tsono fulumirani mubwerere kwa abambo anga ndi kuwawuza kuti, ‘Mwana wanu Yosefe akuti, Mulungu anandisandutsa kukhala mbuye wa dziko lonse la Igupto. Ndiye bwerani kuno musachedwe.
10 Седећеш у земљи гесемској и бићеш близу мене, ти и синови твоји и синови синова твојих, и овце твоје и говеда твоја и шта је год твоје.
Ndipo inu, ana anu, zidzukulu zanu, pamodzi ndi nkhosa ndi ngʼombe zanu ndi antchito anu amene muli nawo muzidzakhala mʼdziko la Goseni pafupi ndi ine.
11 И ја ћу те хранити онде, јер ће још пет година бити глад, да не погинеш од глади ти и дом твој и шта је год твоје.
Ine ndizidzakupatsani zakudya kumeneko chifukwa zaka zisanu za njala zikubwera ndithu. Kupanda kutero, inu ndi mabanja anu pamodzi ndi anthu anu onse mudzasowa chakudya.’
12 А ето видите очима својим, и брат мој Венијамин својим очима, да вам ја из уста говорим.
“Tsono inu nonse pamodzi ndi mʼbale wangayu Benjamini, mukuona kuti ndi inedi amene ndikuyankhula nanu.
13 Кажите оцу мом сву славу моју у Мисиру и шта сте год видели; похитајте и доведите овамо оца мог.
Mukawawuze abambo anga kuti ndili pa ulemerero ku dziko la Igupto kuno ndi zonse zimene mwaziona. Tsopano fulumirani kuti mukabwere nawo kuno abambo anga.”
14 Тада паде око врата Венијамину брату свом и плака. И Венијамин плака о врату његовом.
Kenaka Yosefe anakhumbatira Benjamini, mngʼono wake uja nayamba kulira. Nayenso Benjamini anayamba kulira atamukumbatira.
15 И изљуби сву браћу своју и исплака се над њима. Потом се браћа његова разговараху с њим.
Atatero, Yosefe anapsompsona abale ake onse aja, akulira. Pambuyo pake abale ake aja anacheza ndi Yosefe.
16 И чу се глас у кући Фараоновој, и рекоше: Дођоше браћа Јосифу. И мило би Фараону и слугама његовим;
Akunyumba kwa Farao atamva kuti abale ake a Yosefe abwera, Farao pamodzi ndi nduna zake zonse anakondwera.
17 И рече Фараон Јосифу: Кажи браћи својој: Овако учините: натоварите магарце своје, па идите и вратите се у земљу хананску,
Farao anati kwa Yosefe, “Uwawuze abale ako kuti, ‘Senzetsani nyama zanu katundu ndi kubwerera ku dziko la Kanaani.
18 Па узмите оца свог и чељад своју, и дођите к мени, и даћу вам најбоље што има у земљи мисирској, и јешћете најбоље обиље ове земље.
Mukabwere nawo abambo anu ndi mabanja anu kuno, ndipo ine ndidzakupatsani dera lachonde kwambiri mʼdziko la Igupto. Mudzadya zokoma za mʼdzikoli.’”
19 А ти им заповеди: Овако учините: узмите са собом из земље мисирске кола за децу своју и за жене своје, и поведите оца свог и дођите овамо;
“Uwawuzenso kuti, ‘Tengani ngolo zingapo za kuno ku Igupto kuti mukakwezepo ana anu, akazi anu pamodzi ndi abambo ako ndi kubwera nawo kuno.
20 А на покућство своје не гледајте, јер шта има најбоље у свој земљи мисирској ваше је.
Musadandaule zosiya katundu komweko chifukwa dziko lachonde la kuno ku Igupto lidzakhala lanu.’”
21 И синови Израиљеви учинише тако; и Јосиф им даде кола по заповести Фараоновој; даде им и брашњенице на пут.
Choncho ana a Israeli anachita zimenezo. Yosefe anawapatsa ngolo monga Farao analamulira, ndipo anawapatsanso chakudya cha paulendo wawo.
22 И свакоме даде по две хаљине, а Венијамину даде триста сребрника и петоре хаљине.
Anaperekanso kwa aliyense zovala zatsopano, koma kwa Benjamini anapereka siliva wolemera pafupifupi makilogalamu anayi ndi zovala zisanu.
23 А оцу свом посла још десет магараца натоварених најлепших ствари што има у Мисиру, и десет магарица натоварених жита и хлеба и јестива оцу на пут.
Ndipo abambo ake anawatumizira izi: abulu khumi osenza zinthu zabwino kwambiri za ku Igupto, ndi abulu aakazi khumi osenza tirigu, buledi ndi zakudya zina za pa ulendo wake.
24 Тако оправи браћу своју, и пођоше; и рече им: Немојте се корити путем.
Kenaka anawalola abale ake aja kuti azipita, ndipo akunyamuka, iye anawawuza kuti, “Osakangana mʼnjira!”
25 Тако се вратише из Мисира, и дођоше у земљу хананску к Јакову оцу свом.
Ndipo anachoka ku Igupto nafika kwa abambo awo Yakobo mʼdziko la Kanaani.
26 И јавише му и рекоше: Још је жив Јосиф, и заповеда над свом земљом мисирском. А у њему срце пренеможе, јер им не вероваше.
Iwo anawuza abambo awo kuti, “Yosefe akanali ndi moyo! Ndiponsotu, ndiye akulamulira dziko la Igupto.” Yakobo anangoti kakasi osankhulupirira.
27 Али кад му казаше све речи Јосифове, које им је Јосиф рекао, и виде кола, која посла Јосиф по оца, тада оживе дух Јакова оца њиховог;
Komabe atamufotokozera zonse zimene Yosefe anawawuza ndipo ataona ngolo zimene Yosefe anatumiza kuti adzakweremo popita ku Igupto, mtima wa Yakobo, abambo awo unatsitsimuka.
28 И рече Израиљ: Доста ми је кад је још жив син мој Јосиф; идем да га видим докле нисам умро.
Ndipo Israeli anati, “Ndatsimikizadi! Mwana wanga Yosefe akanali ndi moyodi. Ndipita ndikamuone ndisanafe.”

< 1 Мојсијева 45 >