< Књига пророка Језекиља 39 >
1 Ти дакле, сине човечји, пророкуј против Гога, и реци: Овако вели Господ Господ: Ево ме на те, Гоже, кнеже и главо Месеху и Тувалу.
“Iwe mwana wa munthu, nenera modzudzula Gogi ndi kumuwuza kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa Mesaki ndi Tubala.
2 И вратићу те натраг и водићу те, и извешћу те из северних крајева и довешћу те на горе Израиљеве.
Ine ndidzakuzunguza ndi kukupirikitsira kutsogolo. Ndidzakutenga kuchokera kutali kumpoto ndi kukutumiza kuti ukalimbane ndi anthu a ku mapiri a Israeli.
3 И избићу ти лук твој из леве руке, и просућу ти из десне руке стреле.
Kenaka Ine ndidzathyola uta wa mʼdzanja lako lamanzere ndipo ndidzagwetsa mivi ya mʼdzanja lako lamanja.
4 На горама ћеш Израиљевим пасти ти и све чете твоје и народи који буду с тобом; птицама, свакојаким птицама крилатим и зверима пољским даћу те да те изједу.
Udzagwa ku mapiri a ku Israeli, iwe ndi magulu ako onse ankhondo ndiponso mitundu ya anthu imene ili nawe. Ndidzakusandutsa chakudya cha mitundu yonse ya mbalame zodya nyama, ndiponso cha zirombo zakuthengo.
5 На пољу ћеш пасти, јер ја рекох, говори Господ Господ.
Udzafera pa mtetete kuthengo, pakuti Ine ndayankhula. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
6 И пустићу огањ на Магога и на оне који живе на острвима без страха; и познаће да сам ја Господ.
Ndidzatumiza moto pa Magogi ndi pa onse amene amakhala mwamtendere mʼmbali mwa nyanja. Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’
7 И свето име своје обзнанићу усред народа свог Израиља, и нећу више дати да се скврни свето име моје, него ће познати народи да сам ја Господ, Светац у Израиљу.
“Ndidzachititsa kuti dzina langa loyera lidziwike pakati pa anthu anga Israeli. Sindidzalola kuti dzina langa liyipitsidwenso, ndipo mitundu ya anthu idzadziwa kuti Ine Yehova ndine Woyera mu Israeli.
8 Ево, доћи ће, и збиће се, говори Господ Господ; то је дан за који говорих.
Zikubwera! Ndipo zidzachitikadi, ndikutero Ine Ambuye Yehova. Ndiye tsiku limene ndinanena lija.
9 Тада ће изаћи становници градова Израиљевих, и наложиће на огањ и спалиће оружје и штитове и штитиће, лукове и стреле, сулице и копља, и ложиће их на огањ седам година.
“Pamenepo okhala mʼmizinda ya Israeli adzatuluka ndipo adzasonkhanitsa zida zankhondo kuti zikhale nkhuni ndipo adzazitentha; zishango ndi lihawo, mauta ndi mivi, zibonga za nkhondo ndi mikondo. Adzazisonkhera moto kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
10 И неће носити дрва из поља, нити ће сећи у шуми, него ће оружје ложити на огањ, и оплениће оне који их пленише, и поотимаће од оних који од њих отимаше, говори Господ Господ.
Iwo sadzatolera nkhuni kuthengo kapena kukadula ku nkhalango, chifukwa adzasonkhera moto zidazo. Ndipo iwo adzafunkha amene anawafunkhawo, ndi kulanda chuma cha amene anawalanda, ndikutero Ine Ambuye Yehova.
11 И у то ћу време дати Гогу место за гроб онде у Израиљу, долину којом се иде на исток к мору, и она ће стиснути уста путницима; онде ће бити погребен Гог и све мноштво његово, и прозваће се долина мноштва Гоговог.
“Pa tsiku limenelo ndidzamupatsa Gogi manda mu Israeli, mʼchigwa cha apaulendo, kummawa kwa Nyanja Yakufa. Mandawo adzatseka njira ya apaulendo, chifukwa Gogi ndi gulu lake lankhondo adzayikidwa kumeneko. Ndipo chigwacho chidzatchedwa chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
12 И укопаваће их дом Израиљев седам месеци, да би очистили земљу.
“Nyumba ya Israeli idzakhala ikukwirira mitembo kwa miyezi isanu ndi iwiri ndi cholinga choyeretsa dziko.
13 И укопаваће их сав народ, и биће им на славу у онај дан кад се прославим, говори Господ Господ.
Anthu onse a mʼdzikomo adzakwirira nawo mitembo. Ntchito imeneyo adzatchuka nayo pa tsiku limene ndidzaonetsa ulemerero wanga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
14 И одвојиће људе који ће једнако ићи по земљи и с онима који пролазе укопавати оне који би остали по земљи да је очисте; после седам месеца тражиће.
“Patapita miyezi isanu ndi iwiri adzalemba ntchito anthu ena odzayenda mʼdziko lonse kufunafuna mitembo imene inatsalira nʼkumayikwirira. Choncho adzayeretseratu dzikolo.
15 И проходиће земљу и ићи по њој, и ко види кости људске, начиниће код њих знак, докле их не укопају гробари у долини мноштва Гоговог.
Poyenda mʼdzikomo azidzati akaona fupa la munthu azidzayikapo chizindikiro pambali pake mpaka okumba manda atakalikwirira fupalo ku chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
16 А и граду ће бити име Амона; и тако ће очистити земљу.
(Komwekonso kudzakhala mzinda wotchedwa Gulu la nkhondo). Ndipo potero adzayeretsa dziko.
17 Ти, дакле, сине човечји, овако говори Господ Господ, реци птицама, свакојаким птицама и свим зверима пољским: Скупите се и ходите, саберите се са свих страна на жртву моју, коју кољем за вас, на велику жртву на горама Израиљевим, и јешћете меса и пићете крви;
“Tsono iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Itana mbalame za mitundu yonse ndi zirombo zonse zakuthengo ndipo uziwuze kuti, ‘Sonkhanani ndipo bwerani kuchokera ku mbali zonse ku nsembe imene ndikukonzerani inu, nsembe yayikulu pa mapiri a Israeli. Kumeneko inu mudzadya mnofu ndi kumwa magazi.
18 Јешћете меса јуначког и пићете крви кнезова земаљских, овнова, јагањаца и јараца и телаца, све угојене стоке васанске.
Mudzadya mnofu wa anthu ankhondo amphamvu ndi kumwa magazi a akalonga a dziko lapansi. Onsewo anaphedwa ngati nkhosa zazimuna, ana ankhosa onenepa, mbuzi ndiponso ngati ngʼombe zazimuna zonenepa za ku Basani.
19 И јешћете претилине да ћете се наситити, и пићете крви да ћете се опити од жртава мојих што ћу вам наклати.
Ku phwando lansembe limene ndikukonzera inulo, mudzadya zonona mpaka kukhuta ndi kumwa magazi mpaka kuledzera.
20 И наситићете се за мојим столом коња и коњика, јунака и свакојаких војника, говори Господ Господ.
Pa tebulo langa mudzakhuta pakudya akavalo ndi okwerapo ake, anthu amphamvu ndi asilikali amitundumitundu,’ ndikutero Ine Ambuye Yehova.
21 И пустићу славу своју међу народе, и сви ће народи видети суд мој који ћу учинити и моју руку коју ћу дигнути на њих.
“Ine ndidzaonetsa ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina, ndipo adzaona mmene ndidzawalangire ndikadzayika dzanja langa pa iwo.
22 И познаће дом Израиљев да сам ја Господ Бог њихов, од оног дана и после.
Kuyambira tsiku limenelo mpaka mʼtsogolo Aisraeli adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo.
23 И народи ће познати да се за своје безакоње зароби дом Израиљев, што мени згрешише, те сакрих лице своје од њих, и дадох их у руке непријатељима њиховим, и сви падоше од мача.
Ndipo anthu a mitundu ina adzadziwa kuti anthu a Israeli anatengedwa ukapolo chifukwa cha tchimo lawo, chifukwa anali osakhulupirika kwa Ine. Choncho Ine ndinawabisira nkhope yanga ndi kuwapereka kwa adani awo. Motero anaphedwa pa nkhondo.
24 По нечистоти њиховој и по преступу њихову учиних им и сакрих лице своје од њих.
Ndinawachita zimenezi chifukwa cha kunyansa kwawo ndi zolakwa zawo, ndipo ndinawabisira nkhope yanga.
25 Тога ради овако говори Господ Господ: Повратићу робље Јаковљево и смиловаћу се свему дому Израиљевом и ревноваћу за свето име своје,
“Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Tsopano ndidzakhazikanso pa bwino banja la Yakobo. Ndidzachitira chifundo Aisraeli onse, ndipo ndidzateteza dzina langa loyera.
26 Пошто поднесу срамоту своју и све преступе своје, којима ми преступише док сеђаху у својој земљи без страха и никога не беше да их плаши,
Anthuwo akadzakhala mwamtendere mʼdziko lawo popanda wina wowaopseza, pamenepo adzayiwala zamanyazi zawo zimene zinawachitikira chifukwa chosandikhulupirira Ine.
27 Кад их доведем натраг из народа и саберем их из земаља непријатеља њихових, и посветим се у њима пред многим народима.
Ndidzawabwezeranso kwawo kuchokera pakati pa anthu a mitundu ina ndipo ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko a adani awo. Poteropo ndidzaonetsa pamaso pa anthu a mitundu yambiri kuti ndine Woyera.
28 И познаће да сам ја Господ Бог њихов кад одведавши их у ропство међу народе опет их саберем у земљу њихову не оставивши их ниједнога онде.
Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo, ngakhale kuti ndinawapereka ku ukapolo pakati pa anthu a mitundu ina. Ine ndidzawasonkhanitsanso ku dziko lawo osasiyako wina mʼmbuyo.
29 И нећу више крити лице своје од њих кад излијем Дух свој на дом Израиљев, говори Господ Господ.
Ine sindidzawabisiranso nkhope yanga, pakuti ndidzathira Mzimu wanga pa Aisraeli. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”