< Књига пророка Језекиља 16 >
1 Опет ми дође реч Господња говорећи:
Yehova anayankhula nane kuti,
2 Сине човечји, покажи Јерусалиму гадове његове,
“Iwe mwana wa munthu, udzudzule Yerusalemu za ntchito zake zonyansa.
3 И реци: Овако вели Господ Господ Јерусалиму: Постањем и родом ти си из земље хананске; отац ти беше Аморејац а мати Хетејка.
Umuwuze kuti, ‘Ambuye Yehova akukuwuza, iwe Yerusalemu kuti: Kwawo kwa makolo ako ndi ku Kanaani ndipo iwe unabadwira komweko. Abambo ako anali Mwamori, amayi ako anali Mhiti.
4 А о рођењу твом, кад си се родила, није ти пупак одрезан и ниси окупана водом да би била чиста, нити си сољу натрвена ни пеленама повита.
Pa tsiku lomwe unabadwa sanadule mchombo wako. Sanakusambitse mʼmadzi kuti uyere. Sanakuthire mchere kapena kukukulunga mʼnsalu.
5 Око те не пожали да ти учини шта од тога и да ти се смилује: Него ти би бачена у поље, јер беше мрска душа твоја оног дана кад си се родила.
Palibe ndi mmodzi yemwe anakusamala kapena kukumvera chisoni kuti akuchitire zimenezi. Mʼmalo mwake anakutaya panja poyera, chifukwa ananyansidwa nawe pa tsiku lako lobadwa.
6 И идући мимо тебе и видевши те где се ваљаш у својој крви, рекох ти: Да си жива у својој крви! И опет ти рекох: Да си жива у својој крви!
“‘Tsono pamene ndinkadutsa, ndinakuona ukuvimvinizika mʼmagazi ako. Ndinakuyankhula uli mʼmagazi ako omwewo kuti, ‘Khala ndi moyo,’
7 И учиних да растеш на хиљаде као трава у пољу; и ти нарасте и поста велика и дође до највеће лепоте; дојке ти напупише, и длаке те пробише; али ти беше гола нага.
ndi kuti ukule ngati mbewu ya mʼmunda. Iwe unakula ndipo unatalika ndi kutha msinkhu. Mawere ako anayamba kumera ndi tsitsi lakonso linayamba kutalika. Komabe unali wamaliseche ndi wausiwa.
8 И идући мимо тебе погледах те, и гле, године ти беху године за љубљење; и раширих скут свој на те, и покрих голотињу твоју, и заклех ти се и учиних веру с тобом, говори Господ Господ, и ти поста моја.
“‘Tsono pamene ndinkadutsanso ndinaona kuti nthawi yako yomanga banja inakwana. Tsono ndinakufunditsa chovala changa ndi kubisa umaliseche wako. Ndinachita nawe pangano la ukwati ndipo unakhala wanga, akutero Ambuye Wamphamvuzonse.
9 И окупах те водом, и спрах с тебе крв твоју, и помазах те уљем.
“‘Ine ndinakusambitsa mʼmadzi kutsuka magazi ako ndikukudzoza mafuta.
10 И обукох ти везену хаљину, и обух ти цревље од јазавца, и опасах те танким платном и застрех те свилом.
Ndinakuveka zovala zopetapeta ndi nsapato za chikopa. Ndinakuveka zovala zabafuta ndi kukuveka zovala za bafuta.
11 И накитих те накитом, и метнух ти наруквице на руке и гривну око врата.
Ndinakukongoletsa ndi zokometsera zamtengowapatali: ndinakuveka zibangiri mʼmanja mwako ndi mkanda mʼkhosi mwako,
12 И гривну око чела метнух ти, и обоце у уши, славан венац на главу.
ndipo ndinakuveka chipini pa mphuno yako, ndolo ku makutu ako ndiponso chipewa chaufumu pa mutu wako.
13 И ти беше окићена златом и сребром, и одело ти беше од танког платна и од свиле и везено, јеђаше бело брашно и мед и уље, и беше врло лепа, и приспе до царства.
Choncho unavala zokongoletsa zagolide ndi siliva. Zovala zako zinali zabafuta, zasilika ndi za nsalu zopetapeta. Chakudya chako chinali ufa wosalala uchi ndi mafuta a olivi. Motero unakhala wokongola kwambiri ndipo unasanduka mfumukazi.
14 И разиђе се глас о теби по народима ради лепоте твоје, јер беше савршена красотом мојом, коју метнух на те, говори Господ Господ.
Ndipo mbiri ya kukongola kwako inawanda pakati pa anthu a mitundu ina, chifukwa ulemerero umene ndinakupatsa unapititsa patsogolo kukongola kwako, akutero Ambuye Yehova.
15 Али се ти ослони на лепоту своју, и прокурва се с гласа свог, те си просипала курварство своје свакоме који пролажаше, и бивала си његова.
“‘Koma iwe unatama kukongola kwako ndipo unayamba kuchita zadama chifukwa cha kutchuka kwako. Unkachita chigololo ndi kumangodzipereka kwa aliyense wodutsa ndipo kukongola kwako kunakhala kwake.
16 И узевши од хаљина својих начинила си шарене висине, и курвала си се на њима, како никада није било нити ће бити.
Unatenga zovala zako zina nukakongoletsera malo opembedzerako mafano, ndipo kumeneko umachitirako zigololo. Zinthu izi sizinachitikepo nʼkale lomwe ndipo sizidzachitikanso.
17 И узевши красни накит свој од мог злата и од мог сребра што ти дадох, начинила си себи мушке ликове, и курвала си се с њима.
Unatenga zokongoletsera zopangidwa ndi golide ndi siliva zimene ndinakupatsa ndipo unadzipangira wekha mafano aamuna amene unkachita nawo za dama.
18 И узевши везене хаљине своје заодела си их, и уље моје и кад мој ставила си пред њих.
Ndipo iwe unatenga zovala zako zopetapeta ndi kuveka mafano. Mafuta anga ndi lubani wanga unapereka kwa mafanowo.
19 И хлеб мој, који ти дадох, бело брашно и уље и мед, чим те храњах, поставила си пред њих за мирис угодни. Тако је било, говори Господ Господ.
Chakudya chimene ndinakupatsa, ufa, mafuta ndi uchi, zimene ndinkakudyetsa nazo unazitenga nʼkuzipereka kwa mafanowo ngati nsembe ya fungo lokoma. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
20 И узимала си синове своје и кћери своје које си родила, и њих си им приносила да се спале. Мало ли беше курварства твог,
“‘Ndipo unatenga ana ako aamuna ndi ana aakazi amene unandibalira ine, ndipo unakawapereka ngati nsembe kwa mafanowo. Kodi zigololo zakozo sizinakukwanire
21 Те си и синове моје клала и давала си их да им се проведу кроз огањ?
kuti uziphanso ana anga ndi kuwapereka ngati nsembe kwa mafano akowo?
22 И уза све гадове своје и курварства своја ниси се опомињала дана младости своје кад си била гола и нага и ваљала се у крви својој.
Chifukwa cha zadama zako zonyansazi unayiwala masiku a ubwana wako pamene unali wamaliseche, wausiwa ndiponso womangovivinizika mʼmagazi.
23 И после све злоће своје, (Тешко, тешко теби! Говори Господ Господ, )
“‘Tsoka! Tsoka kwa iwe, akutero Ambuye Yehova chifukwa powonjezera pa zoyipa zako zonse,
24 Саградила си себи кућу курварску, и начинила си себи висине на свакој улици,
wadzimangira wekha nsanja ndi guwa pa mabwalo onse.
25 На свакој распутици начинила си себи висину, и нагрдила си своју лепоту, и разметала си ноге своје свакоме који пролажаше, и умножила си курварство своје.
Pa msewu uliwonse wamanga nsanjazo. Motero wanyazitsa kukongola kwako podzipereka kwa aliyense amene adutsapo.
26 Курвала си се са синовима мисирским, суседима својим великог тела, и умножила си курварство своје да би ме разгневила.
Umachita chigololo ndi Aigupto, anthu adama oyandikana nawe. Choncho unandikwiyitsa chifukwa unachulukitsa za dama zako.
27 Зато гле, дигох руку своју на те и умалих оброк твој, и дадох те на вољу ненавидницима твојим, кћерима филистејским, које беше стид од срамотног пута твог.
Nʼchifukwa chake ndinatambasula dzanja langa kukukantha ndi kuchepetsa dziko lako. Ndinakupereka kwa adani ako, Afilisti amene amayipidwa ndi makhalidwe ako onyansa.
28 Курвала си се са синовима асирским, јер се не могаше наситити; курвала си се с њима, и опет се ниси наситила.
Chifukwa cha chilakolako chako unachitanso zadama ndi Aasiriya. Ngakhale unachita nawo chigololo koma sunakhutitsidwebe.
29 И умножила си курварство своје у земљи хананској све до халдејске, и ни тако се ниси наситила.
Choncho unapitirirabe kuchita chigololo ndi Ababuloni, anthu a mʼdziko lokonda zamalonda. Ngakhale unachita izi, komabe sunakhutitsidwe.
30 Како је изнемогло срце твоје, говори Господ Господ, кад чиниш све што чини најгора курва,
“‘Ambuye Yehova akuti: Mtima wako ndi wofowoka kwambiri chifukwa unachita zonsezo monga ngati mkazi wopanga manyazi.
31 Кад си градила курварску кућу на свакој распутици и чинила висину на свакој улици! А ни као курва ниси, јер ниси марила за плату;
Unamanga nsanja pa msewu uliwonse. Unamanganso kachisi pabwalo lililonse. Komabe sunachite ngati mkazi wadama chifukwa unakana malipiro.
32 Него као жена прељубочиница, која место мужа свог прима друге.
“‘Iwe mkazi wachigololo! Umakonda amuna achilendo kupambana mwamuna wakowako!
33 Свим курвама даје се плата, а ти си давала плату свим милосницама својим и даривала си их да долазе к теби са свих страна да се курвају с тобом.
Amuna ndiwo amapereka malipiro kwa mkazi wadama. Koma iwe ndi amene ukupereka mphatso kwa zibwenzi zako zonse. Choncho umazinyengerera kuti zizibwera kwa iwe kuchokera mbali zonse kudzagona nawe.
34 И тако је у тебе наопако према женама у твом курварству: Јер нико не иде за тобом да се курва, и ти дајеш плату, а не даје се теби плата; то је наопако.
Chotero iwe ukusiyana ndi akazi ena achigololo, pakuti palibe amene ankakunyengerera kuti uchite naye chigololo. Iweyo ndiye unkapereka ndalama osati ena kukupatsa ndalama ayi. Motero unalidi wosiyana kwambiri ndi akazi ena.
35 Зато, курво, чуј реч Господњу.
“‘Tsono mkazi wachigololo iwe, imva mawu a Yehova!
36 Овако вели Господ Господ: Што се отров твој просу, и што се у курвању твом откривала голотиња твоја твојим милосницима и свим гадним идолима твојим, и за крв синова твојих, које си им дала,
Ambuye Yehova akuti, popeza unavula ndi kuonetsa umaliseche wako mopanda manyazi, unachita chigololo ndi zibwenzi zako pamodzi ndi mafano ako onyansa, komanso popeza unapereka ana ako kuti aphedwe ngati nsembe zoperekedwa kwa mafano,
37 Зато, ево, ја ћу скупити све милоснике твоје, с којима си се миловала, и све које си љубила, и све на које си мрзела, скупићу их све око тебе, и открићу им голотињу твоју да виде сву голотињу твоју.
nʼchifukwa chake Ine ndidzasonkhanitsa zibwenzi zako zonse, zimene unkasangalala nazo, amene unkawakonda ndi amene unkawada. Ndidzawasonkhanitsa motsutsana nawe kuchokera ku madera onse okuzungulira ndipo Ine ndidzakuvula pamaso pawo, ndipo iwo adzaona umaliseche wako wonse.
38 И судићу ти како се суди онима које чине прељубу и онима које крв проливају, и даћу те на смрт гневу и ревности.
Ine ndidzakulanga monga mmene amalangira akazi amene amachita chigololo ndiponso opha anthu. Chifukwa cha ukali wanga ndi nsanje yanga, ndidzakhetsa magazi ako mokwiya kwambiri.
39 И предаћу те у њихове руке, те ће разорити твоју кућу курварску и раскопати висине твоје, и свући ће хаљине с тебе, и узеће ти красни накит и оставиће те голу нагу.
Ndidzakupereka mʼmanja mwa zibwenzi zako ndi kuwononga nyumba zopembedzera mafano ako. Iwo adzakuvula zovala zako ndi kutenga zodzikometsera zako zabwino. Choncho adzakusiya wa maliseche ndi wausiwa.
40 И довешће на те људство, те ће те засути камењем, и избошће те мачевима својим.
Iwo adzabweretsa gulu la anthu limene lidzakuponya miyala ndi kukutematema ndi malupanga awo.
41 И попалиће куће твоје огњем, и извршиће на теби суд пред многим женама, и учинићу те ћеш се оканити курвања и нећеш више давати плате.
Adzatentha nyumba zako ndi kukulanga iwe pamaso pa akazi ambiri. Ndidzathetsa chigololo chako, ndipo sudzalipiranso zibwenzi zako.
42 И намирићу гнев свој над тобом, и ревност ће се моја уклонити од тебе, и умирићу се, и нећу се више гневити.
Ukali wanga udzalekera pamenepo ndipo sindidzakuchitiranso nsanje. Ndidzakhala chete osakwiyanso.
43 Зато што се ниси опомињала дана младости своје, него си ме дражила свим тим, зато, ево, и ја ћу обратити пут твој на твоју главу, говори Господ Господ, те нећеш чинити грдила нити каквих гадова својих.
“‘Popeza sunakumbukire masiku a ubwana wako koma unandikwiyitsa ndi zinthu zonsezi, Ine ndidzakubwezera ndithu chilango pamutu pako chifukwa cha zimene wachita, akutero Ambuye Yehova. Paja unawonjezera chigololo pa machitidwe ako onyansa.
44 Гле, ко год говори приче, говориће о теби причу, и рећи ће: Каква мати, таква јој кћи.
“‘Taona, onse onena miyambi adzakuphera mwambi wakuti, ‘Make mbuu, mwana mbuu.’
45 Ти си кћи матере своје, која се одметнула од мужа свог и деце своје, и сестра си сестара својих, које се одметнуше од мужева својих и деце своје, мати вам је Хетејка а отац Аморејац.
Ndiwedi mwana weniweni wamkazi wa mayi wako, amene amanyoza mwamuna wake ndi ana ake. Ndiwe mʼbale weniweni wa abale ako, amene amanyoza amuna awo ndi ana awo. Amayi ako anali Mhiti ndipo abambo ako anali Mwamori.
46 А старија ти је сестра Самарија с кћерима својим, која ти седи с леве стране, а млађа ти је сестра која ти седи с десне стране Содом са кћерима својим.
Mkulu wako anali Samariya, ndipo iye pamodzi ndi ana ake aakazi ankakhala cha kumpoto kwako. Mngʼono wako, Sodomu ankakhala cha kummwera kwako pamodzi ndi ana ake aakazi.
47 А ти ни њиховим путем ниси ходила, нити си чинила по њиховим гадовима, као да ти то беше мало, него си била гора од њих на свим путевима својим.
Iwe sunangotsatira kokha njira zawo zoyipa ndi kuchita zonyansa zawo, koma patangopita nthawi pangʼono machitidwe ako oyipa anaposa awo.
48 Тако ја жив био, говори Господ Господ, сестра твоја Содом и кћери њене нису чиниле како си чинила ти и твоје кћери.
Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, ngakhale mʼbale wako Sodomu ndi ana ake aakazi sanachitepo zimene iwe ndi ana ako aakazi munachita.
49 Ево, ово беше безакоње сестре твоје Содома: У поносу, у изобиљу хлеба и безбрижном миру беше она и кћери њене, а не помагаху сиромаху и убогом;
“‘Tsono tchimo la mʼbale wako Sodomu linali ili: Iye ndi ana ake aakazi ankanyadira kuchuluka kwa chakudya ndi chuma chawo. Koma sanalabadireko kuthandiza osauka ndi aumphawi.
50 Него се понашаху и чињаху гадове преда мном, за то их затрх кад видех.
Anali odzitukumula ndipo ankachita zonyansa pamaso panga. Nʼchifukwa chake ndinawachotsa monga mmene waoneramu.
51 Самарија није згрешила пола колико ти, јер си починила гадова својих више него оне, те си оправдала сестре своје свим гадовима својим које си учинила.
Samariya sanachite ngakhale theka la machimo amene unachita. Iwe wachita zinthu zonyansa zambiri kuposa iwo, motero kuti abale ako awiriwo amaoneka ngati olungama kuyerekeza ndi iye.
52 И ти дакле, која си судила сестрама својим, носи срамоту своју за грехе своје, којима си постала грђа од њих; оне су праведније од тебе; и ти се дакле стиди и носи срамоту, кад си оправдала сестре своје.
Tsono iwenso uyenera kuchita manyazi popeza waonetsa abale ako ngati osachimwa. Popeza kuti machimo ako ndi onyansa kwambiri kupambana awo, tsonotu iwowo akuoneka olungama kupambana iweyo. Choncho iwenso uchite manyazi ndi kunyozedwa popeza unaonetsa abale ako ngati olungama.
53 Ако доведеш натраг њихово робље, робље содомско и кћери њене, и робље самаријско и кћери њене, довешћу и твоје робље из ропства међу њима.
“‘Koma, ndidzadalitsanso Sodomu ndi ana ake aakazi. Ndidzadalitsanso Samariya ndi ana ake aakazi. Pa nthawi yomweyo ndidzakudalitsanso iwe Yerusalemu.
54 Да носиш срамоту своју и да се стидиш за све што си чинила, и да им будеш утеха.
Ndidzatero kuti uchite manyazi ndi kunyozeka chifukwa cha zonse zimene unachita powatonthoza anthuwa.
55 Ако се сестре твоје, Содом и кћери њене поврате као што су биле, и ако се Самарија и кћери њене поврате као што су биле, повратићеш се и ти и кћери твоје као што сте биле.
Motero mʼbale wako Sodomu ndi ana ake akadzakhala monga mmene analili poyamba paja, ndiponso mʼbale wako Samariya akadzakhalanso monga mmene anali poyamba paja, ndiye kuti iwenso ndi ana ako mudzakhala monga mmene munalili payamba paja.
56 Јер уста твоја не помињаше Содом, сестру твоју, у време охолости твоје,
Kale lija pamene unkanyada, suja unkanyogodola mʼbale wako Sodomu
57 Пре него се откри злоћа твоја као у време срамоте од кћери сирских и од свих што су око њих, кћери филистејских, које те срамоћаху са свих страна.
kuyipa kwako kusanadziwike? Koma tsopano wafanana naye. Wasandukano chinthu chonyozeka kwa anthu a ku Edomu ndi kwa onse owazungulira ndiponso kwa Afilisti. Ndithu onse amene akuzungulira amakunyoza.
58 Носи неваљалство своје и гадове своје, говори Господ.
Choncho udzalangidwa chifukwa cha zigololo zako ndi machitidwe anu onyansa, akutero Yehova.
59 Јер овако вели Господ Господ: Учинићу ти како си ти учинила презревши заклетву и преступивши завет.
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzakulanga molingana ndi zimene unachita. Iwe unanyoza lumbiro lako pophwanya pangano langa.
60 Али ћу се ја опоменути завета свог који сам учинио с тобом у време младости твоје, и утврдићу ти вечан завет.
Komabe, Ine ndidzakumbukira pangano limene ndinachita nawe mʼmasiku a unyamata wako, ndipo ndidzakhazikitsa pangano losatha ndi iwe.
61 Тада ћеш се опоменути путева својих и постидећеш се кад примиш сестре своје старије од себе и млађе, које ћу ти дати за кћери, али не по твом завету.
Tsono udzakumbukira njira zako zakale. Udzachita manyazi polandiranso abale ako, wamkulu ndi wamngʼono yemwe. Ndidzawaperekanso kwa iwe kuti akhale ngati ana ako ngakhale kuti sali a mʼpangano langa ndi iwe.
62 И ја ћу утврдити завет свој с тобом, и познаћеш да сам ја Господ,
Kotero ndidzakhazikitsa pangano langa ndi iwe, ndipo iwe udzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
63 Да се опоменеш и постидиш и да не отвориш више уста од срамоте, кад ти опростим све што си учинила, говори Господ Господ
Ndikadzakukhululukira zoyipa zako zonse zimene unachita, udzazikumbukira ndipo udzachita manyazi kwambiri, kotero kuti sudzatha nʼkuyankhula komwe, akutero Ambuye Yehova.’”