< 2 Мојсијева 2 >

1 А неко од племена Левијевог отиде и ожени се кћерју Левијевом.
Ndipo munthu wina wa fuko la Levi anakwatira mkazi wa fuko lomwelo.
2 И она затрудне и роди сина; и видећи га лепог кријаше га три месеца.
Mkaziyo anatenga pathupi ndipo anabereka mwana wamwamuna. Ataona kuti mwanayo anali wokongola, anamubisa kwa miyezi itatu.
3 А кад га не може више крити, уже ковчежић од сите, и обли га смолом и паклином, и метну дете у њ, и однесе га у трску крај реке.
Koma mwanayo atafika pa msinkhu woti sakanathanso kubisidwa, amayi ake anatenga kadengu kopangidwa ndi bango nakamata phula. Kenaka anayika mwanayo mʼmenemo ndi kukamuyika pa mabango mu mtsinje wa Nailo.
4 А сестра његова стаде подаље да види шта ће бити од њега.
Mlongo wake wa mwanayo anayima pataliko kuti aone chimene chidzamuchitikira mwanayo.
5 А кћи Фараонова дође да се купа у реци, и девојке њене ходаху крај реке; и она угледа ковчежић у трсци, и посла дворкињу своју те га извади.
Mwana wamkazi wa Farao anapita ku mtsinje wa Nailo kukasamba ndipo adzakazi ake ankayenda mʼmbali mwa mtsinjewo. Tsono mwana wa Farao uja anaona kadenguko pakati pa mabango ndipo anatuma mdzakazi wake kuti akakatenge.
6 А кад отвори, виде дете, и гле, дете плакаше; и сажали јој се, и рече: То је јеврејско дете.
Iye atavundukula anaona mwana wamwamuna akungolira. Iye anamva naye chisoni mwana uja, nati, “Ameneyu ndi mmodzi mwa ana a Chihebri.”
7 Тада рече сестра његова кћери Фараоновој: Хоћеш ли да идем да ти дозовем дојкињу Јеврејку, да ти доји дете?
Kenaka mlongo wake wa mwanayo anafunsa mwana wa Farao kuti, “Ndingapite kukakupezerani mmodzi mwa amayi a Chihebri kuti azikakulererani mwanayu?”
8 А кћи Фараонова рече јој: Иди. И отиде девојчица, и дозва матер детињу.
Iye anayankha kuti, “Inde, pita.” Ndipo mtsikanayo anapita nakayitana amayi a mwanayo.
9 И кћи Фараонова рече јој: Узми ово дете, и одој ми га, а ја ћу ти платити. И узе жена дете и одоји га.
Mwana wa Farao anati, “Tengani mwanayu mukandilerere, ndidzakulipirani.” Mayiyo anatenga mwanayo kukamulera.
10 А кад дете одрасте, одведе га ка кћери Фараоновој, а она га посини; и надеде му име Мојсије говорећи: Јер га из воде извадих.
Mwanayo atakula anakamupereka kwa mwana wa Farao ndipo anakhala mwana wake. Iye anamutcha dzina lake Mose, popeza anati, “Ndinamuvuwula mʼmadzi.”
11 И кад Мојсије беше велик, изађе к браћи својој, и гледаше невољу њихову. И виде где некакав Мисирац бије човека Јеврејина између браће његове.
Tsiku lina, Mose atakula, anapita kumene kunali anthu a mtundu wake ndipo anawaona akugwira ntchito yowawa. Iye anaona Mwigupto akumenya Mhebri, mmodzi mwa anthu a mtundu wake.
12 И обазрев се и тамо и амо, кад виде да нема никога, уби Мисирца, и закопа га у песак.
Atayangʼana uku ndi uku, naona kuti panalibe wina aliyense, Mose anamupha Mwiguptoyo ndipo anamukwirira mu mchenga.
13 И сутрадан изађе опет, а то се два Јеврејина свађаху, и рече оном који чињаше криво: Зашто бијеш ближњег свог?
Mmawa mwake Mose anapita ndipo anaona anthu awiri a Chihebri akumenyana. Iye anafunsa amene anali wolakwa kuti, “Chifukwa chiyani ukumenya Mhebri mnzako?”
14 А он рече: Ко је тебе поставио кнезом и судијом над нама? Хоћеш ли да ме убијеш као што си убио Мисирца? Тада се Мојсије уплаши и рече: Заиста се дознало.
Munthu uja anati, “Kodi ndani anakuyika kuti ukhale wotilamulira ndi wotiweruza? Kodi ukufuna kundipha monga momwe unaphera Mwigupto uja?” Mose anachita mantha ndipo anati mu mtima mwake, “Chimene ndinachita chija chadziwika.”
15 И Фараон чувши за то тражаше да погуби Мојсија. Али Мојсије побеже од Фараона и дође у земљу мадијанску, и седе код једног студенца.
Farao atamva zimenezi anafuna kuti aphe Mose, koma Mose anathawa ndipo anapita kukakhala ku Midiyani. Ali kumeneko, tsiku lina anakhala pansi pafupi ndi chitsime.
16 А свештеник мадијански имаше седам кћери, и оне дођоше и стадоше захватати воду и наливати у појила да напоје стадо оца свог.
Wansembe wa ku Midiyaniko anali ndi ana aakazi asanu ndi awiri. Iwowa anabwera kudzatunga madzi ndi kudzaza mu zomwera kuti amwetse nkhosa za abambo awo.
17 А дођоше пастири, и отераше их; а Мојсије уста и одбрани их, и напоји им стадо.
Koma kunabwera abusa ena amene anathamangitsa atsikana aja. Ndiye Mose anayimirira nawathandiza atsikana aja ndi kumwetsa nkhosa zawo.
18 И оне се вратише к оцу свом Рагуилу; а он рече: Што се данас тако брзо вратисте?
Atsikana aja atabwerera kwa abambo awo Reueli, iye anawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani lero mwabwera msanga?”
19 А оне рекоше: Један Мисирац одбрани нас од пастира, и нали нам и напоји стадо.
Atsikanawo anayankha kuti, “Mwigupto wina ndiye watilanditsa kwa abusa. Ndiponso anatitungira madzi ndi kumwetsa ziweto zathu.”
20 А он рече кћерима својим: Па где је? Зашто остависте тог човека? Зовите га да једе.
Tsono Reueli anafunsa ana ake kuti, “Ndiye ali kuti munthuyo? Chifukwa chiyani mwamusiya? Kamuyitaneni kuti adzadye.”
21 И Мојсије се склони да живи код оног човека, и он даде Мојсију кћер своју Сефору.
Mose anavomera kukhala ndi Reueli, ndipo anamupatsa Zipora kuti akhale mkazi wake.
22 И она роди сина, и он му надеде име Гирсам, јер сам, рече, дошљак у земљи туђој.
Zipora anabereka mwana wa mwamuna amene Mose anamutcha Geresomu, popeza anati, “Ndakhala mlendo mʼdziko la eni.”
23 А после много времена умре цар мисирски; и уздисаху од невоље синови Израиљеви и викаху; и вика њихова ради невоље дође до Бога.
Nthawi yonseyo nʼkuti ana a Israeli akulira chifukwa cha ukapolo wawo uja. Iwo anafuwula kupempha thandizo, ndipo kulira kwawoko kunafika kwa Mulungu.
24 И Бог чу уздисање њихово, и опомену се Бог завета свог с Аврамом, с Исаком и с Јаковом.
Mulungu anamva kubuwula kwawo ndipo anakumbukira pangano lake ndi Abrahamu, Isake ndi Yakobo.
25 И погледа Бог на синове Израиљеве, и виде их.
Mulungu ataona Aisraeli aja ndi masautso awo, Iye anawamvera chifundo.

< 2 Мојсијева 2 >