< Књига проповедникова 7 >
1 Боље је име него добро уље, и дан смртни него дан у који се ко роди.
Mbiri yabwino ndi yopambana mafuta onunkhira bwino, ndipo tsiku lomwalira ndi lopambana tsiku lobadwa.
2 Боље је ићи у кућу где је жалост него где је гозба, јер је онде крај сваког човека, и ко је жив, слаже у срце своје.
Kuli bwino kupita ku nyumba yamaliro kusiyana ndi kupita ku nyumba yamadyerero: Pakuti imfa ndiye mathero a munthu aliyense; anthu amoyo azichisunga chimenechi mʼmitima mwawo.
3 Боља је жалост него смех, јер кад је лице невесело, срце постаје боље.
Chisoni nʼchabwino kusiyana ndi kuseka, pakuti nkhope yakugwa ndi yabwino chifukwa imakonza mtima.
4 Срце је мудрих људи у кући где је жалост, а срце безумних у кући где је весеље.
Mtima wa munthu wanzeru nthawi zonse umalingalira za imfa, koma mitima ya zitsiru imalingalira za chisangalalo.
5 Боље је слушати карање мудрога него да ко слуша песму безумних.
Kuli bwino kumva kudzudzula kwa munthu wanzeru kusiyana ndi kumvera mayamiko a zitsiru.
6 Јер као што прашти трње под лонцем, такав је смех безумников; и то је таштина.
Kuseka kwa zitsiru kuli ngati kuthetheka kwa moto kunsi kwa mʼphika, izinso ndi zopandapake.
7 Насиље обезумљује мудрога, и поклон изопачује срце.
Kuzunza ena kumasandutsa munthu wanzeru kukhala chitsiru, ndipo chiphuphu chimawononga mtima.
8 Бољи је крај ствари него почетак јој; бољи је ко је стрпљивог духа неголи ко је поноситог духа.
Mathero ake a chinthu ndi abwino kupambana chiyambi chake, ndipo kufatsa nʼkwabwino kupambana kudzikuza.
9 Не буди нагао у духу свом на гнев, јер гнев почива у недрима безумних.
Usamafulumire kukwiya mu mtima mwako, pakuti mkwiyo ndi bwenzi la zitsiru.
10 Не говори: Шта је то, те су пређашњи дани били бољи од ових? Јер не би било мудро да за то питаш.
Usamafunse kuti, “Nʼchifukwa chiyani masiku amakedzana anali abwino kupambana masiku ano?” pakuti si chinthu chanzeru kufunsa mafunso oterewa.
11 Добра је мудрост с имањем, и корисна је онима који виде сунце.
Nzeru ngati cholowa, ndi chinthu chabwino ndipo imapindulitsa wamoyo aliyense pansi pano.
12 Јер је мудрост заклон, и новци су заклон; али је претежније знање мудрости тим што даје живот ономе ко је има.
Nzeru ndi chitetezo, monganso ndalama zili chitetezo, koma phindu la chidziwitso ndi ili: kuti nzeru zimasunga moyo wa munthu amene ali nazo nzeruzo.
13 Погледај дело Божије; јер ко може исправити шта Он искриви?
Taganizirani zimene Mulungu wazichita: ndani angathe kuwongola chinthu chimene Iye anachipanga chokhota?
14 У добро време уживај добро, а у зло време гледај, јер је Бог створио једно према другом за то да човек не зна шта ће бити.
Pamene zinthu zili bwino, sangalala; koma pamene zinthu sizili bwino, ganizira bwino: Mulungu ndiye anapanga nthawi yabwinoyo, ndiponso nthawi imene si yabwinoyo. Choncho munthu sangathe kuzindikira chilichonse cha mʼtsogolo mwake.
15 Свашта видех за времена таштине своје: праведника који пропада у правди својој, и безбожника који дуго живи у својој злоћи.
Pa moyo wanga wopanda phinduwu ndaona zinthu ziwiri izi: munthu wolungama akuwonongeka mʼchilungamo chake, ndipo munthu woyipa akukhala moyo wautali mʼzoyipa zake.
16 Не буди сувише праведан ни сувише мудар; зашто би себе упропастио?
Usakhale wolungama kwambiri kapena wanzeru kwambiri, udziwonongerenji wekha?
17 Не буди сувише безбожан ни луд; зашто би умро пре времена?
Usakhale woyipa kwambiri, ndipo usakhale chitsiru, uferenji nthawi yako isanakwane?
18 Добро је да држиш једно, а друго да не пушташ из руке; јер ко се боји Бога избавиће се од свега.
Nʼkwabwino kuti utsate njira imodzi, ndipo usataye njira inayo. Munthu amene amaopa Mulungu adzapewa zinthu ziwiri zonsezi.
19 Мудрост крепи човека више него десет кнезова који су у граду.
Nzeru zimapereka mphamvu zambiri kwa munthu wanzeru kupambana olamulira khumi a mu mzinda.
20 Доиста нема човека праведног на земљи који твори добро и не греши.
Palibe munthu wolungama pa dziko lapansi amene amachita zabwino zokhazokha ndipo sachimwa.
21 Не узимај на ум свашта што се говори, ако би и слугу свог чуо где те псује;
Usamamvetsere mawu onse amene anthu amayankhula, mwina udzamva wantchito wako akukutukwana,
22 Јер срце твоје зна да си и ти више пута псовао друге.
pakuti iwe ukudziwa mu mtima mwako kuti nthawi zambiri iwenso unatukwanapo ena.
23 Све то огледах мудрошћу и рекох: Бићу мудар; али мудрост беше далеко од мене.
Zonsezi ndinaziyesa ndi nzeru zanga ndipo ndinati, “Ine ndatsimikiza mu mtima mwanga kuti ndikhale wanzeru,” koma nzeruyo inanditalikira.
24 Шта је тако далеко и врло дубоко, ко ће наћи?
Nzeru zimene zilipo, zili kutali ndipo ndi zozama kwambiri, ndani angathe kuzidziwa?
25 Окретох се срцем својим да познам и извидим и изнађем мудрост и разум, и да познам безбожност лудости и лудост безумља.
Kotero ndinayikapo mtima wanga kuti ndidziwe, ndifufuze ndi kumafunafuna nzeru ndi mmene zinthu zimakhalira ndipo ndinafunanso kudziwa kuyipa kwa uchitsiru ndiponso kupusa kwake kwa misala.
26 И нађох да је горча од смрти жена којој је срце мрежа и пругло, којој су руке окови; ко је мио Богу, сачуваће се од ње, а грешника ће ухватити она.
Ndinapeza kanthu kowawa kupambana imfa, mkazi amene ali ngati khoka, amene mtima wake uli ngati khwekhwe, ndipo manja ake ali ngati maunyolo. Munthu amene amakondweretsa Mulungu adzathawa mkaziyo, koma mkaziyo adzakola munthu wochimwa.
27 Гле, то нађох, вели проповедник, једно према другом, тражећи да разумем.
Mlaliki akunena kuti, “Taonani, chimene ndinachipeza ndi ichi: “Kuwonjezera chinthu china pa china kuti ndidziwe mmene zinthu zimachitikira,
28 Још тражи душа моја, али не нађох. Човека једног у хиљаде нађох, али жене међу свима не нађох.
pamene ine ndinali kufufuzabe koma osapeza kanthu, ndinapeza munthu mmodzi wolungama pakati pa anthu 1,000, koma pakati pawo panalibepo mkazi mmodzi wolungama.
29 Само, гле, ово нађох: да је Бог створио човека доброг; а они траже свакојаке помисли.
Chokhacho chimene ndinachipeza ndi ichi: Mulungu analenga munthu, anamupatsa mtima wolungama, koma anthu anatsatira njira zawozawo zambirimbiri.”