< 5 Мојсијева 14 >

1 Ви сте синови Господа Бога свог; немојте се резати нити бријати међу очима за мртвацем.
Inu ndinu ana a Yehova Mulungu wanu. Osamadzichekacheka kapena kudzimeta pamphumi chifukwa cha abale anu amene amwalira,
2 Јер си народ свет Господу Богу свом, и тебе изабра Господ да си му народ особит између свих народа на земљи.
pakuti ndinu anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu. Pakati pa anthu onse pa dziko lonse lapansi, Yehova wasankha inu kuti chikhale chuma chake chamtengo wapatali.
3 Не једи ништа гадно.
Musamadye chinthu chilichonse chonyansa.
4 Ово су животиње које ћете јести: говече, овцу, козу,
Nyama zomwe mukhoza kudya ndi izi: ngʼombe, nkhosa, mbuzi,
5 Јелена, срну, бивола, дивокозу, једнорога и козу камењачу;
mbawala, gwape, mphoyo, mphalapala, ngoma, nyumbu ndi mbalale.
6 И све животиње које имају папке расцепљене на двоје, и које преживају између животиња, њих једите.
Nyama iliyonse imene ili ndi chipondero chogawikana pakati ndi yobzikula mukhoza kudya.
7 Али не једите оне које само преживају или које само имају папке расцепљене на двоје, као: камилу, зеца, питомог зеца, јер преживају, а немају папке раздвојене; да вам је нечисто;
Komabe pakati pa nyama zimene zimabzikula kapena zogawikana zipondero, zimene simukuyenera kudya ndi ngamira, kalulu ndi mbira. Zimenezi ngakhale zimabzikula, zipondero zake sizogawikana, choncho ndi zodetsedwa, musadye.
8 Ни свињче, јер има раздвојене папке, али не прежива; да вам је нечисто; месо од њега не једите, и стрва се његовог не дохватајте.
Nkhumba simabzikula ndi yodetsedwanso ngakhale ili ndi zipondero zogawikana. Musamadye nyama yake kapena kukhudza imene yafa.
9 А између оних што су у води, једите ове: шта год има пера и љуске, једите;
Mwa zamoyo zonse zimene zimakhala mʼmadzi, mukhoza kudya chilichonse chimene chili ndi minga ya pa msana ndi mamba.
10 А што нема пера и љуске, не једите; да вам је нечисто.
Koma chilichonse chimene chilibe minga ya pa msana ndi mamba musadye pakuti nʼchodetsedwa.
11 Све птице чисте једите;
Mukhoza kudya mbalame iliyonse yoyenera kudya.
12 А ове не једите: орла, ни јастреба, ни морског орла,
Koma simukuyenera kudya izi: mphungu, nkhwazi, mwimba,
13 Ни сокола, ни еју, ни крагуја по врстама њиховим,
nankapakapa, akamtema, akhungubwi a mitundu yonse, ndi mtundu uliwonse wa miphamba,
14 Ни гаврана по врстама његовим,
mtundu uliwonse wa khwangwala,
15 Ни ћука, ни совуљагу, ни лиску, ни копца по врстама његовим,
kadzidzi wamphondo, kadzidzi wodzuma, chipudo, mtundu uliwonse wa akabawi,
16 Ни буљину, ни ражња, ни лабуда,
kadzidzi wamngʼono, chiswankhono ndi mantchichi,
17 Ни гема, ни свраку, ни гњурца,
tsekwe, vuwo, dembo,
18 Ни роду, ни чапљу по врстама њеним, ни пупавца, ни љиљка.
indwa, zimeza za mitundu yonse, nsadzu ndi mleme.
19 И све бубине крилате да су вам нечисте; не једите их.
Zowuluka zonse za miyendo inayi ndi zodetsedwa. Musamadye zimenezi.
20 И све птице чисте једите.
Koma chowuluka chilichonse choyenera kudya mukhoza kudya.
21 Ништа мрцино не једите; дошљаку који је код тебе подај нека једе, или продај туђину; јер си народ свет Господу Богу свом; не кувај јаре у млеку матере његове.
Musamadye chilichonse chimene mwachipeza chofaifa. Mukhoza kupatsa mlendo amene akukhala mu mzinda wina uliwonse wa mizinda yanu. Iyeyo akhoza kudya kapena mukhoza kugulitsa kwa wina aliyense amene sali wa mtundu wanu. Koma inu ndinu anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu. Musamaphike mwana wambuzi mu mkaka wa mayi wake.
22 Десетак дај од свега рода усева свог, што дође с њиве твоје сваке године.
Muzionetsetsa kuti mukupatula chakhumi pa zokolola zanu chaka chilichonse.
23 И једи пред Господом Богом својим на месту које изабере да онде настани име своје, десетак од жита свог, од вина свог и уља свог, и првине стоке своје крупне и ситне, да се учиш бојати се Господа Бога свог свагда.
Muzidyera chakhumi cha tirigu wanu, vinyo wanu watsopano ndi mafuta, ndi ana oyamba kubadwa a ngʼombe zanu pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa malo amene adzasankhe ngati kokhalako dzina lake, kuti muphunzire kuopa Yehova Mulungu wanu.
24 Ако би ти пут био далек, те не би могао однети зато што је далеко од тебе место, које изабере Господ Бог твој да онде намести име своје, кад те Господ Бог твој благослови,
Koma ngati malo amenewa ali kutali kwambiri ndipo kuti inu mwadalitsidwa ndi Yehova Mulungu wanu, ndipo simungathe kunyamula chakhumi chanu (chifukwa chakuti malo amene Yehova adzasankha kukayikako dzina lake ali kutali kwambiri),
25 Онда ужини у новац, и узевши у руку своју отиди у место које изабере Господ Бог твој,
ndiye musinthitse chakhumi chanucho ndi siliva, ndipo mutenge silivayo ndi kupita naye kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe.
26 И за те новце узми шта зажели душа твоја, говеда, оваца, вина или другог јаког пића, и шта год би зажелела душа твоја, па једи онде пред Господом Богом својим, и весели се ти и дом твој.
Gwiritsani ntchito silivayo kugula chilichonse chimene muchifuna monga ngʼombe, nkhosa, vinyo kapena zakumwa zina zosasitsa, kapena china chilichonse chimene muchifuna. Ndipo inu ndi anthu a pa banja panu mudzazidyera komweko pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kukondwera.
27 Али Левита који би био у месту твом, немој оставити јер нема део ни наследство с тобом.
Alevi okhala mʼmizinda yanu musaleke kuwathandiza popeza alibe gawo lawo la chuma kapena cholowa chawochawo.
28 Сваке треће године одвој сав десетак од доходака својих оне године, и остави га у свом месту.
Kumapeto kwa zaka zitatu zilizonse muzibweretsa zakhumi zonse pa zokolola za chaka chimenecho ndi kuzisunga mʼmidzi yanu,
29 Па нека дођу Левити (јер немају део ни наследство с тобом) и дошљаци и сироте и удовице што су у месту твом, и нека једу и насите се, да би те благословио Господ Бог твој у сваком послу руку твојих, који би радио.
kuti Alevi (amene alibe gawo lawo la chuma kapena cholowa chawochawo), alendo, ana ndi akazi amasiye, amene akukhala mʼmizinda yanu akhoza kubwera kudzadya ndi kukhuta. Ndipo kuti akutero Yehova Mulungu wanu akudalitseni pa ntchito zanu zonse.

< 5 Мојсијева 14 >