< Књига пророка Данила 6 >
1 Свиде се Дарију те постави над царством сто и педесет управитеља да буду над свим царством;
Kunamukomera Dariyo kusankha akalonga 120 kuti alamulire mu ufumu wonse,
2 А над њима три старешине, од којих један беше Данило, којима ће управитељи давати рачуне да не би цару било штете.
ndikusankha nduna zazikulu zitatu kuti ziwayangʼanire ndipo imodzi mwa ndunazo anali Danieli. Akalongawo amayangʼaniridwa ndi nduna zazikuluzo kuti zinthu za mfumu zisawonongeke.
3 А тај Данило надвишиваше старешине и управитеље, јер у њему беше велик дух и цар мишљаше да га постави над свим царством својим.
Tsono Danieli anadzionetsa kuti akhoza kugwira ntchito bwino kopambana nduna zinzake chifukwa anali wanzeru kwambiri. Ndiye mfumu inaganiza zomuyika kuti akhale woyangʼanira ufumu wonse.
4 Тада старешине и управитељи гледаху како би нашли шта да замере Данилу ради царства; али не могаху наћи забаве ни погрешке, јер беше веран, и не налажаше се у њега погрешке ни мане.
Chifukwa cha ichi, anzake ndi akalonga anayesa kupeza zifukwa zomutsutsira Danieli pa kayendetsedwe ka ntchito za dzikolo, koma sanapeze cholakwa chilichonse. Iwo sanapeze chinyengo mwa iye, chifukwa anali wokhulupirika ndipo sankachita chinyengo kapena kutayirira ntchito.
5 Тада рекоше они људи: Нећемо наћи на тог Данила ништа, ако не нађемо шта на њ ради закона Бога његовог.
Pomaliza, anthu awa ananena kuti, “Sitidzapeza cholakwa chilichonse chomutsutsira Danieli kupatula chokhacho chimene chikhudza chipembedzo cha Mulungu wake.”
6 Тада дођоше старешине и управитељи к цару, и рекоше му овако: Дарије царе, да си жив довека!
Choncho akalonga ndi nduna pamodzi anapita kwa mfumu ndipo anati: “Inu mfumu Dariyo, mukhale ndi moyo wautali!
7 Све старешине у царству, поглавари и управитељи, већници и војводе договорише се да се постави царска наредба и оштра забрана да ко би се год замолио за шта коме год богу или човеку за тридесет дана осим теби, царе, да се баци у јаму лавовску.
Nduna zoyendetsa ufumu wanu, aphungu, akalonga ndi abwanamkubwa tonse tagwirizana kuti inu mfumu mukhazikitse lamulo ndi kulisindikiza kuti aliyense amene apemphera kwa mulungu wina kapena kwa munthu kupatula kwa inu mfumu, pa masiku makumi atatu otsatirawa, adzaponyedwa mʼdzenje la mikango.
8 Зато, царе, постави ту забрану и напиши да се не може променити, по закону мидском и персијском, који је непроменљив.
Tsopano inu mfumu khazikitsani lamulo limeneli ndipo musindikizepo dzina lanu kuti lisasinthike monga mwa malamulo a Amedi ndi Aperezi, amene sasinthidwa.”
9 И цар Дарије написа књигу и забрану.
Choncho mfumu Dariyo anasindikizapo dzina lake pa lamuloli.
10 А Данило кад дозна да је књига написана, отиде својој кући, где беху отворени прозори у његовој соби према Јерусалиму, и падаше на колена своја три пута на дан и мољаше се и хвалу даваше Богу свом као шта чињаше пре.
Danieli atamva kuti lamulo lasindikizidwa, anapita ku nyumba kwake nalowa mʼchipinda chapamwamba chimene mazenera ake anali otsekula kuloza ku Yerusalemu. Katatu pa tsiku iye ankagwada pansi pa mawondo ndipo amapemphera, kuyamika Mulungu wake, monga momwe ankachitira kale.
11 Тада се сабраше они људи, и нађоше Данила где се моли и припада Богу свом.
Ndipo anthu awa anapita pamodzi ndi kukapeza Danieli akupemphera ndi kupempha Mulungu wake kuti amuthandize.
12 И отидоше те рекоше цару за царску забрану: Ниси ли написао заповест, да ко би се год замолио коме год богу или човеку за тридесет дана, осим теби, царе, да се баци у јаму лавовску? Цар одговори и рече: Тако је по закону мидском и персијском, који је непроменљив.
Kotero iwo anapita kwa mfumu ndipo anayankhula naye za lamulo lake kuti, “Kodi simunasindikize lamulo lakuti pa masiku makumi atatu otsatirawa aliyense amene apemphera kwa mulungu wina aliyense kapena kwa munthu kupatula kwa inu mfumu, adzaponyedwa mʼdzenje la mikango?” Mfumu inayankha kuti, “Lamulo lilipobe monga mwa malamulo a Amedi ndi Aperezi, amene sangathe kusinthika.”
13 Тада одговорише и рекоше цару: Данило, који је између робља Јудина, не хаје за те, царе, ни за забрану коју си написао, него се моли три пута на дан својом молитвом.
Kenaka iwo anati kwa mfumu, “Danieli, amene ndi mmodzi mwa akapolo ochokera ku Yuda, sakulabadira inu mfumu, kapena lamulo limene munasindikizapo dzina lanu lija. Iye akupempherabe katatu pa tsiku.”
14 Тада цар чувши то ожалости се врло, и науми да избави Данила, и труђаше се до захода сунчаног да га избави.
Mfumu itamva izi, inavutika kwambiri mu mtima mwake. Iyo inayesa kupeza njira yopulumutsira Danieli. Iyo inachita chotheka chilichonse kufikira kulowa kwa dzuwa kuti imupulumutse.
15 Тада они људи сабраше се код цара и рекоше цару: Знај, царе, да је закон у Мидијана и Персијана да се никаква забрана и наредба коју постави цар, не мења.
Ndipo anthuwo anapita pamodzi kwa mfumu ndipo anati kwa iye, “Kumbukirani, inu mfumu kuti monga mwa lamulo la Amedi ndi Aperezi, palibe chimene mfumu inalamulira kapena kukhazikitsa chimasinthidwa.”
16 Тада цар рече те доведоше Данила и бацише га у јаму лавовску; и цар проговори и рече Данилу: Бог твој, коме без престанка служиш, нека те избави.
Choncho mfumu inalamula, ndipo anabwera naye Danieli ndi kukamuponya mʼdzenje la mikango. Mfumu inati kwa Danieli, “Mulungu wako amene umutumikira nthawi zonse, akupulumutse!”
17 И донесоше камен и метнуше јами на врата, и цар га запечати својим прстеном и прстеном својих кнезова да се ништа не промени за Данила.
Anatenga mwala natseka pa khoma pa dzenje la mikango, ndipo mfumu inadindapo chizindikiro chake ndi cha nduna zake kuti wina asasinthepo kanthu pa za Danieli.
18 Тада отиде цар у свој двор, и преноћи не једавши нити допустивши да му се донесе шта чим би се развеселио, и не може заспати.
Kenaka mfumu inabwerera ku nyumba yake ndipo inakhala usiku wonse osadya kanthu, osalola chosangalatsa chilichonse. Ndipo sinagone tulo.
19 Потом цар уста ујутро рано и отиде брже к јами лавовској.
Mʼbandakucha, mfumu inanyamuka ndi kufulumira kupita ku dzenje la mikango lija.
20 И кад дође к јами, викну Данила жалосним гласом; и проговори цар и рече Данилу: Данило, слуго Бога Живога, Бог твој, коме служиш без престанка, може ли те избавити од лавова?
Itayandikira pa dzenjelo, inayitana Danieli moonetsa nkhawa, “Danieli, mtumiki wa Mulungu wa moyo! Kodi Mulungu wako, amene umutumikira nthawi zonse, wakulanditsa ku mikango?”
21 Тада Данило рече цару: Царе, да си жив довека!
Danieli anayankha kuti, “Inu mfumu mukhale ndi moyo wautali!
22 Бог мој посла анђела свог и затвори уста лавовима, те ми не наудише; јер се нађох чист пред Њим, а ни теби царе, не учиних зла.
Mulungu wanga anatumiza mngelo wake, ndipo anatseka pakamwa pa mikango. Iyo sinandivulaze chifukwa Mulungu anaona kuti ndine wosalakwa ndi kutinso sindinakulakwireni inu mfumu.”
23 Тада се цар веома обрадова том, и заповеди да изваде Данила из јаме. И извадише Данила из јаме, и не нађе се ране на њему, јер верова Богу свом.
Mfumu inali ndi chimwemwe chopambana ndipo inalamulira kuti amutulutse Danieli mʼdzenjemo. Ndipo atamutulutsa Danieli mʼdzenjemo, sanapezeke ndi chilonda chilichonse pa thupi lake, chifukwa iye anadalira Mulungu wake.
24 Потом заповеди цар, те доведоше људе који беху оптужили Данила, и бацише у јаму лавовску њих, децу њихову и жене њихове; и још не дођоше на дно јами, а лавови их зграбише и све им кости потрше.
Mwa lamulo la mfumu, anthu onse amene ananeneza Danieli aja anagwidwa ndi kukaponyedwa mʼdzenje la mikango, pamodzi ndi akazi awo ndi ana awo. Ndipo asanafike pansi pa dzenjelo, mikango inawawakha ndi mphamvu ndi kuteketa mafupa awo onse.
25 Тада цар Дарије писа свим народима и племенима и језицима што живљаху у свој земљи: Мир да вам се умножи.
Kenaka mfumu Dariyo inalembera anthu a mitundu yonse, ndi anthu a ziyankhulo zosiyanasiyana a mʼdziko lonse kuti, “Mtendere uchuluke pakati panu!
26 Од мене је заповест да се у свој држави царства мог свак боји и страши Бога Даниловог, јер је Он Бог живи, који остаје довека, и царство се Његово неће расути, и власт ће Његова бити до краја;
“Ndikukhazikitsa lamulo kuti paliponse mʼdziko langa anthu ayenera kuopa ndi kuchitira ulemu Mulungu wa Danieli.
27 Он избавља и спасава, и чини знаке и чудеса на небу и на земљи, Он је избавио Данила од силе лавовске.
Iye amalanditsa ndipo amapulumutsa,
28 И тај Данило беше срећан за царовања Даријевог и за царовања Кира Персијанца.
Choncho Danieli anapeza ufulu pa nthawi ya ulamuliro wa Dariyo ndi ulamuliro wa Koresi wa ku Perisiya.