< 2 Књига Самуилова 16 >

1 А кад Давид пређе мало преко врха, гле, Сива, Мефивостејев, срете га, са два магарца натоварена, на којима беше двеста хлебова и сто гроздова сувих и сто груда смокава и мех вина.
Davide atapitirira pangʼono pamwamba pa phiri, anakumana ndi Ziba mtumiki wa Mefiboseti akudikira kuti akumane naye. Iye anali ndi abulu a chishalo pa msana ndipo ananyamula malofu a buledi 200, ntchintchi 100 za mphesa zowuma, zipatso za pa nthawi yachilimwe 100 ndi thumba la vinyo.
2 И рече цар Сиви: Шта ће ти то? А Сива му рече: Магарци су за чељад цареву, да јашу, а хлебови и воће да једу момци, а вино да пије ко се умори у пустињи.
Mfumu inafunsa Ziba kuti, “Nʼchifukwa chiyani wabweretsa izi?” Ziba anayankha kuti, “Abuluwa ndi oti anthu a mʼbanja mwanu akwerepo, buledi ndi zipatso ndi za anthu anu kuti adye, ndipo vinyoyo ndi woti atsitsimutse anthu amene atope mʼchipululu.”
3 А цар му рече: А где је син твог господара? Рече Сива цару: Ено га, остао је у Јерусалиму, јер рече: Данас ће ми дом Израиљев вратити царство оца мог.
Kenaka mfumu inafunsa kuti, “Kodi chidzukulu cha mbuye wako chili kuti?” Ziba anati kwa iye, “Watsalira ku Yerusalemu chifukwa akuganiza kuti, ‘Lero Aisraeli andibwezera ufumu wa agogo anga.’”
4 Тада рече цар Сиви: Ево, твоје је све што је било Мефивостејево. А Сива рече: Клањам ти се, да нађем милост пред тобом, царе господару!
Ndipo mfumu inati kwa Ziba, “Zonse zimene zinali za Mefiboseti ndi zako tsopano.” Ziba anati, “Ine modzichepetsa ndikukugwandirani, mbuye wanga mfumu, kuti ndipeze chisomo pamaso panu.”
5 И дође цар Давид до Ваурима; а гле, изиђе оданде један од рода дома Сауловог, по имену Симеј, син Гирин, и идући псоваше.
Mfumu Davide itayandikira Bahurimu, munthu wochokera ku fuko limodzi ndi banja la Sauli anabwera kuchokera mʼmenemo. Dzina lake linali Simei, mwana wa Gera ndipo amatukwana pamene amabwera.
6 И бацаше се камењем на Давида и на слуге цара Давида, коме и с десне и с леве стране беше сав народ и сви јунаци.
Iye amagenda Davide miyala ndi akuluakulu onse a mfumu, ngakhale kuti ankhondo onse ndi oteteza Davide anali ali kumanzere ndi kumanja kwake.
7 А Симеј овако говораше псујући: Одлази, одлази, крвопијо и зликовче!
Potukwana, Simeiyo amati, “Choka iwe, choka iwe, munthu wopha anthu, munthu wachabechabe iwe!
8 Обрати Господ на тебе сву крв дома Сауловог, на чије си се место зацарио, и предаде Господ царство у руке Авесалому сину твом; ето те сада у твом злу, јер си крвопија.
Yehova wakubwezera chifukwa cha magazi onse amene unakhetsa pa nyumba ya Sauli, yemwe iwe ukulamulira mʼmalo mwake. Yehova wapereka ufumu kwa mwana wako Abisalomu. Ndipo ona mathero ako ndi amenewa chifukwa ndiwe munthu wopha anthu!”
9 Тада рече цару Ависај син Серујин: Зашто да псује овај мртви пас цара господара мог? Идем да му скинем главу.
Ndipo Abisai mwana wa Zeruya anati kwa mfumu, “Nʼchifukwa chiyani galu wakufa uyu akutukwana mbuye wanga mfumu? Ndiloleni ndipite kuti ndikadule mutu wake.”
10 Али цар рече: Шта је вама до мене, синови Серујини? Нека псује; јер му је Господ рекао: Псуј Давида. Па ко сме казати: Зашто тако чиниш?
Koma mfumu inati, “Inu ana a Zeruya, kodi ndikuchitireni chiyani? Ngati iye akutukwana chifukwa Yehova wamuwuza kuti, ‘Tukwana Davide,’ angafunse ndani kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani ukuchita zimenezi?’”
11 Још рече Давид Ависају и свим слугама својим: Ето, мој син, који је изашао од бедара мојих, тражи душу моју, а како неће овај син Венијаминов? Оставите га нека псује, јер му је Господ заповедио.
Tsono Davide anati kwa Abisai ndi akuluakulu ake onse, “Mwana wanga wobereka ndekha akufuna kundipha. Nanji tsono munthu wa fuko la Benjamini uyu! Musiyeni; mulekeni atukwane pakuti Yehova wachita kumuwuza kuti atero.
12 Да ако Господ погледа на невољу моју, и врати ми Господ добро за псовку његову данашњу.
Mwina Yehova adzaona mazunzo anga ndipo adzandibwezera zabwino chifukwa cha kutukwanidwa kumene ndikulandira lero.”
13 И тако Давид са својим људима иђаше својим путем; а Симеј иђаше покрај горе према њему једнако псујући и бацајући се камењем на њ, и подижући прах.
Kotero Davide ndi anthu ake anapitirira kuyenda mu msewu pamene Simei amayenda mʼmbali mwa phiri moyangʼanana naye akutukwana ndi kuponya miyala pamene amayenda nʼkumamutsiranso dothi.
14 И дође цар и сав народ што беше с њим, уморни, и одморише се онде.
Mfumu ndi anthu ake onse anafika kumene amapita atatopa kwambiri. Ndipo kumeneko anapumula.
15 А Авесалом и сав народ Израиљев дођоше у Јерусалим, и Ахитофел с њим.
Pa nthawi imeneyi Abisalomu ndi Aisraeli ena onse anabwera ku Yerusalemu, Ahitofele anali naye.
16 А кад Хусај Архијанин пријатељ Давидов дође к Авесалому, рече Хусај Авесалому: Да живи цар! Да живи цар!
Tsono Husai Mwariki bwenzi la Davide anapita kwa Abisalomu ndipo anati kwa iye, “Ikhale ndi moyo wautali mfumu! Ikhale ndi moyo wautali mfumu!”
17 А Авесалом рече Хусају: Таква ли је љубав твоја према пријатељу твом? Зашто ниси отишао с пријатељем својим?
Abisalomu anafunsa Husai, “Kodi ichi ndi chikondi chimene ukumuonetsa bwenzi lako? Nʼchifukwa chiyani sunapite ndi bwenzi lako?”
18 А Хусај рече Авесалому: Не; него кога је изабрао Господ и овај народ и сви Израиљци, његов ћу бити и код њега ћу остати.
Husai anati kwa Abisalomu, “Ayi, ndidzakhala wake wa amene Yehova wamusankha, wosankhidwa ndi anthu awa ndi anthu onse a Israeli, ndipo ndidzakhala wake nthawi zonse.
19 Сврх тога, коме бих служио? Еда ли не сину његовом? Како сам служио оцу твом, тако ћу и теби.
Kodi ndidzatumikiranso yani? Kodi sinditumikira mwana wa mfumu? Monga momwe ndinatumikira abambo anu, kotero ndidzatumikiranso inu.”
20 А Авесалом рече Ахитофелу: Саветуј шта ћемо чинити.
Abisalomu anati kwa Ahitofele, “Tiwuze malangizo ako. Kodi tichite chiyani?”
21 А Ахитофел рече Авесалому: Лези с иночама оца свог, које је оставио да му чувају кућу, па кад чује сав Израиљ како си се омразио с оцем својим, осилиће рука свима који су с тобом.
Ahitofele anayankha kuti, “Mugone ndi azikazi a abambo anu amene awasiya kuti asamalire nyumba yaufumu. Aisraeli onse adzamva kuti mwachitira abambo anu chinthu chonyansa kotheratu ndipo anthu onse amene ali ndi iwe adzalimbikitsidwa.”
22 Тада разапеше Авесалому шатор на крову, и Авесалом леже с иночама оца свог на видику свему Израиљу.
Choncho anamangira tenti Abisalomu pa denga la nyumba ndipo iye anagona ndi azikazi a abambo ake Aisraeli onse akuona.
23 И савет који даваше Ахитофел у оно време беше као да би ко Бога упитао; такав беше сваки савет Ахитофелов и у Давида и у Авесалома.
Tsono masiku amenewo malangizo amene Ahitofele amapereka anali ngati mawu ochokera kwa Mulungu. Umu ndi mmene Davide ndi Abisalomu amalandirira malangizo onse a Ahitofele.

< 2 Књига Самуилова 16 >