< 2 Књига о царевима 12 >

1 Седме године Јујеве поче царовати Јоас, и царова четрдесет година у Јерусалиму. Матери му беше име Сивија из Вирсавеје.
Mʼchaka chachisanu ndi chiwiri cha Yehu, Yowasi anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka makumi anayi. Amayi ake anali Zibiya wa ku Beeriseba.
2 И чињаше Јоас што је право пред Господом докле га год учаше свештеник Јодај.
Yowasi anachita zolungama pamaso pa Yehova masiku onse amene wansembe Yehoyada ankamulangiza.
3 Али висине не бише оборене; народ још приношаше жртве и кађаше на висинама.
Komabe sanachotse malo opembedzerapo mafano ndipo anthu anapitiriza kupereka nsembe ndi kufukiza lubani ku malo opembedzerako mafanowo.
4 И Јоас рече свештеницима: Сав новац посвећени, што се доноси у дом Господњи, новац оних који иду у бој, и новац од уцене свачије, и сав новац што ко доноси од своје воље у дом Господњи.
Yowasi anati kwa ansembe, “Tolerani ndalama zonse zimene zimaperekedwa monga chopereka chopatulika ku Nyumba ya Yehova, ndalama zonse zamsonkho wa munthu aliyense, ndalama zomwe munthu amapereka akalonjeza ndiponso ndalama zimene munthu amapereka mwaufulu ku Nyumba ya Yehova.
5 Нека свештеници узимају, сваки од свог познаника, и они нека оправљају што је трошно у дому где се год нађе да треба оправити.
Wansembe aliyense alandire ndalamazo kuchokera kwa abwenzi ake, ndipo zigwiritsidwe ntchito yokonzera chilichonse chimene chipezeke kuti ndi chowonongeka mʼnyumbayo.”
6 Али до године двадесет треће царовања Јоасовог свештеници још не оправише шта беше трошно у дому.
Koma pofika chaka cha 23 cha ufumu wa Yowasi, ansembewo anali asanakonze nyumbayo.
7 Тада цар Јоас дозва Јодаја свештеника и остале свештенике, и рече им: Зашто не оправљате што је трошно у дому? Одселе не узимајте новац од својих познаника, јер треба да вратите да се оправи што је трошно у дому.
Choncho Mfumu Yowasi inayitanitsa wansembe Yehoyada ndi ansembe ena ndipo inafunsa kuti, “Chifukwa chiyani simukukonza malo owonongeka a mʼnyumbayi? Musasungenso ndalama zina zochokera kwa abwenzi anu, koma muzipereke kuti akonzere nyumbayi.”
8 И свештеници присташе да не узимају новац од народа и да не оправљају (они) што је трошно у дому.
Ansembe anavomera kuti salandiranso ndalama kuchokera kwa anthu ndipo kuti sindiwo amene ati akonzenso nyumbayo.
9 Тада свештеник Јодај узе један ковчег, и прореза рупу на заклопцу, и метну га код олтара с десне стране како се улази у дом Господњи; и свештеници који чуваху врата меташе у њ све новце који се доношаху у дом Господњи.
Koma wansembe Yehoyada anatenga bokosi ndipo anabowola chivundikiro chake. Anayika bokosilo pambali pa guwa lansembe, kudzanja lamanja la aliyense amene akulowa mʼNyumba ya Yehovayo. Ansembe amene ankalondera pa khomopo ankaponya mʼbokosi ndalama zonse zimene ankabwera nazo ku nyumba ya Yehova.
10 А кад виђаху да има много новаца у ковчегу, тада долажаше писар царев с поглаваром свештеничким, и избројавши свезиваху новце који би се нашли у дому Господњем.
Nthawi zonse akaona kuti mʼbokosimo muli ndalama zambiri, mlembi wa mfumu ndi mkulu wa ansembe ankabwera ndipo ankawerenga ndalama zomwe anthu ankabwera nazo ku Nyumba ya Yehova ndi kuziyika mʼmatumba.
11 Потом даваху готове новце онима који управљаху послом и стараху се за дом Господњи, а они их издаваху дрводељама и посленицима који оправљаху дом Господњи,
Ankati akadziwa kuti ndalamazo zilipo zingati, ankazipereka kwa anthu amene ankayangʼanira ntchito yokonza nyumbayo. Ndalamazo ankalipira anthu amene ankagwira ntchito yokonza Nyumba ya Yehova, amisiri a matabwa ndi amisiri omanga nyumba,
12 И зидарима и каменарима, и да се добавља дрво и тесано камење, да се оправи шта беше трошно у дому Господњем, и да се добави све што требаше да се оправи дом.
amisiri a miyala ndiponso anthu ophwanya miyala. Iwo ankagula matabwa ndi miyala yosema yokonzera Nyumba ya Yehova ndipo ankalipira zinthu zonse zofunika pokonzanso nyumbayo.
13 Али новцима који доношаху у дом Господњи не грађаху чаша сребрних за дом Господњи, ни виљушака, ни котлића, ни труба, нити каквих судова златних ни сребрних;
Koma ndalama zomwe anthu ankabwera nazo ku nyumbayo sanagulire siliva wopangira mabeseni, zozimitsira nyale, mbale zowazira magazi, malipenga kapena ziwiya zina zilizonse zagolide kapena zasiliva za ku Nyumba ya Yehova.
14 Него их даваху онима који беху над послом да се оправи за њих дом Господњи.
Ndalamazi anazipereka kwa anthu antchito amene anazigwiritsa ntchito yokonzera nyumbayo.
15 И не тражаху рачуна од људи којима предаваху новце да издају посленицима, јер верно рађаху.
Koma sanawafunse kuti afotokoze kagwiritsidwe ntchito ka ndalama zolipira amene ankagwira ntchito, chifukwa anthuwo ankagwira ntchitoyo mokhulupirika kwambiri.
16 Новци за преступ и новци за грехе не доношаху се у дом Господњи; припадаху свештеницима.
Ndalama zomwe zinkaperekedwa pa nsembe yopepesera machimo ndi nsembe yoperekedwa chifukwa cha tchimo sanabwere nazo ku Nyumba ya Yehova pakuti zinali za ansembe.
17 Тада изађе Азаило, цар сирски, и удари на Гат и узе га; потом се окрете Азаило да иде на Јерусалим.
Pa nthawi imeneyo, Hazaeli, mfumu ya Aramu anapita kukathira nkhondo mzinda wa Gati nawulanda. Kenaka Hazaeli anatembenuka kupita kukathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu.
18 А Јоас, цар Јудин узе све посвећене ствари, што Јосафат и Јорам и Охозија, оци његови цареви Јудини, беху посветили, и све што сам беше посветио, и све злато што се нађе у ризницама дома Господњег и дома царевог, и посла Азаилу цару сирском; и тако отиде од Јерусалима.
Koma Yowasi mfumu ya Yuda anatenga zinthu zonse zopatulika zomwe anazipatula Yehosafati, Yehoramu, ndi Ahaziya abambo ake, mafumu a Yuda ndi mphatso zonse zomwe iye mwini anazipereka: golide yense amene anapezeka mʼnyumba yosungiramo chuma cha mʼnyumba ya Yehova ndi zomwe zinali mʼnyumba ya mfumu, nazipereka kwa Hazaeli mfumu ya Aramu. Pamenepo iye anachoka ku Yerusalemuko.
19 А остала дела Јоасова и све што је чинио, није ли то записано у дневнику царева Јудиних?
Ndipo ntchito zina za Yowasi ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
20 А слуге његове подигоше се и побунише се, и убише Јоаса у дому Милону, куда се иде у Силу.
Akuluakulu ake anamuchitira chiwembu ndi kumupha ku Beti Milo, pa njira yotsikira ku Silo.
21 Јоазахар, син Симеатов и Јозавад син Сомиров, слуге његове, убише га, те умре; и погребоше га код отаца његових у граду Давидовом; а на његово место зацари се Амасија, син његов.
Yozakara mwana wa Simeati ndi Yehozabadi mwana wa Someri atumiki ake anamukantha nafa. Ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Amaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< 2 Књига о царевима 12 >