< 1 Књига Самуилова 1 >
1 Беше један човек из Раматајим-Софима, из горе Јефремове, коме име беше Елкана син Јероама, сина Елива, сина Това, сина Суфовог, Ефраћанин.
Panali munthu wina wochokera ku Ramataimu, Mzofimu wa ku dziko la mapiri la Efereimu. Iyeyu dzina lake anali Elikana ndipo anali mwana wa Yerohamu, mwana wa Elihu, mwana wa Tohu, mwana wa Zufu wa fuko la Efereimu.
2 И имаше две жене, једној беше име Ана а другој Фенина; и Фенина имаше деце, а Ана немаше деце.
Iye anali ndi akazi awiri, Hana ndi Penina. Penina anali ndi ana, koma Hana analibe.
3 И иђаше тај човек сваке године из свог града да се поклони и принесе жртву Господу над војскама у Силом; а онде беху два сина Илијева, Офније и Финес, свештеници Господњи.
Chaka ndi chaka Elikana ankachoka ku mudzi kwawo kupita ku Silo kukapembedza ndi kukapereka nsembe kwa Yehova Wamphamvuzonse. Ku Siloko kunali ana awiri a Eli, Hofini ndi Finehasi amene anali ansembe a Yehova.
4 И један дан кад Елкана принесе жртву, даде Фенини жени својој и свим синовима њеним и кћерима њеним по део;
Tsiku lopereka nsembe likafika Elikana amapereka magawo a nsembeyo kwa mkazi wake Penina ndi kwa ana ake onse aamuna ndi aakazi.
5 Ани пак даде два дела, јер љубљаше Ану, а њој Господ беше затворио материцу.
Ngakhale ankamukonda Hana, koma ankamupatsa gawo limodzi popeza Yehova sanamupatse ana.
6 И противница је њена врло цвељаше пркосећи јој што јој Господ беше затворио материцу.
Tsono popeza Yehova sanamupatse Hana ana, mkazi mnzakeyo ankamuyamba dala ndi cholinga chomukwiyitsa.
7 Тако чињаше Елкана сваке године, и Ана хођаше у дом Господњи, а она је цвељаше, те плакаше и не јеђаше.
Izi zimachitika chaka ndi chaka. Hana ankati akamapita ku Nyumba ya Yehova mkazi mnzakeyo ankamunyogodola. Choncho Hana ankangokhalira kulira osafuna ndi kudya komwe.
8 А Елкана муж њен рече јој једном: Ана, зашто плачеш? И зашто не једеш? И зашто је срце твоје невесело? Нисам ли ти ја бољи него десет синова?
Tsono mwamuna wake Elikana ankamufunsa kuti, “Hana ukulira chifukwa chiyani? Wakhumudwa ndi chiyani kuti sukufuna ndi kudya komwe? Kodi ine kwa iwe sindili woposa ana aamuna khumi?”
9 А Ана уста, пошто једоше и пише у Силому; а Илије свештеник сеђаше на столици, на прагу дома Господњег.
Tsiku lina atatha kudya ndi kumwa ku Silo kuja, Hana anayimirira kukapemphera. Nthawiyi nʼkuti wansembe Eli atakhala pa mpando pa khomo la Nyumba ya Yehova.
10 И она, тужна у срцу помоли се Господу плачући много.
Hana anavutika mʼmoyo mwake, ndipo anapemphera kwa Yehova akulira kwambiri.
11 И заветова се говорећи: Господе над војскама! Ако погледаш на муку слушкиње своје, и опоменеш ме се, и не заборавиш слушкиње своје, него даш слушкињи својој мушко чедо, ја ћу га дати Господу докле је год жив, и бритва неће прећи преко главе његове.
Ndipo iye analumbira kuti, “Inu Yehova Wamphamvuzonse, ngati muyangʼana kusauka kwa mtumiki wanune, ndi kuyankha pemphero langa osandiyiwala ine mtumiki wanu pondipatsa mwana wamwamuna, ine ndidzamupereka mwanayo kwa inu Yehova masiku onse a moyo wake. Lumo silidzapita pa mutu pake.”
12 И кад се она дуго мољаше пред Господом, Илије мотраше на уста њена.
Akupemphera choncho kwa Yehova, Eli ankamuyangʼana pakamwa.
13 Али Ана говораше у срцу свом, уста јој се само мицаху а глас јој се не чујаше; стога Илије помисли да је пијана.
Hana ankapemphera chamumtima ndipo milomo yake inkangogwedera koma mawu ake samamveka. Choncho Eli anaganiza kuti anali ataledzera.
14 Па јој рече Илије: Докле ћеш бити пијана? Отрезни се од вина свог.
Ndipo anamufunsa Hana kuti, “Kodi mukhala chiledzerere mpaka liti? Pitani, ayambe wakuchokani vinyo mwamwayo.”
15 Али Ана одговори и рече: Нисам пијана, господару, него сам жена тужна у срцу; нисам пила вина ни силовитог пића; него изливам душу своју пред Господом.
Koma Hana anayankha kuti, “Sichoncho mbuye wanga. Ndakhala ndikumukhuthulira Yehova chisoni changa. Sindinamwe vinyo kapena chakumwa choledzeretsa chilichonse, popeza nthawi yonseyi ndakhala ndikupereka kwa Yehova nkhawa yayikulu ndi mavuto anga.
16 Немој једначити слушкиње своје с неваљалом женом; јер сам од велике туге и жалости своје говорила досад.
Musaganize kuti mtumiki wanu ndi kukhala mkazi wachabechabe. Ine ndakhala ndi kupereka nkhawa yanga yayikulu ndi zowawa zanga.”
17 Тада одговори Илије и рече: Иди с миром; а Бог Израиљев да ти испуни молбу, за шта си Га молила.
Eli anayankha, “Pitani mu mtendere, ndipo Mulungu wa Israeli akupatseni zimene mwamupemphazo.”
18 А она рече: Нека нађе слушкиња твоја милост пред тобом! Тада отиде жена својим путем, и једе, и лице јој не беше више као пре.
Hana anati, “Mundikomerebe mtima mtumiki wanune.” Kenaka anachoka nakadya, ndipo sanaonekenso wachisoni.
19 И сутрадан уранише, и поклонише се Господу, и вратише се и дођоше кући својој у Рамат. И Елкана позна Ану жену своју, и Господ се опомену ње.
Elikana ndi banja lake anadzuka mmawa mwake nakapemphera pamaso pa Yehova. Pambuyo pake anabwerera kwawo ku Rama. Elikana anakhala pamodzi ndi mkazi wake, ndipo Yehova anamukumbuka Hanayo.
20 И кад би време, пошто Ана затрудне, роди сина и наде му име Самуило, јер, рече, испросих га у Господа.
Motero Hana anakhala ndi pakati ndipo anabereka mwana wamwamuna. Anamutcha dzina lake Samueli, popeza anati, “Ndinachita kumupempha kwa Yehova.”
21 Потом пође онај човек Елкана са свим домом својим да принесе Господу годишњу жртву и завет свој.
Elikana ndi banja lake lonse anapita kukapereka nsembe ya pa chaka kwa Yehova ndi kukakwaniritsa malonjezo ake.
22 Али Ана не пође, јер рече мужу свом: Докле одојим дете, онда ћу га одвести да изађе пред Господа и остане онде до века.
Koma Hana sanapite nawo popeza anawuza mwamuna wake kuti, “Mwanayu akadzaleka kuyamwa, ndidzapita naye ndi kukamupereka pamaso pa Yehova ndipo adzakhala kumeneko moyo wake wonse.”
23 И рече јој Елкана, муж њен: Чини како ти драго; остани докле год не одојиш; само да хоће Господ испунити реч своју. И тако жена оста; и дојаше сина свог докле га не одоји.
Elikana mwamuna wake anamuwuza kuti, “Chita chimene chakukomera. Tsala kuno mpaka utamusiyitsa kuyamwa, Yehova yekha akwaniritse mawu ake.” Choncho mkaziyo anatsala ku nyumba ndi kusamalira mwana wake mpaka atamuletsa kuyamwa.
24 А кад га одоји, одведе га са собом узевши три телета и ефу брашна и мех вина, и уведе га у дом Господњи у Силому; а дете беше још мало.
Atamuletsa kuyamwa, Hana anatenga mwanayo ali wachichepere, ndikupita naye ku nyumba ya Yehova ku Silo. Anatenga ngʼombe yamphongo ya zaka zitatu, ufa wa makilogalamu khumi, ndi thumba lachikopa la vinyo.
25 И заклаше теле и доведоше дете к Илију.
Tsono anapha ngʼombe yamphongo ija ndi kupereka mwana uja kwa Eli.
26 И она рече: Чуј господару, како је жива душа твоја, господару, ја сам она жена која је стајала овде код тебе молећи се Господу.
Ndipo Hana anati kwa Eli, “Mbuye wanga, ine ndikunenetsadi pamaso panu kuti ndine mkazi uja amene anayima pamaso panu ndi kumapemphera kwa Yehova.
27 Молих се за ово дете, и испуни ми Господ молбу моју, за шта сам Га молила.
Ndinapempha mwana uyu, ndipo Yehova wandipatsa chimene ndinamupempha.
28 Зато и ја дајем њега Господу, докле је год жив, да је дат Господу. И поклонише се онде Господу.
Ndiye tsopano ine ndikumupereka kwa Yehova. Pa moyo wake wonse adzakhala wa Yehova.” Ndipo onse anapembedza Yehova kumeneko.