< 1 Књига Самуилова 3 >

1 А дете Самуило служаше Господу пред Илијем; и реч Господња беше ретка у оно време, и не јављаху се утваре.
Samueli ankatumikira Yehova moyangʼaniridwa ndi Eli. Masiku amenewo mawu a Yehova sankamveka pafupipafupi. Kuona zinthu mʼmasomphenya sikunkachitikanso kawirikawiri.
2 Једном у то време Илије лежаше на свом месту; а очи му почињаху тамнети те не могаше видети.
Tsiku lina Eli, amene maso anali ofowoka ndi kuti sankatha kuona bwino, anagona pa malo ake.
3 И Самуило лежаше у дому Господњем где беше ковчег Божји, и жишци Господњи још не беху погашени.
Nthawiyi nʼkuti nyale ya Mulungu isanazimitsidwe. Samueli anali gone mu Nyumba ya Yehova, kumene kunali Bokosi la Chipangano cha Mulungu.
4 И викну Господ Самуила, а он рече: Ево ме.
Yehova anayitana Samueli. Iye anayankha kuti, “Wawa.”
5 И притрча к Илију, и рече му: Ево ме, што си ме звао? А он рече: Нисам те звао, иди лези. И он отиде и леже.
Ndipo iyeyo anathamangira kwa Eli ndipo anati, “Ndabwera ndamva kuyitana.” Koma Eli anati, “Ine sindinakuyitane, bwerera kagone.” Ndipo iye anapita kukagona.
6 А Господ опет викну Самуила, и Самуило уста, и отиде к Илију, и рече: Ево ме, што си ме звао? А он рече: Нисам те звао, сине; иди лези.
Yehova anayitananso, “Samueli!” Ndipo Samueli anadzuka ndi kupita kwa Eli nati, “Ndabwera popeza ndamva mukundiyitana.” Eli nati, “Mwana wanga, ine sindinakuyitane, bwerera kagone.”
7 А Самуило још не познаваше Господа, и још му не беше јављена реч Господња.
Nthawiyi nʼkuti Samueli asanadziwe Yehova ndipo Mawu a Yehova nʼkuti asanawululidwe kwa iye.
8 Тада опет викну Господ Самуила трећи пут, и он уста и отиде к Илију, и рече: Ево ме, што си ме звао? Тада разуме Илије да Господ зове дете.
Yehova anayitananso Samueli kachitatu ndipo Samueli anadzuka ndikupita kwa Eli ndipo anati, “Ndabwera popeza mwandiyitana ndithu.” Apo Eli anazindikira kuti Yehova ndiye ankayitana mnyamatayo.
9 И рече Илије Самуилу: Иди лези; а ако те зовне, а ти реци: Говори Господе, чује слуга твој. И Самуило отиде, и леже на своје место.
Tsono Eli anamuwuza Samueli kuti, “Pita ukagone ndipo akakuyitananso ukanene kuti, ‘Yankhulani Yehova, pakuti mtumiki wanu ndikumvetsera.’” Choncho Samueli anapita ndi kukagona pamalo pake.
10 А Господ дође и стаде; и зовну као пре: Самуило! Самуило! А Самуило рече: Говори, чује слуга твој.
Yehova anabwera ndi kuyima pomwepo, ndi kuyitana monga nthawi zina zija, “Samueli! Samueli!” Ndipo Samueli anayankha, “Yankhulani, pakuti mtumiki wanu akumvetsera.”
11 И рече Господ Самуилу: Ево учинићу нешто у Израиљу да ће зујати оба уха свакоме ко чује.
Ndipo Yehova anati kwa Samueli, “Taona, patsala pangʼono kuti ndichite chinthu china mu Israeli chimene chidzadabwitsa aliyense amene adzamve.
12 У тај дан ћу учинити Илију све што сам говорио за кућу његову, од почетка до краја.
Tsiku limenelo ndidzachitadi zonse zimene ndinayankhula zokhudza banja la Eli kuyambira poyamba mpaka pomaliza.
13 Јер сам му јавио да ћу судити дому његовом довека за неваљалство, за које је знао да њим навлаче на се проклетство синови његови, па им није забранио.
Pakuti ndinamudziwitsa kuti Ine ndikhoza kulanga banja lake kwamuyaya chifukwa cha zoyipa zimene ana ake ankadziyipitsa nazo. Iye ankadziwa zimenezi koma osawaletsa.
14 Зато се заклех дому Илијевом да се неће очистити неваљалство дома Илијевог никаквом жртвом ни приносом довека.
Nʼchifukwa chake ndinalumbira kuti, ‘Zoyipa zimene banja la Eli linandichita sizidzafafanizidwa mpaka muyaya ngakhale adzapereke nsembe kapena zopereka zina.’”
15 И Самуило спава до јутра, па отвори врата дома Господњег. Али се бојаше Самуило казати Илију за утвару.
Samueli anagona mpaka mmawa. Atadzuka anatsekula zitseko za Nyumba ya Yehova. Iye anachita mantha kumuwuza Eli za masomphenya ake.
16 А Илије зовну Самуила и рече: Самуило, сине! А он рече: Ево ме.
Koma Eli anamuyitana nati, “Samueli mwana wanga.” Samueli anayankha kuti, “Wawa.”
17 А он рече: Какве су речи што ти је казао? Немој затајити од мене; тако ти учинио Бог и тако ти додао, ако затајиш од мене шта год ти је казао.
Tsono Eli anafunsa kuti, “Yehova wakuwuza chiyani? Usandibisire. Mulungu akulange ndithu ngati undibisira chilichonse cha zimene wakuwuza.”
18 И Самуило му каза све, и ништа не затаји од њега. А он рече: Господ је, нека чини оно што Му је воља.
Choncho Samueli anamuwuza zonse, sanamubisire kalikonse. Ndipo Eli anati, “Iye ndi Yehova, mulekeni achite chimene chamukomera.”
19 А Самуило растијаше, и Господ беше с њим, и не пусти да падне на земљу ниједна реч његова.
Yehova anali ndi Samueli pamene amakula, ndipo zonse zimene ankayankhula zinkachitikadi.
20 И сав Израиљ од Дана до Вирсавеје позна да је Самуило веран пророк Господњи.
Ndipo Aisraeli onse kuyambira ku dera la Dani mpaka ku Beeriseba anazindikira kuti Yehova analozadi chala pa Samueli kuti akhale mneneri wake.
21 И Господ се стаде опет јављати у Силому, јер се Господ јављаше Самуилу у Силому речју Господњом.
Yehova anapitiriza kuoneka ku Silo, ndipo kumeneko anadziwulula yekha kwa Samueli mwa mawu ake.

< 1 Књига Самуилова 3 >