< 1 Књига Самуилова 20 >

1 А Давид побеже из Најота у Рами, и дође и рече Јонатану: Шта сам учинио? Каква је кривица моја? И шта сам згрешио оцу твом, те тражи душу моју?
Tsono Davide anathawa ku Nayoti ku Rama ndi kupita kwa Yonatani ndipo anamufunsa kuti, “Kodi ine ndinachita chiyani? Kodi ndinalakwa chiyani? Kodi abambo ako ndinawalakwira chiyani kuti azifuna kundipha?”
2 А он му рече: Сачувај Боже! Нећеш ти погинути. Ево отац мој не чини ништа, ни велико ни мало, а да мени не каже; а како би то тајио од мене отац мој? Неће то бити.
Yonatani anayankha kuti, “Sizitheka! Iwe sufa ayi! Taona abambo anga sachita chinthu chilichonse chachikulu kapena chachingʼono wosandiwuza ine. Tsopano abambo anga angandibisire bwanji zimenezi? Sichoncho ayi.”
3 А Давид заклињући се опет рече: Отац твој зна добро да сам нашао љубав у тебе, па вели: Не треба да дозна за ово Јонатан, да се не ожалости. Али тако жив био Господ и тако жива била душа твоја, само је један корак између мене и смрти.
Koma Davide analumbira kuti, “Abambo ako akudziwa bwino lomwe kuti iwe umandikonda ndipo iwo amaganiza kuti, Yonatani sayenera kudziwa zimenezi mwina adzamva chisoni kwambiri. Komabe, pali Yehova ndi pali iwe, imfa sinanditalikire.”
4 А Јонатан рече Давиду: Шта жели душа твоја? Ја ћу ти учинити.
Yonatani anawuza Davide kuti, “Chilichonse chimene iwe ukufuna kuti ndichite, ndidzakuchitira.”
5 И Давид рече Јонатану: Ево сутра је младина, кад треба с царем да једем, пусти ме дакле да се сакријем у пољу до треће вечери.
Ndipo Davide anati, “Taona mawa ndi tsiku la chikondwerero cha mwezi watsopano, ndipo ine ndiyenera kukadya ndi mfumu. Koma undilole ndipite ndikabisale mʼmunda mpaka mkuja madzulo.
6 Ако запита за ме отац твој, ти реци: Врло ми се молио Давид да отрчи у Витлејем град свој, јер је онде годишња жртва свега рода његовог.
Ngati abambo ako akafunsa za ine, ukawawuze kuti, ‘Davide anandiwumiriza kuti ndimulole apite msanga kwawo ku Betelehemu, chifukwa akupereka nsembe yapachaka ya banja lonse.’
7 Ако каже: Добро, биће миран слуга твој; ако ли се разгневи, знај да је зло наумио.
Akanena kuti, ‘Wachita bwino,’ ndiye kuti zinthu zindiyendera bwino ine mtumiki wako. Koma ngati akapsa mtima, ndiye udziwe kuti iwo atsimikiza zondichita zoyipa.
8 Учини, дакле, милост слузи свом, кад си веру Господњу ухватио са слугом својим; ако је каква кривица на мени, убиј ме сам, јер зашто би ме водио к оцу свом?
Koma undikomere mtima ine mtumiki wako, pakuti unapangana nane pangano pamaso pa Yehova. Ngati ndine wolakwa undiphe ndiwe, koma usandipereke kwa abambo ako.”
9 А Јонатан му рече: Боже сачувај; јер да дознам да је отац мој наумио зло да те задеси, зар ти не бих јавио?
Yonatani anati, “Sizitheka! Ndikanadziwa kuti abambo anga atsimikiza kuti akuchite choyipa, kodi sindikanakuwuza?”
10 А Давид рече Јонатану: Ко ће ми јавити ако ти отац одговори шта је зло?
Davide anafunsa kuti, “Adzandiwuza ndani ngati abambo ako akuyankhe mwaukali?”
11 А Јонатан рече Давиду: Ходи да изађемо у поље. И изиђоше обојица у поље.
Yonatani anawuza Davide kuti, “Tiyeni tikayende ku mundako.” Ndipo anapita onse awiri.
12 И Јонатан рече Давиду: Господе Боже Израиљев! Кад искушам оца свог сутра у ово доба или прекосутра, и буде добро по Давида, ако не пошаљем к теби и не јавим ти,
Kenaka Yonatani anawuza Davide kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akhale mboni! Ine ndikadzafunsa abambo anga nthawi yonga ino mmawa kapena mkuja, ndipo ndikadzapeza kuti akukufunira zabwino, ine ndidzatuma mawu kuti udziwe.
13 Нека Господ учини тако Јонатану и тако нека дода. Ако ли отац мој буде наумио да ти учини зло, ја ћу ти јавити, и оправићу те, и отићи ћеш с миром; и Господ нека буде с тобом као што је био с оцем мојим.
Koma ngati abambo anga atsimikiza kukuchita choyipa, Yehova andilange ine Yonatani, ndipotu kwambiri ngati sindidzakudziwitsa ndi kukulola kuti upite mu mtendere. Yehova akhale nawe monga anakhalira ndi abambo anga.
14 А и ти, докле сам жив, чинићеш мени милост Господњу да не погинем;
Ndikakhalabe ndi moyo udzandionetse kukoma mtima monga kwa Yehova nthawi yonse ya moyo wanga, kuti ine ndisaphedwe.
15 И нећеш ускратити милости своје дому мом довека, ни онда кад Господ истреби све непријатеље Давидове са земље.
Ndipo usadzaleke kuchitira chifundo banja langa. Pamene Yehova adzawatha adani onse a Davide pa dziko lapansi.”
16 Тако Јонатан учини веру с домом Давидовим говорећи: Господ нека тражи из руку непријатеља Давидових.
“Dzina la ine Yonatani lisadzafafanizidwe nawo pamodzi. Yehova alange adani onse a Davide.”
17 И још закле Јонатан Давида љубављу својом к њему, јер га љубљаше као своју душу
Kenaka Yonatani anamulumbiritsanso Davide kuti asaleke kumukonda, pakuti ankamukonda monga ankadzikondera yekha.
18 Потом рече му Јонатан: Сутра је младина, и питаће се за те, јер ће твоје место бити празно.
Kenaka Yonatani anawuzanso Davide kuti, “Mawa ndi tsiku la chikondwerero cha mwezi watsopano. Zidzadziwika kuti iwe palibe chifukwa mpando wako udzakhala wopanda munthu.
19 А ти чекај до трећег дана, па онда отиди брзо и дођи на место где си се био сакрио кад се ово радило, и седи код камена Езила.
Mkuja adzakufunafuna. Tsono udzapite pamalo pamene unabisala poyamba paja ndipo ukadikire pa mulu wa miyala uli apowo.
20 А ја ћу бацити три стреле украј тог камена, као да гађам белегу.
Ine ndidzaponya mivi itatu pambali pake, ngati ndikulasa chinthu.
21 И ево послаћу момка говорећи му: Иди, нађи стреле. Ако кажем момку: Ето стреле су за тобом овамо ближе, дигни их; тада дођи, добро је по те, и неће ти бити ништа, тако жив био Господ!
Ndipo ndidzatuma mnyamata ndi kuti, ‘Pita ukatole miviyo!’ Ngati ndidzanena kwa iye kuti, ‘Taona, mivi ili mbali yakuno, kayitole,’ iwe ukatuluke, pakuti ndikulumbira, pali Yehova Wamoyo, ndiye kuti zako zili bwino, palibe choopsa chilichonse.
22 Ако ли овако кажем момку: Ето стреле су пред тобом, тамо даље; онда иди, јер те Господ шаље.
Koma ndikadzati, ‘Taona mivi ili patsogolo pako,’ iwe udzachoke chifukwa Yehova ndiye walola kuti uchokepo.
23 А за ове речи што рекосмо ја и ти, ево, Господ је сведок између мене и тебе довека.
Tsono zimene tapanganazi Yehova ndiye mboni pakati pa iwe ndi ine mpaka muyaya.”
24 Потом се Давид сакри у пољу; и дође младина, и цар седе за сто да једе.
Choncho Davide anakabisala mʼmunda ndipo nthawi ya chikondwerero cha mwezi watsopano itakwana mfumu Sauli anadzakhala pansi kuti adye.
25 А кад цар седе на своје место, по обичају на место код зида, Јонатан уста, а Авенир седе до Саула, а место Давидово беше празно.
Iye anakhala pa malo ake a nthawi zonse pafupi ndi khoma moyangʼanana ndi Yonatani, ndipo Abineri anakhala moyandikana ndi Sauli, koma pa malo a Davide panalibe munthu.
26 И Саул не рече ништа онај дан, јер мишљаше, догодило му се штагод, те није чист, зацело није чист.
Sauli sananene chilichonse tsiku limenelo pakuti ankaganiza kuti “Chilipo chimene chachitika ndi Davide. Mwina mwake ngosayenera za chipembedzo.”
27 А сутрадан, други дан месеца, опет беше празно место Давидово, а Саул рече Јонатану сину свом: Зашто син Јесејев не дође на обед ни јуче ни данас?
Koma pa tsiku lachiwiri la chikondwerero cha mwezi watsopano pamalo pa Davide panalibenso munthu. Kenaka Sauli anafunsa Yonatani kuti, “Nʼchifukwa chiyani mwana wa Yese sanabwere kudzadya, dzulo ngakhale lero?”
28 А Јонатан одговори Саулу: Врло ме је молио Давид да отиде до Витлејема,
Yonatani anayankha kuti, “Davide anandiwumiriza kuti ndimulole kuti apite ku Betelehemu.
29 Рекавши: Пусти ме, јер породица наша има жртву у граду, и сам ми је брат заповедио; ако сам, дакле, нашао милост пред тобом, да отидем и видим браћу своју. Зато није дошао на царев обед.
Anati, ‘Undilole ndipite, chifukwa banja lathu likupereka nsembe mu mzindamo ndipo mʼbale wanga wandiwumiriza kuti ndikakhale nawo. Ngati wandikomera mtima, chonde ndilole ndipite ndikaone abale anga.’ Nʼchifukwa chake sanabwere kudzadya ndi mfumu.”
30 Тада се разгневи Саул на Јонатана, те му рече: Неваљали и непослушни сине! Зар ја не знам да си изабрао сина Јесејевог себи на срамоту и на срамоту својој неваљалој мајци?
Sauli anamupsera mtima Yonatani ndipo namuwuza kuti, “Iwe mwana wobadwa mwa mkazi wamakhalidwe oyipa ndi wowukira! Kodi ukuyesa kuti ine sindikudziwa kuti umagwirizana ndi mwana wa Yese, amene akufuna kukuchititsa manyazi iwe ndi amayi ako?
31 Јер, докле је жив син Јесејев на земљи, нећеш се утврдити ни ти ни царство твоје; зато пошљи сада и доведи га к мени, јер је заслужио смрт.
Mwana wa Yese akakhala ndi moyo pa dziko lapansi lino, iwe sudzakhala mfumu. Tsopano tumiza munthu akamutenge kubwera naye kwa ine, pakuti Davide ayenera kufa basi!”
32 А Јонатан одговори Саулу оцу свом и рече му: Зашто да се погуби? Шта је учинио?
Yonatani anafunsa abambo ake kuti, “Nʼchifukwa chiyani mufuna kuti Davide aphedwe? Iye walakwa chiyani?”
33 Тада се Саул баци копљем на њ да га убије. Тада виде Јонатан да је отац његов наумио убити Давида.
Apo Sauli anamuponyera mkondo wake kuti amuphe. Tsono Yonatani anadziwa kuti abambo ake atsimikiza mtima kuti aphe Davide.
34 И уста Јонатан од стола његовог, и ништа не једе други дан по младини; јер се забрину за Давида, што га отац осрамоти.
Yonatani anachoka pa tebulopo ali wopsa mtima kwambiri. Tsiku lachiwiri la chikondwererocho Yonatani sanadye chakudya. Iye anawawidwa mtima chifukwa abambo ake anatsimikiza zakupha Davide.
35 А кад би ујутру, изађе Јонатан у поље у време како беше уговорио с Давидом, и с њим једно момче.
Tsono mmawa Yonatani anapita ku munda kumene anapangana ndi Davide. Anali ndi mnyamata wake.
36 И рече момку свом: Трчи да ми нађеш стреле које ћу пустити. И момче отрча, а он пусти стрелу преко њега.
Tsono anawuza mnyamatayo kuti, “Thamanga ukatole muvi umene nditi ndiponye.” Mnyamatayo akuthamanga Yonatani anaponya muvi patsogolo pa mnyamatayo.
37 А кад дође момак до места куда беше застрелио Јонатан, викну Јонатан за момком говорећи: Није ли стрела даље напред?
Mnyamatayo atafika pamene muvi wa Yonatani unagwera,
38 Још викну Јонатан за момком: Брже, не стој. И момак Јонатанов покупи стреле, и врати се господару свом.
Yonatani anayitananso mnyamatayo kuti, “Fulumira, pita msanga usayime.” Choncho mnyamatayo anatola muvi uja ndi kubwera nayo kwa mbuye wake.
39 Али момак не знаше ништа, само Јонатан и Давид знаху шта је.
(Mnyamatayo sanadziwe chimene chimachitika koma Yonatani ndi Davide ndiwo ankadziwa).
40 И Јонатан даде оружје своје момку који беше с њим, и рече му: Иди, однеси у град.
Pambuyo pake Yonatani anapereka zida zake za nkhondo kwa mnyamatayo ndipo anati, “Pita, nyamula ubwerere nazo ku mzinda.”
41 И кад момак отиде, Давид уста с јужне стране и паде ничице на земљу, и поклони се три пута, и пољубише се, и плакаше обојица, а Давид особито.
Mnyamatayo anapita. Kenaka Davide anatuluka ku mbali ina ya mulu wa miyala uja, nadzigwetsa pansi ndi kugunditsa nkhope yake pansi katatu. Anapsompsona nayamba kulira onse awiri, koma Davide analira kwambiri.
42 И рече Јонатан Давиду: Иди с миром, као што смо се заклели обојица именом Господњим рекавши: Господ да је сведок између мене и тебе и између мог семена и твог семена довека. И тако Давид уставши отиде, а Јонатан се врати у град.
Yonatani anawuza Davide kuti, “Pita mu mtendere pakuti ife awiri tinalumbira mʼdzina la Yehova kuti, ‘Yehova ndiye akhale mboni pakati pa iwe ndi ine ndiponso pakati pa zidzukulu zako ndi zidzukulu zanga kwa nthawi yonse.’” Kenaka Davide anachoka, ndipo Yonatani anabwerera ku mzinda kuja.

< 1 Књига Самуилова 20 >