< 1 Књига о царевима 3 >
1 А Соломун се опријатељи с фараоном, царем мисирским, и ожени се кћерју фараоновом, и доведе је у град Давидов докле не доврши свој дом и дом Господњи и зид око Јерусалима.
Solomoni anachita ubale ndi Farao mfumu ya ku Igupto ndipo anakwatira mwana wake wamkazi. Mkaziyo anabwera naye mu Mzinda wa Davide mpaka anatsiriza kumanga nyumba yaufumu ndi Nyumba ya Yehova ndiponso khoma lozungulira Yerusalemu.
2 Али народ приношаше жртве на висинама; јер још не беше сазидан дом имену Господњем до тада.
Koma anthu ankaperekabe nsembe ku malo achipembedzo osiyanasiyana chifukwa chakuti mpaka pa nthawi imeneyo Dzina la Yehova anali asanalimangire nyumba.
3 А Соломун љубљаше Господа ходећи по уредбама оца свог Давида, само што на висинама приношаше жртве и кађаше.
Solomoni anaonetsa chikondi chake pa Yehova poyenda motsatira malamulo a abambo ake Davide, kupatula kuti ankapereka nsembe ndi kufukiza lubani ku malo osiyanasiyana achipembedzo.
4 Зато отиде цар у Гаваон да онде принесе жртву, јер то беше велика висина; и Соломун принесе хиљаду жртава паљеница на оном олтару.
Mfumu inapita ku Gibiyoni kukapereka nsembe popeza kumeneko ndiye kunali malo oposa malo ofunika kwambiri pachipembedzo. Kumeneko Solomoni anapereka nsembe zopsereza 1,000 pa guwa lansembe.
5 И јави се Господ Соломуну у Гаваону ноћу у сну, и рече Бог: Ишти шта хоћеш да ти дам.
Ku Gibiyoniko Yehova anaonekera kwa Solomoni mʼmaloto usiku, ndipo Mulungu anati, “Pempha chilichonse chimene ukufuna ndipo ndidzakupatsa.”
6 А Соломун рече: Ти си учинио велику милост слузи свом Давиду оцу мом, као што је ходио пред Тобом верно и праведно и с правим срцем према Теби; и сачувао си му ову велику милост, те му дао сина да седи на престолу његовом, као што се види данас.
Solomoni anayankha kuti, “Inu munaonetsa kukoma mtima kwanu kwakukulu kwa kapolo wanu, abambo anga Davide, chifukwa anali wokhulupirika pamaso panu, wolungama mtima ndiponso wa mtima wangwiro. Inu mukupitirizabe kukoma mtima kwanu kwakukulu kwa iye ndipo mwamupatsa mwana kuti akhale pa mpando wake waufumu lero lino.
7 И тако Господе Боже мој, Ти си поставио слугу свог царем на место Давида оца мог, а ја сам млад, нити знам полазити ни долазити.
“Tsopano Inu Yehova Mulungu wanga, mtumiki wanune mwandiyika kukhala mfumu mʼmalo mwa abambo anga Davide. Komatu ndine mwana wamngʼono ndipo sindidziwa kagwiridwe kake ka ntchito yangayi.
8 И Твој је слуга међу народом Твојим, који си изабрао, народом великим, који се не може избројати ни прорачунати од множине.
Mtumiki wanu ali pakati pa anthu amene munawasankha, mtundu waukulu, anthu ochuluka kwambiri osatheka kuwawerenga.
9 Дај дакле слузи свом срце разумно да може судити народу Твом и распознавати добро и зло. Јер ко може судити народу Твом тако великом?
Choncho mupatseni mtumiki wanu nzeru zolamulira anthu anu ndi kuti azitha kusiyanitsa pakati pa chabwino ndi choyipa. Pakuti ndani amene angathe kulamulira anthu anu ochulukawa?”
10 И би мило Господу што Соломун то заиска.
Ambuye anakondwera kuti Solomoni anapempha zimenezi.
11 И рече му Бог: Кад то иштеш, а не иштеш дуг живот нити иштеш благо нити иштеш душе непријатеља својих него иштеш разум да умеш судити;
Tsono Mulungu anati kwa Solomoni, “Popeza wapempha zinthu zimenezi osati moyo wautali kapena chuma chako kapena imfa ya adani ako koma nzeru zolamulira anthu mwachilungamo,
12 Ево учиних по твојим речима; ево ти дајем срце мудро и разумно да таквог какав си ти ни пре тебе није било нити ће после тебе настати такав какав си ти.
Ine ndidzakuchitira zimene wapempha. Ndidzakupatsa mtima wanzeru ndi wozindikira zinthu, kotero kuti sipanakhalepo wina wofanana nawe ndipo sipadzapezekanso wina wonga iwe pambuyo pako.
13 А сврх тога дајем ти и шта ниси искао, и благо и славу, да таквог какав ћеш ти бити неће бити међу царевима свега века твог.
Kuwonjeza apo, ndidzakupatsa zimene sunazipemphe: chuma ndi ulemu, kotero kuti pa masiku onse a moyo wako sipadzakhala mfumu yofanana nawe.
14 И ако узидеш мојим путевима држећи уредбе моје и заповести моје, као што је ишао Давид отац твој, продужићу дане твоје.
Ndipo ngati udzayenda mʼnjira zanga ndi kumvera malamulo anga ndiponso malangizo anga monga abambo ako Davide anachitira, ndidzakupatsa moyo wautali.”
15 Тада се пробуди Соломун, и гле, оно беше сан. И дође у Јерусалим, и ставши пред ковчег завета Господњег принесе жртве паљенице и жртве захвалне, и почасти све слуге своје.
Kotero Solomoni anadzuka ndipo anazindikira kuti anali maloto. Iye anabwerera ku Yerusalemu nakayimirira patsogolo pa Bokosi la Chipangano la Ambuye ndipo anapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Kenaka anakonzera phwando atumiki ake onse.
16 Тада дођоше две жене курве к цару, и стадоше пред њим.
Nthawi ina amayi awiri adama anabwera kwa mfumu ndipo anayima pamaso pake.
17 И рече једна жена: Ах, господару; ја и ова жена седимо у једној кући, и породих се код ње у истој кући.
Mmodzi mwa amayiwo anati, “Mbuye wanga, mayi uyu ndi ine timakhala nyumba imodzi. Ine ndinabala mwana tili limodzi ndi mnzangayu.
18 А трећи дан после мог порођаја породи се и ова жена, и бејасмо заједно и не беше нико други с нама у кући, само нас две бејасмо у кући.
Tsiku lachitatu ine nditabala mwana, mnzangayunso anabereka mwana wake. Tinalipo awiriwiri mʼnyumbamo ndipo munalibe wina aliyense.
19 И умре син ове жене ноћас, јер она леже на њ.
“Nthawi ya usiku mwana wa mnzangayu anafa chifukwa anamugonera.
20 Па уставши у по ноћи узе сина мог искрај мене, кад слушкиња твоја спаваше, и стави га себи у наручје, а сина свог мртвог стави мени у наручје.
Tsono iyeyu anadzuka pakati pa usiku, natenga mwana wanga ku mimba kwanga pamene ine mdzakazi wanu ndinali mʼtulo. Anamuyika mwanayo ku mimba kwake ndi kuyika mwana wake wakufayo ku mimba kwanga.
21 А кад устах ујутру да подојим сина свог, а то мртав; али кад разгледах ујутру, а то, не беше мој син, ког ја родих.
Mmawa nditadzuka kuti ndiyamwitse mwana wanga ndinapeza kuti ndi wakufa! Koma kutacha nditamuyangʼanitsitsa ndinaona kuti si mwana amene ine ndinabala.”
22 Тада рече друга жена: Није тако; него је мој син овај живи, а твој је син онај мртви. Али она рече: Није тако, него је твој син онај мртви, а мој је син овај живи. Тако говораху пред царем.
Koma mayi winayo anati, “Ayi! Mwana wamoyoyu ndi wanga, mwana wakufayu ndi wako.” Koma mayi woyambayo analimbikira kuti. “Ayi! Mwana wakufayu ndi wako; wamoyoyu ndi wanga.” Motero akaziwa anatsutsana pamaso pa mfumu.
23 А цар рече: Ова каже: Овај је живи мој син, а твој је син овај мртви; а она каже: Није тако, него је твој син онај мртви, а мој је син овај живи.
Pamenepo mfumu inati, “Wina akuti, ‘Mwana wanga ndi wamoyoyu ndipo mwana wako ndi wakufayu,’ pamene winanso akuti, ‘Ayi! Mwana wako ndi wakufayu wanga ndi wamoyoyu.’”
24 И рече цар: Дајте ми мач. И донесоше мач пред цара.
Pamenepo mfumu inati, “Patseni lupanga.” Ndipo anabwera nalo lupanga kwa mfumu.
25 Тада рече цар: Расеците живо дете на двоје, и подајте половину једној и половину другој.
Tsono mfumu inagamula kuti, “Muduleni pakati mwana wamoyoyu ndipo wina mumupatse gawo limodzi, gawo linalo mumupatse winayo.”
26 Тада жена које син беше живи рече цару, јер јој се усколеба утроба за сином: Ах, господару, подајте њој дете живо, а немојте га убијати. А она рече: Нека не буде ни мени ни теби, расеците га.
Mayi amene mwana wake anali moyo anagwidwa ndi chisoni chifukwa cha mwana wakeyo ndipo anawuza mfumu kuti, “Chonde mbuye wanga, mupatseni mnzangayu mwana wamoyoyu! Musamuphe!” Koma winayo anati, “Ayi, asandipatse ine kapena iwe. Muduleni pakati!”
27 Тада одговори цар и рече: Подајте оној живо дете, немојте га убити, она му је мати.
Choncho mfumu inagamula kuti, “Perekani mwana wamoyoyu kwa mayi woyambayu. Musamuphe, iyeyu ndiye mayi wake wa mwanayu.”
28 И сав Израиљ чу суд који изрече цар, и побојаше се цара; јер видеше да је у њему мудрост Божја да суди.
Pamene Aisraeli onse anamva za chigamulo chimene mfumu inapereka, anaopa mfumuyo kwambiri, chifukwa anaona kuti mfumu inali ndi nzeru zochokera kwa Mulungu zoweruzira mwachilungamo.