< 1 Књига о царевима 11 >
1 Али цар Соломун љубљаше многе жене туђинке осим кћери Фараонове, Моавке, Амонке, Едомке, Сидонке и Хетејке,
Komatu Mfumu Solomoni anakonda akazi ambiri achilendo ndipo kuwonjezera pa mwana wamkazi wa Farao, analinso ndi akazi a mitundu iyi: Amowabu, Aamoni, Aedomu, Asidoni, ndi Ahiti.
2 Од ових народа за које беше рекао Господ синовима Израиљевим: Не идите к њима и они да не долазе к вама, јер ће занети срце ваше за својим боговима. За њих приону Соломун љубећи их.
Akazi amenewa anali ochokera ku mitundu ija imene Yehova anawuza Aisraeli kuti, “Simuyenera kudzakwatirana nawo amenewa, chifukwa ndithu, amenewa adzatembenuza mitima yanu kuti mutsatire milungu yawo.” Komabe Solomoni anawakonda kwambiri akazi amenewa.
3 Те имаше жена царица седам стотина, и три стотина иноча; и жене његове занесоше срце његово.
Iye anali ndi akazi 700 ochokera ku mabanja achifumu ndi azikazi 300 ndipo akaziwo anamusocheretsa.
4 И кад остаре Соломун, жене занесоше срце његово за туђим боговима; и срце његово не би цело према Господу Богу његовом као што је било срце Давида, оца његовог.
Solomoni atakalamba, akazi akewo anakopa mtima wake kuti atsatire milungu ina, ndipo sanatsatire Yehova Mulungu wake ndi mtima wodzipereka, monga unalili mtima wa Davide abambo ake.
5 И Соломун хођаше за Астаротом, богињом сидонском, и за Мелхомом, гадом амонским.
Pakuti iye ankapembedza Asitoreti, mulungu wamkazi wa Asidoni, ndiponso Moleki mulungu wonyansa wa Aamoni.
6 И чињаше Соломун шта беше зло пред Господом, и не хођаше сасвим за Господом као Давид, отац његов.
Kotero Solomoni anachita zoyipa pamaso pa Yehova. Sanatsatire Yehova kwathunthu monga anachitira Davide abambo ake.
7 Тада сагради Соломун висину Хемосу, гаду моавском, на гори према Јерусалиму, и Молоху гаду амонском.
Pa phiri la kummawa kwa Yerusalemu, anamanga malo opembedzerapo Kemosi, mulungu wonyansa wa Mowabu, ndiponso malo a Moleki, mulungu wonyansa wa Aamoni.
8 Тако учини свим женама туђинкама, те кађаху и приношаху жртве својим боговима.
Iye anamangiranso malo oterewa akazi ake onse achilendo, amene amafukiza lubani ndi kumapereka nsembe kwa milungu yawo.
9 А Господ се разгневи на Соломуна што се одврати срце његово од Господа Бога Израиљевог, који му се беше јавио два пута,
Choncho Yehova anakwiyira Solomoni chifukwa mtima wake unatembenuka kuchoka kwa Yehova Mulungu wa Israeli, amene anamuonekera kawiri konse.
10 И беше му заповедио да не иде за другим боговима, а он не одржа шта му Господ заповеди.
Ngakhale kuti Yehova anamuletsa Solomoni kutsatira milungu ina, iyeyo sanamvere lamulo la Yehova.
11 И рече Господ Соломуну: Што се то нађе на теби, и ниси држао завет мој ни уредбе моје, које сам ти заповедио, зато ћу отргнути од тебе царство и даћу га слузи твом.
Pamenepo Yehova anati kwa Solomoni, “Popeza mtima wako ndi wotere ndipo sunasunge pangano langa ndi malamulo anga amene ndinakuwuza, ndithudi, Ine ndidzawugawa ufumuwu kuwuchotsa kwa iwe ndi kuwupereka kwa mmodzi mwa atumiki ako.
12 Али за твог века нећу то учинити ради Давида оца твог; него ћу га отргнути из руке сина твог.
Koma chifukwa cha Davide abambo ako, sindidzachita zimenezi iwe uli moyo. Ndidzawugawa mʼdzanja la mwana wako.
13 Али нећу отргнути сво царство; једно ћу племе дати сину твом ради Давида слуге свог и ради Јерусалима, који изабрах.
Komabe sindidzamulanda ufumu wonse, koma ndidzamusiyira fuko limodzi chifukwa cha mtumiki wanga Davide ndiponso chifukwa cha Yerusalemu, mzinda umene ndinawusankha.”
14 И подиже Господ противника Соломуну, Адада Идумејца, који беше од царског рода у Идумеји.
Ndipo Yehova anamuutsira Solomoni mdani, Hadadi Mwedomu, wochokera ku banja laufumu ku Edomu.
15 Јер кад Давид беше у Идумеји и Јоав војвода дође да покопа побијене, поби све мушкиње у Идумеји.
Kale pamene Davide ankachita nkhondo ndi Aedomu, Yowabu mkulu wa ankhondo, amene anapita kukakwirira Aisraeli akufa, anakantha amuna onse ku Edomu.
16 Јер Јоав оста онде шест месеци са свим Израиљем докле не поби све мушкиње у Идумеји.
Yowabu ndi Aisraeli onse anakhala kumeneko miyezi isanu ndi umodzi mpaka anawononga amuna onse a ku Edomu.
17 Тада утече Адад с неколико Идумејаца, слуга оца свог, и отиде у Мисир; а Адад беше тада дете.
Koma Hadadi akanali mwana anathawira ku Igupto pamodzi ndi akuluakulu ena a ku Edomu amene ankatumikira abambo ake.
18 И отишавши из Мадијана дођоше у Фаран; и узевши са собом људи из Фарана дођоше у Мисир к Фараону, цару мисирском, који му даде кућу и одреди му храну, и даде му и земље.
Iwo ananyamuka ku Midiya ndi kupita ku Parani. Ndipo anatenga amuna ena ku Paraniko, napita nawo ku Igupto, kwa Farao mfumu ya Igupto, amene anamupatsa nyumba, malo ndiponso chakudya.
19 И Адад нађе велику милост у Фараона, те га ожени сестром жене своје, сестром царице Тахпенесе.
Farao anamukomera mtima Hadadi ndipo anamupatsa mkazi amene anali mngʼono wake wa Mfumukazi Tahipenesi.
20 И сестра Тахпенесина роди му сина Генувата, ког отхрани Тахпенеса на двору Фараоновом, и беше Генуват на двору Фараоновом међу синовима Фараоновим.
Mngʼono wake wa Tahipenesi anabereka mwana wamwamuna ndipo anamutcha Genubati, amene analeredwa mʼnyumba yaufumu ndi Tahipenesi. Genubatiyo ankakhala limodzi ndi ana a Farao.
21 А кад Адад чу у Мисиру да је Давид починуо код отаца својих и да је умро Јоав војвода, рече Адад Фараону: Пусти ме да идем у своју земљу.
Ali ku Iguptoko, Hadadi anamva kuti Davide ndi Yowabu anamwalira. Pamenepo Hadadi anati kwa Farao, “Loleni ndichoke kuti ndibwerere ku dziko la kwathu.”
22 А Фараон му рече: А шта ти је мало код мене, те хоћеш да идеш у своју земљу? А он рече: Ништа; али ме пусти.
Farao anafunsa kuti, “Kodi ukusowa chiyani kuno kuti ufune kubwerera ku dziko la kwanu?” Hadadi anayankha kuti, “Palibe chimene ndikusowa, koma loleni kuti ndichoke!”
23 Подиже му Бог још једног противника, Резона сина Елијадиног, који беше побегао од господара свог Адад-Езера, цара совског.
Ndipo Mulungu anawutsira Solomoni mdani wina, Rezoni mwana wa Eliada, amene anali atathawa mbuye wake, Hadadezeri mfumu ya ku Zoba.
24 И скупивши к себи људе поста старешина од чете кад их Давид уби; потом отишавши у Дамаск осташе онде и овладаше Дамаском.
Iye anasonkhanitsa anthu ndipo anali mtsogoleri wa anthu owukira pamene Davide anapha ankhondo a ku Zoba. Anthu owukirawa anapita ku Damasiko, nakakhala kumeneko ndi kuyamba kulamulira.
25 И беше противник Израиљев свега века Соломуновог, и то осим зла које чињаше Адад; и мржаше на Израиља царујући у Сирији.
Rezoni anali mdani wa Israeli pa masiku onse a Solomoni, kuwonjezera pa mavuto amene ankabweretsa Hadadi. Kotero Rezoni ankalamulira ku Aramu ndipo ankadana ndi Israeli.
26 И Јеровоам син Наватов, Ефраћанин из Сариде, чија мати беше по имену Серуја жена удовица, слуга Соломунов, подиже се на цара.
Yeroboamu, mwana wa Nebati anawukiranso mfumu. Iye anali mmodzi mwa akuluakulu a Solomoni wa fuko la Efereimu, wa ku Zeredi, ndipo amayi ake anali Zeruya, mkazi wamasiye.
27 А ово би узрок зашто се подиже на цара: Соломун грађаше Милон и зазиђиваше пролом града Давида, оца свог;
Nkhani ya kuwukira kwa Yeroboamu inali yotere: Solomoni anamanga malo a chitetezo a Milo ndipo anakonza khoma logumuka la mzinda wa Davide, abambo ake.
28 А Јеровоам беше крепак и храбар; зато видећи Соломун младића да настаје за послом постави га над свим поданицима дома Јосифовог.
Tsono Yeroboamu anali munthu wamphamvu kwambiri ndipo Solomoni ataona kuti mnyamatayo amadziwa kugwira ntchito bwino, anamuyika kukhala woyangʼanira anthu a ntchito onse a nyumba ya Yosefe.
29 Па у то време кад Јеровоам отиде из Јерусалима, нађе га на путу Ахија Силомљанин, пророк имајући на себи нову хаљину, и беху њих двојица сами у пољу.
Tsiku lina Yeroboamu ali pa ulendo kuchokera ku Yerusalemu, anakumana ndi mneneri Ahiya pa msewu, ndipo Ahiyayo anali atavala mwinjiro watsopano. Awiriwo anali okha kuthengoko,
30 И Ахија узе нову хаљину која беше на њему, и раздре је на дванаест комада.
ndipo Ahiya anagwira mwinjiro watsopano umene anavala ndi kuwungʼamba zidutswa 12.
31 И рече Јеровоаму: Узми десет комада; јер овако вели Господ Бог Израиљев: Ево истргнућу царство из руке Соломунове, и даћу теби десет племена.
Tsono iye anati kwa Yeroboamu, “Tenga zidutswa khumi, pakuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Taona, Ine ndidzachotsa ufumu mʼdzanja la Solomoni ndipo ndidzakupatsa iwe mafuko khumi.
32 Само ће једно племе остати њему ради слуге мог Давида и ради града Јерусалима, који изабрах између свих племена Израиљевих.
Koma chifukwa cha mtumiki wanga Davide ndiponso mzinda wa Yerusalemu, umene ndinawusankha pakati pa mafuko a Israeli, iye adzakhala ndi fuko limodzi lokha.
33 Јер оставише мене и поклонише се Астароти, богињи сидонској и Хемосу богу моавском и Мелхому богу синова Амонових, и не ходише путевима мојим чинећи што је право преда мном, уредбе моје и законе моје, као Давид отац његов.
Ndidzachita zimenezi chifukwa wandisiya Ine ndi kupembedza Asitoreti mulungu wamkazi wa Asidoni, Kemosi mulungu wa Amowabu ndiponso Moleki mulungu wa Aamoni, ndipo sanayende mʼnjira yanga, kapena kusunga mawu anga ndi malamulo anga monga anachitira Davide abambo ake.
34 Али нећу узети царство из руку његових, него ћу га оставити нека влада докле је год жив Давида ради слуге свог, ког изабрах, који је држао заповести моје и уредбе моје.
“‘Koma sindidzalanda ufumu wonse mʼdzanja la Solomoni. Ine ndamuyika kukhala wolamulira masiku onse a moyo wake chifukwa cha mtumiki wanga Davide, amene ndinamusankha ndiponso amene anamvera malamulo anga ndi mawu anga.
35 Него ћу узети царство из руку сина његовог, и даћу теби од њега десет племена.
Ndidzalanda ufumu mʼdzanja la mwana wake ndipo ndidzakupatsa iwe mafuko khumi.
36 А сину ћу његовом дати једно племе да буде видело Давиду слузи мом вазда преда мном у граду Јерусалиму, који изабрах да у њему наместим име своје.
Ndidzapereka fuko limodzi kwa mwana wake ndi cholinga choti Davide mtumiki wanga adzakhale nyale nthawi zonse pamaso panga mu Yerusalemu, mzinda umene ndinawusankha kuyikamo Dzina langa.
37 Тебе ћу, дакле, узети да царујеш над свим шта ти душа жели, и бићеш цар над Израиљем.
Koma kunena za iwe, ndidzakutenga ndipo udzalamulira chilichonse chimene mtima wako ukukhumba; udzakhala mfumu ya Israeli.
38 И ако узаслушаш све што ти заповедим, и узидеш мојим путевима и ушчиниш што је право преда мном, држећи уредбе моје и заповести моје, као што је чинио Давид слуга мој, бићу с тобом и сазидаћу ти тврд дом, као што сам сазидао Давиду, и даћу ти Израиља.
Ngati udzamvera zonse zimene ndidzakulamula ndi kuyenda mʼnjira yanga ndi kuchita zabwino pamaso panga, posunga malamulo anga ndi mawu anga monga anachitira Davide mtumiki wanga, Ine ndidzakhala nawe. Ndidzakupatsa ufumu umene udzakhala wokhazikika monga ndinamupatsira Davide, ndipo Ine ndidzakupatsa Israeli.
39 И мучићу семе Давидово зато, али не свагда.
Ine ndidzalanga zidzukulu za Davide chifukwa cha zimenezi, koma osati kwamuyaya.’”
40 Зато тражаше Соломун да убије Јеровоама; али се Јеровоам подиже и побеже у Мисир к Сисаку, цару мисирском, и би у Мисиру докле не умре Соломун.
Solomoni anafunitsitsa kupha Yeroboamu, koma Yeroboamu anathawira ku Igupto, kwa Sisaki mfumu ya Igupto ndipo anakhala kumeneko mpaka Solomoni atamwalira.
41 А остала дела Соломунова и шта је год чинио, и мудрост његова, није ли то записано у књизи дела Соломунових?
Ntchito zina za Solomoni, zonse zomwe anachita komanso za nzeru zake, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya Solomoni?
42 А царова Соломун у Јерусалиму над свим Израиљем четрдесет година.
Solomoni analamulira Aisraeli onse mu Yerusalemu kwa zaka makumi anayi.
43 И почину Соломун код отаца својих, и би погребен у граду Давида, оца свог; а Ровоам, син његов, зацари се на његово место.
Ndipo anagona ndi makolo ake nayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide abambo ake. Ndipo Rehobowamu mwana wake analowa ufumu mʼmalo ake.