< 1 Књига дневника 18 >
1 А после тога поби Давид Филистеје и покори их, и узе Гат и села његова из руку филистејских.
Patapita nthawi, Davide anagonjetsa Afilisti ndipo anakhala pansi pa ulamuliro wake. Iye analanda Gati ndi midzi yake yozungulira mʼmanja mwa Afilistiwo.
2 Поби и Моавце, и посташе Моавци слуге Давидове и плаћаше му данак.
Davide anagonjetsanso Amowabu, nakhala pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho kwa iye.
3 Разби Давид и Адад-Езера цара совског у Емату изашав да рашири власт своју до реке Ефрата.
Komanso Davide anagonjetsa Hadadezeri mfumu ya Zoba, mpaka ku Hamati, pamene anapita kukakhazikitsa ulamuliro wake mʼmbali mwa mtsinje wa Yufurate.
4 И узе му Давид хиљаду кола и седам хиљада коњика и двадесет хиљада пешака, и подреза Давид жиле свим коњима колским, само остави за сто кола.
Davide analanda magaleta 1,000, anthu okwera magaleta 7,000 pamodzi ndi asilikali oyenda pansi 20,000. Iye anadula mitsempha ya akavalo onse okoka magaleta, koma anasiyapo akavalo 100 okha.
5 А беху дошли Сирци из Дамаска у помоћ Адад-Езеру цару совском, и Давид поби двадесет и две хиљаде Сираца.
Aramu wa ku Damasiko atabwera kudzathandiza Hadadezeri mfumu ya ku Zoba, Davide anakantha asilikali 22,000.
6 И намести Давид војску у Сирији што је под Дамаском, и Сирци посташе слуге Давидове плаћајући му данак. И Господ чуваше Давида куда год иђаше.
Iye anakhazikitsa maboma mu ufumu wa Aramu wa ku Damasiko, ndipo Aaramu anakhala pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho. Yehova ankamupatsa chipambano Davide kulikonse kumene ankapita.
7 И Давид узе златне штитове које имаху слуге Адад-Езерове, и донесе их у Јерусалим.
Davide anatenga zishango zagolide zimene ankanyamula akuluakulu ankhondo a Hadadezeri ndi kubwera nazo ku Yerusalemu.
8 И из Тивата и из Хуна градова Адад-Езерових однесе Давид силну бронзу, од које Соломун начини море бронзано и ступове и посуђе бронзано.
Kuchokera ku Teba ndi Kuni, mizinda ya Hadadezeri, Davide anatengako mkuwa wambiri umene Solomoni anapangira chimbiya, zipilala ndi zida zosiyanasiyana zamkuwa.
9 А кад ћу Тоја цар ематски да је Давид побио сву војску Адад-Езера, цара совског,
Tou, mfumu ya Hamati atamva kuti Davide wagonjetsa gulu lonse lankhondo la Hadadezeri mfumu ya Zoba,
10 Посла Адорама, сина свог к цару Давиду да га поздрави и да му честита што је војевао на Адад-Езера и убио га, јер Тоја имаше рат са Адад-Езером и свакојаких заклада златних и сребрних и бронзаних.
anatumiza mwana wake Hadoramu kwa mfumu Davide kukamulonjera ndi kukamuyamikira chifukwa cha kupambana kwake pa nkhondo yake ndi Hadadezeriyo, amene analinso pa nkhondo ndi Tou. Hadoramu anabweretsa ziwiya zosiyanasiyana zagolide, zasiliva ndi zamkuwa.
11 Па и то цар Давид посвети са сребром и златом што беше узео од свих народа, од Едомаца и од Моаваца и од синова Амонових и од Филистеја и од Амалика.
Mfumu Davide inapereka zinthu zimenezi kwa Yehova, monga anachitira ndi siliva ndi golide zochokera ku mayiko ena onse monga Edomu ndi Mowabu, Aamoni ndi Afilisti, ndi Aamaleki.
12 И Ависај син Серујин поби осамнаест хиљада Идумејаца у сланој долини.
Abisai mwana wa Zeruya anakantha Aedomu 18,000 mu Chigwa cha Mchere.
13 И намести војску по Идумеји, и сви Идумејци посташе слуге Давидове. И Господ чуваше Давида куда год иђаше.
Iye anayika maboma ku Edomu, ndipo Aedomu onse anakhala pansi pa Davide. Yehova ankapambanitsa Davide kulikonse kumene ankapita.
14 Тако царова Давид над свим Израиљем судећи и дајући правду свему народу свом.
Davide analamulira dziko lonse la Israeli ndipo ankachita zonse mwachilungamo ndi molondola pamaso pa anthu ake onse.
15 И Јоав, син Серујин беше над војском, а Јосафат син Ахилудов паметар,
Yowabu, mwana wa Zeruya anali mkulu wa ankhondo; Yehosafati mwana wa Ahiludi anali mlembi wa zochitika;
16 А Садок син Ахитовов и Авимелех син Авијатаров свештеници, а Суса писар,
Zadoki, mwana wa Ahitubi ndi Ahimeleki mwana wa Abiatara anali ansembe; Savisa anali mlembi;
17 А Венаја, син Јодајев беше над Херетејима и Фелетејима, а синови Давидови први до цара.
Benaya mwana wa Yehoyada anali mtsogoleri wa Akereti ndi Apeleti, ndipo ana a Davide anali alangizi a mfumu.