< Psalmi 72 >
1 Bože, daj caru sud svoj, i pravdu svoju sinu carevu:
Salimo la Solomoni. Patsani mwana wa mfumu nzeru zanu zoweruzira mwa chilungamo, Inu Mulungu mupatseni mwana wa mfumu chilungamo chanu.
2 On æe suditi narodu tvojemu po pravdi, i nevoljnicima tvojim po pravici.
Iye adzaweruza anthu anu mwachilungamo, anthu anu ozunzika mosakondera.
3 Rodiæe narodu gore mirom, i humovi pravdom.
Mapiri adzabweretsa chuma kwa anthu anu, timapiri tidzabweretsa zipatso zachilungamo.
4 On æe suditi nevoljnima u narodu, pomoæi æe sinovima ništega, i nasilnika æe oboriti,
Iye adzateteza ozunzika pakati pa anthu ndi kupulumutsa ana a anthu osowa; adzaphwanya ozunza anzawo.
5 Bojaæe se tebe dok je sunca i mjeseca, od koljena do koljena.
Adzakhala ndi moyo pa mibado yonse, nthawi zonse pamene dzuwa ndi mwezi zikuwala.
6 Siæi æe kao dažd na pokošenu livadu, kao kaplje koje porašaju zemlju.
Iye adzakhala kugwa kwa mvula pa minda yolimidwa ngati mivumbi yothirira dziko lapansi.
7 Procvjetaæe u dane njegove pravednik i svuda mir dokle teèe mjeseca.
Mʼmasiku a munthu wolungama adzakhazikika; chuma chidzachuluka mpaka mwezi utaleka kuwala.
8 Vladaæe od mora do mora, i od rijeke do krajeva zemaljskih.
Iye adzalamulira kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina ndiponso kuchokera ku mtsinje mpaka ku malekezero a dziko lapansi.
9 Pred njim æe popadati divljaci, i neprijatelji njegovi prah æe lizati.
Mafuko a mʼchipululu adzawerama pamaso pake ndipo adani ake adzanyambita fumbi.
10 Carevi Tarsiski i ostrvljani donijeæe dare, carevi Šavski i Savski daæe danak.
Mafumu a ku Tarisisi ndi a ku zilumba zakutali adzabweretsa mitulo kwa iye, mafumu a ku Seba ndi Seba adzapereka mphatso kwa iyeyo.
11 Klanjaæe mu se svi carevi, svi narodi biæe mu pokorni.
Mafumu onse adzamuweramira ndipo mitundu yonse idzamutumikira.
12 Jer æe izbaviti ubogoga koji cvili i nevoljnoga koji nema pomoænika.
Pakuti iye adzawombola wosowa amene akulira, wozunzika amene alibe wina womuthandiza.
13 Biæe milostiv ništemu i ubogom, i duše æe jadnima spasti.
Iye adzachitira chifundo anthu ofowoka ndi anthu osowa ndi kupulumutsa osowa ku imfa.
14 Od prijevare i nasilja iskupiæe duše njihove, i skupa æe biti krv njihova pred oèima njegovima.
Iye adzalanditsa iwo ku mazunzo ndi chiwawa pakuti magazi awo ndi amtengo wapatali pamaso pake.
15 Oni æe dobro živjeti, i donijeæe mu zlato iz Šave; i svagda æe se moliti za njega, i svaki æe ga dan blagosiljati.
Iye akhale ndi moyo wautali; golide ochokera ku Seba apatsidwe kwa iye. Anthu amupempherere nthawi zonse ndi kumudalitsa tsiku lonse.
16 Biæe pšenice na zemlji izobila; po vrhovima gorskim lelijaæe se klasje njezino kao Livanska šuma, i po gradovima cvjetaæe ljudi kao trava na zemlji.
Mulole kuti tirigu achuluke mʼdziko lonse; pamwamba pa mapiri pakhale tirigu. Zipatso zake zichuluke ngati za ku Lebanoni; zichuluke ngati udzu wakuthengo
17 Ime æe njegovo biti uvijek; dokle teèe sunca, ime æe njegovo rasti. Blagosloviæe se u njemu, svi æe ga narodi zvati blaženim.
Dzina lake likhazikike kwamuyaya, lipitirire kukhala monga momwe limakhalira dzuwa. Mitundu yonse idzadalitsika kudzera mwa iye ndipo iwo adzamutcha iye wodala.
18 Blagosloven Gospod Bog, Bog Izrailjev, koji jedan èini èudesa!
Matamando akhale kwa Yehova Mulungu, Mulungu wa Israeli amene Iye yekha amachita ntchito zodabwitsa.
19 I blagosloveno slavno ime njegovo uvijek! slave njegove napuniæe se sva zemlja. Amin i amin.
Matamando akhale ku dzina lake laulemerero kwamuyaya dziko lonse lapansi lidzaze ndi ulemerero wake. Ameni ndi Ameni.
20 Svršiše se molitve Davida, sina Jesejeva.
Uku ndiko kumaliza kwa mapemphero a Davide mwana wa Yese.