< Psalmi 37 >

1 Nemoj se žestiti gledajuæi nevaljale, nemoj zavidjeti onima koji èine bezakonje.
Salimo la Davide. Usamavutike chifukwa cha anthu oyipa kapena kuchitira nsanje amene akuchita cholakwa;
2 Jer se kao trava brzo kose, i kao zeleno bilje venu.
pakuti monga udzu iwo adzafota msanga, ngati mbewu zobiriwira adzanyala msanga.
3 Uzdaj se u Gospoda i tvori dobro; živi na zemlji i hrani istinu.
Khulupirira Yehova ndipo uzichita zabwino; khazikika mʼdziko ndi kutsata zokhulupirika.
4 Tješi se Gospodom, i uèiniæe ti što ti srce želi.
Udzikondweretse wekha mwa Yehova ndipo Iye adzakupatsa zokhumba za mtima wako.
5 Predaj Gospodu put svoj, i uzdaj se u njega, on æe uèiniti.
Pereka njira yako kwa Yehova; dalira Iye ndipo Iyeyo adzachita izi:
6 I izvešæe kao vidjelo pravdu tvoju, i pravicu tvoju kao podne.
Iye adzachititsa chilungamo chako kuwala ngati mʼbandakucha, chiweruzo chako ngati dzuwa la masana.
7 Osloni se na Gospoda, i èekaj ga. Nemoj se žestiti gledajuæi koga gdje napreduje na putu svojem, èovjeka, koji radi što namisli.
Khala chete pamaso pa Yehova ndipo umudikire mofatsa; usavutike pamene anthu apambana mʼnjira zawo, pamene iwo achita zinthu zawo zoyipa.
8 Utišaj gnjev, i ostavi jarost; nemoj se dražiti da zlo èiniš.
Pewa kupsa mtima ndipo tembenuka kuchoka ku ukali, usavutike chifukwa zimenezi zimatsogolera ku zoyipa.
9 Jer æe se istrijebiti koji èine zlo, a koji èekaju Gospoda naslijediæe zemlju.
Pakuti anthu oyipa adzachotsedwa, koma iwo amene amayembekeza mwa Yehova adzalandira dziko.
10 Još malo, pa neæe biti bezbožnika; pogledaæeš na mjesto njegovo, a njega nema.
Kwa kanthawi oyipa sadzapezekanso; ngakhale muwafunefune, sadzapezekanso.
11 A smjerni æe naslijediti zemlju, i naslaðivaæe se množinom mira.
Koma ofatsa adzalandira dziko ndipo adzasangalala ndi mtendere waukulu.
12 Zlo misli bezbožnik pravedniku, i škrguæe na nj zubima svojim.
Oyipa amakonza chiwembu kutsutsana ndi olungama ndipo amawakukutira mano;
13 Ali mu se Gospod smije, jer vidi da se primièe dan njegov.
koma Ambuye amaseka oyipa pakuti Iye amadziwa kuti tsiku lawo likubwera.
14 Maè potežu bezbožnici, zapinju luk svoj, da obore ubogoga i ništega i pokolju one koji idu pravim putem.
Oyipa amasolola lupanga ndi kupinda uta kugwetsa osauka ndi osowa, kupha iwo amene njira zawo ndi zolungama.
15 Maè æe njihov udariti u njihovo srce, i lukovi njihovi polomiæe se.
Koma malupanga awo analasa mitima yawo yomwe, ndipo mauta awo anathyoka.
16 Bolje je malo u pravednika nego bogatstvo mnogih bezbožnika.
Zabwino zochepa zimene olungama ali nazo ziposa chuma cha anthu oyipa ambiri;
17 Jer æe se mišice bezbožnicima potrti, a pravednike utvrðuje Gospod.
pakuti mphamvu ya oyipa idzasweka, koma Yehova amasunga olungama.
18 Zna Gospod dane bezazlenima, i dio njihov traje dovijeka.
Masiku a anthu osalakwa amadziwika ndi Yehova, ndipo cholowa chawo chidzakhala mpaka muyaya.
19 Neæe se postidjeti u zlo doba, u dane gladne biæe siti.
Pa nthawi ya mavuto iwo sadzafota; mʼmasiku a njala adzakhala ndi zinthu zambiri.
20 A bezbožnici ginu, i neprijatelji Gospodnji kao ljepota šumska prolaze, kao dim prolaze.
Koma oyipa adzawonongeka; adani a Yehova adzakhala ngati kukongola kwa kuthengo, iwo adzazimirira ngati utsi.
21 Bezbožnik uzaima i ne vraæa, a pravednik poklanja i daje.
Oyipa amabwereka ndipo sabweza koma olungama amapereka mowolowamanja.
22 Jer koje on blagoslovi, oni naslijede zemlju, a koje on prokune, oni se istrijebe.
Iwo amene Yehova amawadalitsa adzalandira dziko, koma amene Iye amawatemberera adzachotsedwa.
23 Gospod utvrðuje korake svakoga èovjeka i mio mu je put njegov.
Ngati Yehova akondwera ndi njira ya munthu, amakhazikitsa mayendedwe ake;
24 Kad posrne da padne, neæe pasti, jer ga Gospod drži za ruku.
ngakhale atapunthwa sadzagwa, pakuti Yehova amamutchinjiriza ndi dzanja lake.
25 Bijah mlad i ostarjeh, i ne vidjeh pravednika ostavljena, ni djece njegove da prose hljeba.
Ine ndinali wamngʼono ndipo tsopano ndakalamba koma sindinaonepo olungama akusiyidwa kapena ana awo akupempha chakudya.
26 Svaki dan poklanja i daje u zajam, i na natražju je njegovu blagoslov.
Iwo ndi owolowamanja nthawi zonse ndipo amabwereketsa mwaufulu; ana awo adzadalitsika.
27 Uklanjaj se oda zla, i èini dobro, i živi dovijeka.
Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; pamenepo udzakhazikika mʼdziko kwamuyaya.
28 Jer Gospod ljubi pravedni sud, i ne ostavlja svetaca svojijeh; uvijek se oni èuvaju; a pleme æe se bezbožnièko istrijebiti.
Pakuti Yehova amakonda wolungama ndipo sadzasiya okhulupirika ake. Iwo adzatetezedwa kwamuyaya, koma zidzukulu za oyipa zidzachotsedwa;
29 Pravednici æe naslijediti zemlju, i živjeæe na njoj dovijeka.
olungama adzalandira dziko ndipo adzakhazikikamo kwamuyaya.
30 Usta pravednikova govore mudrost, i jezik njegov kazuje istinu.
Pakamwa pa munthu wolungama pamayankhula za nzeru, ndipo lilime lake limayankhula zolungama.
31 Zakon je Boga njegova njemu u srcu, stopala se njegova ne spotièu.
Lamulo la Mulungu wake lili mu mtima mwake; mapazi ake saterereka.
32 Bezbožnik vreba pravednika, i traži da ga ubije;
Oyipa amabisala kudikira olungama; kufunafuna miyoyo yawoyo;
33 Ali ga Gospod neæe pustiti u ruke njegove, niti æe dati da ga okrive kad se stanu suditi.
koma Yehova sadzawasiya pansi pa mphamvu yawo kapena kuti atsutsidwe pamene abweretsedwa pa milandu.
34 Èekaj Gospoda i drži se puta njegova, i on æe te postaviti da vladaš zemljom; vidjeæeš kako æe se istrijebiti bezbožnici.
Khulupirira Yehova, ndipo sunga njira yake; Iye adzakukweza ndipo udzalandira dziko kuti likhale lako; udzaona anthu oyipa akuwonongeka.
35 Vidjeh bezbožnika strašna koji se raširivaše kao granato drvo;
Ine ndinaona munthu woyipa ndi munthu wopanda chifundo akupeza bwino ngati mtengo wobiriwira pa nthaka ya makolo ake.
36 Ali proðe, i evo nema ga; tražim ga i ne nahodim.
Koma sanachedwe kumwalira ndipo sanaonekenso; ngakhale ndinamuyangʼanayangʼana, sanapezekenso.
37 Hrani èistotu i pazi pravdu, jer æe u èovjeka mirna ostati natražje.
Ganizira za munthu wosalakwa, yangʼanitsitsa munthu wolungama; udzaona kuti ali ndi tsogolo labwino ndipo ali ndi zidzukulu zambiri.
38 A bezakonika æe nestati sasvijem; natražje æe se bezbožnièko zatrti.
Koma anthu ochimwa adzawonongeka; iwowo pamodzi ndi zidzukulu zawo zomwe.
39 Od Gospoda je spasenje pravednicima; on je krjepost njihova u nevolji.
Chipulumutso cha olungama chimachokera kwa Yehova; Iye ndiye linga lawo pa nthawi ya masautso.
40 Gospod æe im pomoæi, i izbaviæe ih; izbaviæe ih od bezbožnika, i saèuvaæe ih, jer se u njega uzdaju.
Yehova amawathandiza ndi kuwalanditsa; Iye amawalanditsa kwa oyipa ndi kuwapulumutsa, pakuti amathawira kwa Iye.

< Psalmi 37 >