< Psalmi 113 >

1 Hvalite, sluge Gospodnje, hvalite ime Gospodnje,
Tamandani Yehova. Mutamandeni, inu atumiki a Yehova, tamandani dzina la Yehova.
2 Da bude ime Gospodnje blagosloveno otsad i dovijeka.
Yehova atamandidwe, kuyambira tsopano mpaka muyaya.
3 Od istoka sunèanoga do zapada da se slavi ime Gospodnje.
Kuyambira ku matulukiro a dzuwa mpaka ku malowero ake, dzina la Yehova liyenera kutamandidwa.
4 Uzvišen je nad svima narodima Gospod; svrh nebesa je slava njegova.
Yehova wakwezeka pa anthu a mitundu yonse, ulemerero wake ndi woposa mayiko akumwamba.
5 Ko je kao Gospod, Bog naš, koji sjedi na visini;
Ndani wofanana ndi Yehova Mulungu wathu, Iye amene amakhala mwaufumu mmwamba?
6 Koji se sagiba da vidi što je na nebesima i na zemlji;
amene amawerama pansi kuyangʼana miyamba ndi dziko lapansi?
7 Koji iz praha podiže ubogoga, i iz kala uzvišuje ništega;
Iye amakweza munthu wosauka kuchoka pa fumbi ndi kutukula munthu wosowa kuchoka pa dzala;
8 I posaðuje ga s knezovima, s knezovima u narodu njegovu;
amawakhazika pamodzi ndi mafumu, pamodzi ndi mafumu a anthu ake.
9 Od nerotkinje naseljava kuæu, uèinivši je radosnom majkom sinovima. Aliluja!
Amakhazikitsa mayi wosabereka mʼnyumba yake monga mayi wa ana wosangalala. Tamandani Yehova.

< Psalmi 113 >