< Brojevi 1 >
1 Još reèe Gospod Mojsiju u pustinji Sinajskoj u šatoru od sastanka prvi dan drugoga mjeseca druge godine po izlasku njihovu iz zemlje Misirske, govoreæi:
Yehova anayankhula ndi Mose mʼchipululu cha Sinai, mu tenti ya msonkhano, pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, mʼchaka chachiwiri atatuluka mu Igupto, kuti,
2 Izbrojte sav zbor sinova Izrailjevih po porodicama njihovijem i po domovima otaca njihovijeh i po imenima njihovijem, sve muškinje, glavu po glavu,
“Werengani Aisraeli onse mʼmafuko awo ndi mʼmabanja awo, lemba dzina la munthu wamwamuna aliyense, mmodzimmodzi.
3 Od dvadeset godina i više, sve koji mogu iæi na vojsku u Izrailju, izbrojte ih po èetama njihovijem ti i Aron;
Iwe ndi Aaroni mwawerenge mwa magulu awo mu Israeli, amuna onse a zaka makumi awiri zakubadwa ndi opitirirapo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali.
4 I s vama neka bude po jedan èovjek od svakoga plemena, koji je poglavar u domu otaca svojih.
Munthu mmodzi wochokera ku fuko lililonse yemwe ndi mtsogoleri wa banja lake, ndiye akuthandizeni pa ntchitoyi.
5 A ovo su imena ljudi koji æe biti s vama: od plemena Ruvimova Elisur sin Sedijurov;
Mayina a anthu amene akuthandizeniwo ndi awa: Elizuri mwana wa Sedeuri, kuchokera ku fuko la Rubeni,
6 Od Simeunova Salamilo sin Surisadejev;
Selumieli mwana wa Zurisadai, kuchokera ku fuko la Simeoni,
7 Od Judina Nason sin Aminadavov;
Naasoni mwana wa Aminadabu, kuchokera ku fuko la Yuda,
8 Od Isaharova Natanailo sin Sogarov;
Netanieli mwana wa Zuwara, kuchokera ku fuko la Isakara,
9 Od Zavulonova Elijav sin Helonov;
Eliabu mwana wa Heloni, kuchokera ku fuko la Zebuloni,
10 Od sinova Josifovijeh: od plemena Jefremova Elisama sin Emijudov; od Manasijina Gamalilo sin Fadasurov;
Mwa ana a Yosefe: kuchokera ku fuko la Efereimu, Elisama mwana wa Amihudi; kuchokera ku fuko la Manase, Gamalieli mwana wa Pedazuri;
11 Od Venijaminova Avidan sin Gadeonijev;
Abidani mwana wa Gideoni, kuchokera ku fuko la Benjamini,
12 Od Danova Ahijezer sin Amisadajev;
Ahiyezeri mwana wa Amisadai, kuchokera ku fuko la Dani,
13 Od Asirova Fagailo sin Ehranov;
Pagieli mwana wa Okirani, kuchokera ku fuko la Aseri,
14 Od Gadova Elisaf sin Raguilov;
Eliyasafu mwana wa Deuweli, kuchokera ku fuko la Gadi,
15 Od Neftalimova Ahirej sin Enanov.
Ahira mwana wa Enani, kuchokera ku fuko la Nafutali.”
16 To su koji se sazivahu na zbor, knezovi u plemenima otaca svojih, tisuænici Izrailjevi.
Amenewa ndi anthu amene anasankhidwa kuchokera mʼmagulu mwawo, eni mbumba a mafuko a makolo awo. Iwowa anali atsogoleri a mafuko a Israeli.
17 I uze Mojsije i Aron te ljude, koji biše imenovani.
Mose ndi Aaroni anatenga anthu amene mayina awo anaperekedwa,
18 I sabraše sav zbor prvi dan drugoga mjeseca, i prepisaše ih po porodicama njihovijem i po domovima otaca njihovijeh i po imenima njihovijem od dvadeset godina i više, glavu po glavu.
ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wachiwiri, anasonkhanitsa anthu onse pamodzi. Anthuwo anafotokoza za makolo awo mwa mafuko awo ndi mabanja awo. Ndipo mayina a amuna onse amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo analembedwa, mmodzimmodzi
19 Kako bješe Gospod zapovjedio Mojsiju, tako ih izbroji u pustinji Sinajskoj.
monga momwe Yehova analamulira Mose. Motero iyeyo anawawerenga mʼchipululu cha Sinai:
20 I bješe sinova prvenca Izrailjeva Ruvima, roda njihova po porodicama njihovijem i po domovima otaca njihovijeh, kad se izbroji po imenima s glave na glavu sve muškinje od dvadeset godina i više, što mogaše iæi na vojsku,
Kuchokera mwa ana a Rubeni, mwana wamwamuna woyamba wa Israeli: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali, anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
21 Bješe ih izbrojenijeh od plemena Ruvimova èetrdeset i šest tisuæa i pet stotina.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Rubeni chinali 46,500.
22 Sinova Simeunovijeh, roda njihova po porodicama njihovijem i po domovima otaca njihovijeh, kad se izbroji po imenima s glave na glavu sve muškinje od dvadeset godina i više, što mogaše iæi na vojsku,
Kuchokera mwa zidzukulu za Simeoni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo, mmodzimmodzi monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
23 Bješe ih izbrojenijeh od plemena Simeunova pedeset i devet tisuæa i tri stotine.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Simeoni chinali 59,300.
24 Sinova Gadovijeh, roda njihova po porodicama njihovijem i po domovima otaca njihovijeh, kad se izbrojiše po imenima od dvadeset godina i više svi što mogahu iæi na vojsku,
Kuchokera mwa zidzukulu za Gadi: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
25 Bješe ih izbrojenijeh od plemena Gadova èetrdeset i pet tisuæa, šest stotina i pedeset.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Gadi chinali 45, 650.
26 Sinova Judinijeh, roda njihova po porodicama njihovijem i po domovima otaca njihovijeh, kad se izbrojiše po imenima od dvadeset godina i više svi što mogahu iæi na vojsku,
Kuchokera mwa zidzukulu za Yuda: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
27 Bješe ih izbrojenijeh od plemena Judina sedamdeset i èetiri tisuæe i šest stotina.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Yuda chinali 74, 600.
28 Sinova Isaharovijeh, roda njihova po porodicama njihovijem i po domovima otaca njihovijeh, kad se izbrojiše po imenima od dvadeset godina i više svi što mogahu iæi na vojsku,
Kuchokera mwa zidzukulu za Isakara: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
29 Bješe ih izbrojenijeh od plemena Isaharova pedeset i èetiri tisuæe i èetiri stotine.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Isakara chinali 54,400.
30 Sinova Zavulonovijeh, roda njihova po porodicama njihovijem i po domovima otaca njihovijeh, kad se izbrojiše po imenima od dvadeset godina i više svi što mogahu iæi na vojsku,
Kuchokera mwa zidzukulu za Zebuloni: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
31 Bješe ih izbrojenijeh od plemena Zavulonova pedeset i sedam tisuæa i èetiri stotine.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Zebuloni chinali 57,400.
32 Od sinova Josifovijeh: sinova Jefremovijeh, roda njihova po porodicama njihovijem i po domovima otaca njihovijeh, kad se izbrojiše po imenima od dvadeset godina i više svi što mogahu iæi na vojsku,
Kuchokera mwa ana aamuna a Yosefe: Kuchokera mwa zidzukulu za Efereimu: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
33 Bješe ih izbrojenijeh od plemena Jefremova èetrdeset tisuæa i pet stotina.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Efereimu chinali 40,500.
34 Sinova Manasijinih, roda njihova po porodicama njihovijem i po domovima otaca njihovijeh, kad se izbrojiše po imenima od dvadeset godina i više svi što mogahu iæi na vojsku,
Kuchokera mwa zidzukulu za Manase: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
35 Bješe ih izbrojenijeh od plemena Manasijina trideset i dvije tisuæe i dvjesta.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Manase chinali 32,200.
36 Sinova Venijaminovijeh, roda njihova po porodicama njihovijem i po domovima otaca njihovijeh, kad se izbrojiše po imenima od dvadeset godina i više svi što mogahu iæi na vojsku,
Kuchokera mwa zidzukulu za Benjamini: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
37 Bješe ih izbrojenijeh od plemena Venijaminova trideset i pet tisuæa i èetiri stotine.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Benjamini chinali 35,400.
38 Sinova Danovijeh, roda njihova po porodicama njihovijem i po domovima otaca njihovijeh, kad se izbrojiše po imenima od dvadeset godina i više svi što mogahu iæi na vojsku,
Kuchokera mwa zidzukulu za Dani: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
39 Bješe ih izbrojenijeh od plemena Danova šezdeset i dvije tisuæe i sedam stotina.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Dani chinali 62,700.
40 Sinova Asirovijeh, roda njihova po porodicama njihovijem i po domovima otaca njihovijeh, kad se izbrojiše po imenima od dvadeset godina i više svi što mogahu iæi na vojsku,
Kuchokera mwa zidzukulu za Aseri: Amuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
41 Bješe ih izbrojenijeh od plemena Asirova èetrdeset i jedna tisuæa i pet stotina.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Aseri chinali 41,500.
42 Sinova Neftalimovijeh, roda njihova po porodicama njihovijem i po domovima otaca njihovijeh, kad se izbrojiše po imenima od dvadeset godina i više svi što mogahu iæi na vojsku,
Kuchokera mwa zidzukulu za Nafutali: Aamuna onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali anawalemba mayina awo monga mwa mbiri ya mafuko awo ndi mabanja awo.
43 Bješe ih izbrojenijeh od plemena Neftalimova pedeset i tri tisuæe i èetiri stotine.
Chiwerengero cha anthu ochokera mʼfuko la Nafutali chinali 53,400.
44 Ovo su oni koje Mojsije i Aron izbrojiše s knezovima Izrailjskim, s dvanaest ljudi, koji bijahu po jedan za svaki dom otaca svojih.
Amenewa ndiwo anthu amene Mose ndi Aaroni anawawerenga mothandizidwa ndi atsogoleri khumi ndi awiri a Israeli, aliyense kuyimira fuko lake.
45 I svega bješe sinova Izrailjevijeh izbrojenijeh po domovima otaca svojih od dvadeset godina i više, svijeh što mogahu iæi na vojsku,
Aisraeli onse a zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, omwe akanatha kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli anawawerenga monga mwa mabanja awo.
46 Bješe ih izbrojenijeh šest stotina i tri tisuæe i pet stotina i pedeset.
Chiwerengero cha anthu onse pamodzi chinali 603,550.
47 Ali Leviti po plemenu otaca svojih ne biše brojeni meðu njih.
Koma mabanja a fuko la Levi okha sanawawerenge pamodzi ndi ena.
48 Jer Gospod reèe Mojsiju govoreæi:
Pakuti Yehova anawuza Mose kuti,
49 Plemena Levijeva nemoj brojati, niti broja njihova sastaviti sa sinovima Izrailjevijem.
“Usawerenge fuko la Levi kapena kuliphatikiza mʼkawundula wa Aisraeli.
50 Nego postavi Levite nad šatorom od svjedoèanstva i nad svijem posuðem u njemu i nad svijem što pripada njemu; oni neka nose šator i sve posuðe njegovo, neka služe u njemu, i staju oko šatora.
Koma uyike Aleviwo kuti aziyangʼanira tenti yanga yopatulika, zipangizo zake ndi zonse zili mʼmenemo. Azinyamula tentiyo pamodzi ndi zipangizo zake zonse; azisamalira ndi kumanga misasa mozungulira tentiyo.
51 I kad se šator krene, neka ga slože Leviti; i kad šator stane, onda neka ga razapnu Leviti. A ko bi drugi pristupio, da se pogubi.
Pamene akusamutsa tentiyo, Alevi ndiwo aziyitsitsa, akafuna kuyimanganso, Alevi ndiwo aziyimiritsa. Wina aliyense amene adzayandikire tentiyo adzaphedwa.
52 I sinovi Izrailjevi neka staju svaki u svom okolu i svaki kod svoje zastave po èetama svojim.
Aisraeli azimanga matenti awo mʼmagulumagulu, munthu aliyense ku gulu lake pansi pa mbendera yake.
53 A Leviti neka staju oko šatora od svjedoèanstva, da ne doðe gnjev na zbor sinova Izrailjevijeh; i neka Leviti rade što treba oko šatora od svjedoèanstva.
Alevi nawonso, azimanga matenti awo mozungulira tenti yopatulika kuti chilango chisagwere Aisraeli onse. Ndipo Alevi aziyangʼanira ndi kusamalira tenti yopatulikayo.”
54 I uèiniše sinovi Izrailjevi kako Gospod zapovjedi, sve tako uèiniše.
Choncho Aisraeli anachita monga Yehova analamulira Mose.